< KwabaseKholose 3 >

1 Ngakho uba livuswe loKristu, dingani okwaphezulu, lapho akhona uKristu ehlezi ngakwesokunene sikaNkulunkulu.
Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
2 Nakanani ngezinto eziphezulu, kungeyisikho ngezinto ezisemhlabeni.
Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
3 Ngoba lifile, lempilo yenu ifihlwe loKristu kuNkulunkulu.
Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
4 Nxa ebonakaliswa uKristu, oyimpilo yethu, ngalesosikhathi lani lizabonakaliswa laye enkazimulweni.
Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
5 Ngakho bulalani amalunga enu asemhlabeni, ukuphinga, ukungcola, inkanuko embi, ukufisa okubi, lomhawu, oyikukhonza izithombe,
Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
6 okwehla ngalezizinto ulaka lukaNkulunkulu phezu kwabantwana bokungalaleli;
Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
7 elake lahamba kuzo lani, lapho lalihlezi phakathi kwazo.
Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
8 Kodwa khathesi lani khuphani konke lokhu, ulaka, ukuthukuthela, inzondo, inhlamba, ukukhuluma amanyala emlonyeni wenu;
Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
9 lingaqambelani amanga, lokhu selimhlubule umuntu omdala lezenzo zakhe,
Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
10 selembethe omutsha, owenziwa kutsha elwazini njengomfanekiso walowo owamdalayo;
ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
11 okungekho umGriki lomJuda, ukusoka lokungasoki, owezizweni, umSikethiya, isigqili, okhululekileyo; kodwa uKristu uyikho konke lakukho konke.
Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
12 Ngakho yembathani, njengabakhethiweyo bakaNkulunkulu, abangcwele labathandekayo, imihelo yesihawu, ububele, ukuzithoba, ubumnene, ukubekezela;
Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
13 libekezelelane, lithethelelane uba umuntu elensolo komunye; njengoba loKristu walithethelela, ngokunjalo lani;
Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
14 phezu kwakho konke-ke yembathani uthando, oluyisibopho sokuphelela.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
15 Lokuthula kukaNkulunkulu kakubuse enhliziyweni zenu, elibizelwa kukho lani emzimbeni munye; futhi banini ngababongayo.
Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
16 Ilizwi likaKristu kalihlale phakathi kwenu ngokwenotho enhlakanipheni yonke; lifundisane lilayane, ngezihlabelelo, lamahubo odumo, lengoma zomoya, lihlabelela lilomusa enhliziyweni zenu eNkosini.
Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
17 Njalo konke loba yini eliyenzayo, elizwini loba esenzweni, konke kwenzeni ebizweni leNkosi uJesu, libonge uNkulunkulu loBaba ngaye.
Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
18 Bafazi, zehliseleni ngaphansi kwawenu amadoda, njengokufanele eNkosini.
Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Madoda, thandani omkenu, lingabi lokubaba kubo.
Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Bantwana, lalelani abazali ezintweni zonke; ngoba lokhu kuyayithokozisa iNkosi.
Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Bobaba, lingabathukuthelisi abantwana benu, ukuze bangadani.
Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Zisebenzi, lalelani ezintweni zonke labo abangamakhosi njengokwenyama, kungeyisikho ngenkonzo yamehlo njengabathokozisa abantu, kodwa ngobuqotho benhliziyo, lisesaba uNkulunkulu;
Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
23 njalo yonke loba yini eliyenzayo, yenzeni ngenhliziyo, njengeNkosini, njalo kungeyisikho ebantwini;
Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
24 lisazi ukuthi eNkosini lizakwemukela umvuzo welifa; ngoba likhonza iNkosi uKristu.
Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
25 Kodwa owenza okubi uzazemukelela okubi akwenzileyo; njalo kakukho ukubandlulula umuntu.
Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

< KwabaseKholose 3 >