< ULukha 23 >

1 Kwasekusukuma ixuku labo lonke, lamusa kuPilatu.
Kenaka gulu lonse la anthuwo linayimirira ndi kumutengera kwa Pilato.
2 Baqala ukummangalela, besithi: Simficile lo eduhisa isizwe, esalela ukuthela kuKesari, esithi nguye onguKristu iNkosi.
Ndipo iwo anayamba kumuneneza nati, “Ife tinapeza munthu uyu akusokoneza anthu a mtundu wathu ndipo amatsutsa zopereka msonkho kwa Kaisara komanso amati ndi Khristu, Mfumu.”
3 UPilatu wasembuza, wathi: Wena uyiNkosi yamaJuda yini? Wasemphendula wathi: Uyatsho wena.
Pamenepo Pilato anamufunsa Yesu kuti, “Kodi Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda?” Yesu anayankha kuti, “Mwatero ndinu.”
4 Wasesithi uPilatu kubapristi abakhulu lemaxukwini: Kangitholi cala kulumuntu.
Kenaka Pilato anawawuza akulu a ansembe ndi gulu la anthu, “Ine sindikumupeza cholakwa munthuyu.”
5 Kodwa baqinisa, besithi: Udunga abantu, efundisa kuyo yonke iJudiya, eqala eGalili kuze kufike lapha.
Koma iwo analimbikirabe kuti, “Iyeyu amasokoneza anthu ku Yudeya konse ndi chiphunzitso chake, Iyeyu anayambira ku Galileya ndipo wayenda mtunda wonse mpaka kuno.”
6 Lapho uPilatu esizwa kuthiwa iGalili wabuza ukuthi lumuntu ungumGalili yini.
Pakumva zimenezi, Pilato anafunsa ngati munthuyo ndi Mgalileya.
7 Kwathi esezwile ukuthi ungowombuso kaHerodi, wamthumela kuHerodi, owayekhona laye eJerusalema ngalezonsuku.
Iye atamva kuti Yesu anali pansi pa ulamuliro wa Herode, anamutumiza kwa Herodeyo, amene pa nthawi imeneyo analinso mu Yerusalemu.
8 Kwathi uHerodi embona uJesu wathokoza kakhulu; ngoba wayekade ethanda ukumbona, ngoba wayezwile okunengi ngaye; wayethemba ukuthi uzabona isibonakaliso esithile sisenziwa nguye.
Herode ataona Yesu, anakondwa kwambiri, chifukwa kwa nthawi yayitali, ankafunitsitsa atamuona. Kuchokera pa zimene anamva za Iye, anayembekezera kuti achita zodabwitsa.
9 Wambuza ngamazwi amanengi; kodwa yena kamphendulanga lutho.
Iye anamufunsa mafunso ambiri, koma Yesu sanayankhe.
10 Abapristi abakhulu lababhali babemi, bemmangalela ngamandla.
Akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, anayimirira pamenepo ndi kumuneneza kwambiri.
11 UHerodi lamabutho akhe bamyangisa, bamklolodela, basebemgqokisa isembatho esikhazimulayo, bambuyisela kuPilatu.
Pamenepo Herode ndi asilikali ake anamuseka ndi kumunyoza Iye. Atamuveka mkanjo wonyezimira, anamutumizanso kwa Pilato.
12 Ngalolosuku uHerodi kanye loPilatu baba ngabangane omunye komunye; ngoba ngaphambi kwalokhu babelobutha phakathi kwabo.
Tsiku limenelo, Herode ndi Pilato anakhala abwenzi. Zisanachitike izi anali adani.
13 UPilatu wasebizela ndawonye abapristi abakhulu lababusi labantu,
Pilato anasonkhanitsa akulu a ansembe, oweruza ndi anthu,
14 wathi kubo: Limlethile kimi lumuntu, ngokungathi ungoduhisa abantu; njalo khangelani, mina ngimhlolile phambi kwenu, kangitholanga cala kulumuntu ngalezozinto elimmangalela ngazo;
ndipo anawawuza kuti, “Munabweretsa munthuyu kwa ine ngati ndiye amawuza anthu kuti awukire. Ine ndamufunsa pamaso panu ndipo sindinapeze chomuyimbira mlandu.
