< ULukha 14 >

1 Kwasekusithi ekungeneni kwakhe ngesabatha endlini yomunye wabakhulu kubaFarisi ukuthi adle isinkwa, bona basebemqaphela.
Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
2 Njalo khangela, kwakukhona umuntu othile phambi kwakhe owayelombizankulu.
Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo.
3 UJesu wasephendula wakhuluma lezazumthetho labaFarisi, wathi: Kuvunyelwe yini ukusilisa ngesabatha?
Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?”
4 Kodwa bathula. Wasembamba wamsilisa wamyekela ukuthi ahambe.
Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.
5 Wasebaphendula esithi: Nguwuphi kini ongathi elobabhemi kumbe inkabi yakhe ewele emgodini, futhi angahle ayikhuphe ngosuku lwesabatha?
Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?”
6 Abasazange babuyisele impendulo kuye ngalezizinto.
Ndipo iwo analibe choyankha.
7 Wasekhuluma umfanekiso kubo abanxusiweyo, ebona ukuthi bakhetha njani izihlalo zabahloniphekayo, wathi kubo:
Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili:
8 Nxa unxusiwe ngumuntu emtshadweni, ungahlali esihlalweni sabahloniphekayo; hlezi kukhona omkhulu kulawe onxusiweyo nguye,
“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu.
9 futhi okunxusileyo wena laye eze athi kuwe: Mxekele lo; khona uzaqala ukuhlala endaweni esekucineni usulenhloni.
Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.
10 Kodwa nxa unxusiwe, hamba uhlale endaweni esekucineni; ukuze, nxa efika okunxusileyo, athi kuwe: Mngane, yenyukela ngaphezulu; khona kuzakuba ludumo kuwe phambi kwabo abahlezi ekudleni lawe.
Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse.
11 Ngoba wonke oziphakamisayo uzathotshiswa, lozithobayo uzaphakanyiswa.
Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
12 Wasesithi lakulowo owayemnxusile: Nxa usenza ukudla kwemini loba ukudla kwantambama, unganxusi abangane bakho, loba abafowenu, loba izihlobo zakho, loba omakhelwane abanothileyo; hlezi labo babuye bakunxuse, futhi ukwenananiswa kwenziwe kuwe.
Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako.
13 Kodwa nxa usenza idili, nxusa abayanga, izilima, iziqhuli, iziphofu;
Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona.
14 njalo uzabusiswa, ngoba abalalutho lokukwenanisa; ngoba uzakwenaniselwa ekuvukeni kwabalungileyo.
Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
15 Kwathi omunye kwababehlezi laye ekudleni esezwile lezizinto wathi kuye: Ubusisiwe lowo ozakudla isinkwa embusweni kaNkulunkulu.
Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
16 Kodwa wathi kuye: Umuntu othile wenza ukudla kwantambama okukhulu, wanxusa abanengi.
Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri.
17 Ngesikhathi sokudla kwantambama wasethuma inceku yakhe ukuthi ithi kwabanxusiweyo: Wozani, ngoba sekulungisiwe konke.
Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
18 Kodwa bonke baqala omunye lomunye ukuzixolisela. Owokuqala wathi kuye: Ngithenge insimu, ngimele ukuhamba ngiyeyibona; ngiyakuncenga, akungixolisele.
“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
19 Lomunye wathi: Sengithenge izipane ezinhlanu zenkabi, ngiya ukuzilinga; ngiyakuncenga, akungixolisele.
“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
20 Lomunye wathi: Sengithethe umfazi, ngakho ngingeze ngeza.
“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
21 Isibuyile leyonceku yayibikela lezizinto inkosi yayo. Wasethukuthela umninindlu wathi encekwini yakhe: Phuma ngokuphangisa uye emigwaqweni lendleleni zomuzi, ulethe abayanga lezilima leziqhuli leziphofu ubangenise lapha.
“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
22 Inceku yasisithi: Nkosi, sekwenziwe njengokulaya kwakho, njalo indawo isesekhona.
“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
23 Yasisithi inkosi encekwini: Phuma uye ezindleleni lezintangweni ubacindezele bangene, ukuze igcwaliswe indlu yami.
“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze.
24 Ngoba ngithi kini: Kakho kulamadoda ayenxusiwe ozakuzwa ukudla kwami kwantambama.
Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’”
25 Kwakuhamba laye amaxuku amanengi; wasetshibilika wathi kuwo:
Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati,
26 Uba umuntu esiza kimi, futhi engazondi uyise, lonina, lomkakhe, labantwana, labafowabo, labodadewabo, yebo ngitsho leyakhe impilo, angebe ngumfundi wami.
“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.
27 Njalo loba ngubani ongathwali isiphambano sakhe angilandele, angebe ngumfundi wami.
Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.
28 Ngoba nguwuphi kini, othi efuna ukwakha umphotshongo, ongaqali ahlale phansi, abale indleko, ukuthi ulakho yini okokuqedisa?
“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire?
29 Ukuze hlezi, kuthi esebekile isisekelo kodwa angabi lamandla okuqeda, bonke abakubonayo baqale ukumhleka,
Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka,
30 besithi: Lumuntu waqala ukwakha, kodwa kabanga lamandla okuqeda.
nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’
31 Loba yiyiphi inkosi ezakuya empini imelene lenye inkosi engaqali ihlale phansi inakane ngokuthi ilamandla yini ngenkulungwane ezilitshumi okuhlangabezana laleyo eza ilenkulungwane ezingamatshumi amabili ukumelana layo?
“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000?
32 Kodwa uba kungenjalo, ingathi isekhatshana leyo, ithume amanxusa icele okokuthula.
Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere.
33 Ngakho kunjalo wonke kini ongadeli konke alakho, angeke aba ngumfundi wami.
Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.
34 Itshwayi lihle; kodwa uba itshwayi seliduma, lizavuselelwa ngani?
“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani?
35 Kalifanele lamhlabathi ledundulu lomquba; kodwa liyalahlwa ngaphandle. Olendlebe zokuzwa, akezwe.
Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja. “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”

< ULukha 14 >