15 hatshi ngitsho loHerodi; ngoba ngilithumeze kuye, njalo khangelani, kakulalutho olufanele ukufa olwenziwe nguye.
Herodenso sanapeze chifukwa pakuti wamutumizanso kwa ife monga mmene mukuoneramu. Iyeyu sanachite chinthu chakuti aphedwe.
16 Ngakho ngizamtshaya ngimkhulule.
Nʼchifukwa chake, ine ndingomulanga, nʼkumumasula.”
17 Kwakufanele ukuthi abakhululele abe munye ngomkhosi.
(Pa nthawi yachikondwerero cha Paska iye ankayenera kumasula munthu mmodzi).
18 Bamemeza bonke kanyekanye besithi: Msuse lo, usikhululele uBarabasi
Onse pamodzi anafuwula kuti, “Muchotseni munthuyu! Timasulireni Baraba!”
19 (owayephoselwe entolongweni ngenxa yomvukela othile owenzeka phakathi komuzi langenxa yokubulala).
(Baraba anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe mu mzinda ndi kupha).
20 Ngakho uPilatu wabuya wakhuluma labo, efuna ukumkhulula uJesu.
Pofuna kumumasula Yesu, Pilato anawadandaulira iwo.
21 Kodwa bamemeza, besithi: Bethela, mbethele!
Koma iwo anapitirirabe kufuwula kuti, “Mpachikeni! Mpachikeni!”
22 Wasesithi kubo ngokwesithathu: Ngoba lo enze bubi bani? Kangitholanga kuye icala afanele ukufa ngalo; ngakho ngizamtshaya ngimkhulule.
Kachitatu anawafunsanso iwo kuti, “Chifukwa chiyani? Kodi munthu uyu wachita choyipa chanji? Ine sindinapeze cholakwa mwa Iye chakuti aphedwe choncho ndingomukwapula ndi kumumasula.”
23 Kodwa baqinisa ngamazwi amakhulu, befuna ukuthi abethelwe; lamazwi abo lawabapristi abakhulu aphumelela.
Koma ndi mawu ofuwulitsa, analimbikirabe kuti Iye apachikidwe, ndipo kufuwulako kunapitirira.
24 UPilatu wasequma ukuthi kwenziwe isicelo sabo.
Choncho Pilato anatsimikiza kuchita zofuna zawozo.
25 Wasebakhululela lowo ababemcelile owayephoselwe entolongweni ngenxa yomvukela lokubulala; kodwa uJesu wamnikela entandweni yabo.
Iye anawamasulira munthu amene anaponyedwa mʼndende chifukwa choyambitsa chipolowe ndi kupha, amene ankamufunayo, ndipo anawapatsa Yesu mwakufuna kwawo.
26 Kwathi sebemqhuba, babamba uSimoni othile umKurene owayevela emaphandleni, bamethesa isiphambano, ukuthi asithwale ngemva kukaJesu.
Ndipo pamene ankapita naye, anagwira Simoni wa ku Kurene, amene ankachokera ku munda, namusenzetsa mtanda namuyendetsa pambuyo pa Yesu.
27 Laselimlandela ixuku elikhulu labantu, labesifazana labo ababekhala bemlilela.
Gulu lalikulu la anthu linamutsata Iye, kuphatikiza amayi amene ankabuma ndi kumulirira.
28 Kodwa uJesu ephendukela kubo wathi: Madodakazi eJerusalema, lingangikhaleli mina, kodwa zikhaleleni lina labantwana benu,
Yesu anatembenuka nati kwa iwo, “Ana aakazi a Yerusalemu, musandilirire Ine; dzililireni nokha ndi ana anu.
29 ngoba khangelani, ziyeza insuku abazakutsho ngazo ukuthi: Zibusisiwe inyumba, lezizalo ezingazalanga, lamabele angamunyisanga.
Pakuti nthawi idzabwera imene inu mudzati, ‘Ndi odala amayi osabereka, mimba zimene sizinabereke ndi mawere amene sanayamwitse!’
30 Khona bezaqalisa ukuthi ezintabeni: Welani phezu kwethu; lemaqaqeni: Sisibekeleni.
Kenaka, “adzawuza mapiri kuti tigwereni ife; zitunda kuti tiphimbeni ife.
31 Ngoba uba besenza lezizinto esihlahleni esimanzi, kuzakwenzakalani kwesomileyo?
Chifukwa ngati anthu akuchita izi pa mtengo wauwisi, chidzachitike nʼchiyani ndi wowuma?”
32 Kwaqhutshwa labanye abenzi bobubi ababili, ukuthi babulawe kanye laye.
Amuna ena awiri, onsewo achifwamba, anatengedwanso pamodzi ndi Yesu kukaphedwa.
33 Sebefikile endaweni ethiwa luKhakhayi, bambethela khona, labenzi bobubi, omunye ngakwesokunene, lomunye ngakwesokhohlo.
Pamene anafika pamalo otchedwa Bade, anamupachika Iye pamodzi ndi achifwambawo, mmodzi kudzanja lake lamanja ndi winayo la ku lamazere.
34 UJesu wasesithi: Baba, bathethelele; ngoba kabakwazi abakwenzayo. Njalo babelana izembatho zakhe, benza inkatho yokuphosa.
Yesu anati, “Atate, akhululukireni, pakuti sakudziwa chimene akuchita.” Ndipo anagawana malaya ake mochita maere.
35 Labantu bema babukela. Lababusi kanye labo bamklolodela, besithi: Wasindisa abanye, kazisindise yena, uba yena enguKristu, okhethiweyo kaNkulunkulu.
Anthu anayimirira nʼkumaonerera, ngakhalenso akuluakulu ankamulalatira Iye. Iwo anati, “Iye anapulumutsa ena; adzipulumutse yekha ngati ndi Khristu wa Mulungu, Wosankhidwayo.”
36 Labebutho bamklolodela, beza kuye bamnika iviniga,
Asilikalinso anabwera ndi kumunyoza Iye. Iwo anamupatsa vinyo wosasa,
37 besithi: Uba wena uyiNkosi yamaJuda, zisindise wena.
ndipo anati, “Ngati ndiwe Mfumu ya Ayuda, dzipulumutse wekha.”
38 Kwakukhona lombhalo ngaphezu kwakhe kulotshiwe ngamabala esiGriki langesiRoma langesiHebheru othi: LO UYINKOSI YAMAJUDA.
Ndipo panalembedwa chikwangwani pamwamba pake chimene chinati: uyu ndi mfumu ya ayuda.
39 Lomunye wabenzi bobubi ababelengisiwe wamthuka, esithi: Uba wena unguKristu, zisindise wena lathi.
Mmodzi wa achifwambawo, amene anapachikidwa, anamunenera Iye zamwano nati, “Kodi sindiwe Khristu? Dzipulumutse wekha ndi ifenso!”
40 Kodwa omunye waphendula emkhuza, esithi: Wena kawumesabi yini uNkulunkulu, lokhu lawe ukulokhukulahlwa?
Koma wachifwamba winayo anamudzudzula iye nati, “Suopa Mulungu, iwenso ukulandira chilango chomwechi?
41 Thina kambe kusilungele, ngoba semukela okulingene ukwenza kwethu; kodwa lo kenzanga lutho olungafanelanga.
Ife tikulangidwa mwachilungamo, pakuti ife tikulandira monga mwa ntchito zathu. Koma munthu uyu sanachimwe kanthu.”
42 Wasesithi kuJesu: Ungikhumbule, Nkosi, lapha ufika embusweni wakho.
Kenaka anati, “Yesu, mundikumbukire ine pamene mulowa mu ufumu wanu.”
43 UJesu wasesithi kuye: Ngiqinisile ngithi kuwe: Lamuhla uzakuba lami eParadise.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti lero lino udzakhala ndi Ine mʼparadaiso.”
44 Kwakungaba lihola lesithupha, kwaba khona ubumnyama phezu komhlaba wonke kwaze kwaba lihola lesificamunwemunye,
Linali tsopano pafupi ora lachisanu ndi chimodzi, ndipo mdima unagwa pa dziko lonse mpaka ora lachisanu ndi chinayi,
45 futhi ilanga lalifiphaziwe, leveyili lethempeli ladatshulwa phakathi.
pakuti dzuwa linaleka kuwala. Ndipo chinsalu cha mʼNyumba ya Mulungu chinangʼambika pakati.
46 UJesu wasememeza ngelizwi elikhulu esithi: Baba, ezandleni zakho ngibeka umoya wami; esetshilo lokhu waphefumula okokucina.
Yesu anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Atate, ndikupereka mzimu wanga mʼmanja mwanu.” Atanena zimenezi, anamwalira.
47 Kwathi induna yekhulu isibonile okwenzekileyo, yamdumisa uNkulunkulu, isithi: Isibili lumuntu ubelungile.
Kenturiyo, ataona zimene zinachitikazi, analemekeza Mulungu ndipo anati, “Zoonadi, uyu anali munthu wolungama.”
48 Lamaxuku wonke ayebuthene ukubukela lokho, sebebonile izinto ezenzekileyo, babuyela betshaya izifuba zabo.
Anthu onse amene anasonkhana kudzaonerera izi, ataona zinachitikazo, anadziguguda pachifuwa ndipo anachoka.
49 Bonke abazana laye, labesifazana ababemlandela bevela eGalili, bema khatshana, bebona lezizinto.
Koma onse amene anamudziwa Iye, kuphatikiza amayi amene anamutsatira kuchokera ku Galileya, anayimirira akuona zinthu izi.
50 Njalo khangela, indoda ethiwa nguJosefa, ilunga lomphakathi, indoda elungileyo eqotho;
Ndipo taonani panali munthu wina wotchedwa Yosefe, mmodzi wa gulu loweruza, munthu wabwino ndi wolungama.
51 yena wayengavumelananga lecebo lesenzo sabo; wayevela eArimathiya umuzi wamaJuda, laye ngokwakhe wayelindele umbuso kaNkulunkulu;
Iye sanavomereze zimene anzake abwalo anagwirizana ndi kuchita. Iye ankachokera ku mudzi wa Arimateyu wa ku Yudeya ndipo ankayembekezera ufumu wa Mulungu.
52 lowo waya kuPilatu wacela isidumbu sikaJesu.
Atapita kwa Pilato, iye anakapempha mtembo wa Yesu.
53 Wasesethula wasigoqela ngelembu elicolekileyo, wasibeka engcwabeni elaligujwe edwaleni, lapho okwakungazanga kubekwe khona umuntu.
Ndipo anawutsitsa, nawukulunga nsalu yabafuta nawuyika mʼmanda wosemedwa mʼmwala, amene panalibe wina amene anayikidwamo.
54 Kwakulusuku lwamalungiselelo, lesabatha laselisondela.
Linali tsiku lokonzekera ndipo Sabata linatsala pangʼono kuyamba.
55 Labesifazana, ababeze laye bevela eGalili, balandela, balibona ingcwaba, lokuthi isidumbu sibekwe njani.
Amayi amene anabwera ndi Yesu kuchokera ku Galileya, anatsata Yosefe ndipo anaona manda ndi momwe mtembo wake anawuyikira.
56 Basebebuyela emuva balungisa amakha lamagcobo. Ngesabatha basebephumula njengokomlayo.
Kenaka anapita ku mudzi ndi kukakonza mafuta onunkhira. Koma anapuma pa tsiku la Sabata pomvera malamulo.

< ULukha 23 >