< 2 UPhetro 1 >

1 USimoni Petro, inceku lomphostoli kaJesu Kristu, kulabo abazuze ukholo oluligugu njengathi ngokulunga kukaNkulunkulu wethu loMsindisi wethu uJesu Kristu:
Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
2 Kakwandiswe kini umusa lokuthula elwazini lukaNkulunkulu lolukaJesu iNkosi yethu.
Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
3 Njengamandla akhe obuNkulunkulu asinike zonke izinto ezimayelana lempilo lokukhonza uNkulunkulu, ngokolwazi lwalowo owasibiza ngobukhosi langobuhle;
Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
4 okungakho siphiwe izithembiso ezinkulu kakhulu leziligugu, ukuze ngalezi libe ngabahlanganyeli bemvelo yobuNkulunkulu, seliphephe ekuboleni okusemhlabeni ngenxa yenkanuko.
Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
5 Njalo ngenxa yalokhu-ke selenze yonke inkuthalo, yengezelelani ukulunga ekholweni lwenu, lekulungeni ulwazi,
Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
6 lelwazini ukuzithiba, lekuzithibeni ukubekezela, lekubekezeleni ukwesaba uNkulunkulu,
Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
7 lekwesabeni uNkulunkulu uthando lwabazalwane, lethandweni lwabazalwane uthando.
Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
8 Ngoba uba lezizinto zikhona kini, njalo zisanda, kaziyikulenza livilaphe njalo lingabi lezithelo elwazini lweNkosi yethu uJesu Kristu;
Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
9 ngoba ongelazo lezizinto, uyisiphofu ubonela eduze, esekhohlwe ukuthi wahlanjululwa ezonweni zakhe ezindala.
Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
10 Ngakho, bazalwane, tshisekelani kakhulu ukuqinisa ubizo lokhetho lwenu; ngoba uba lisenza lezizinto, kalisoze likhubeke loba nini.
Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
11 Ngoba ngokunjalo lizakwengezelelwa ngokukhulu ukungena embusweni ophakade weNkosi yethu loMsindisi uJesu Kristu. (aiōnios g166)
Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios g166)
12 Ngakho kangisoze ngiyekele ukulikhumbuza njalonjalo ngalezizinto, lanxa lisazi, njalo liqinisiwe eqinisweni elikhona.
Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
13 Njalo ngibona kulungile ukuthi, nxa ngisesekhona kulelithabhanekele, ngilivuse ngesikhumbuzo;
Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
14 ngisazi ukuthi kuyaphangisa ukususwa kwethabhanekele lami, njengalokhu leNkosi yethu uJesu Kristu ingitshengisile.
chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
15 Kodwa lami ngizakhuthala ukuthi ngezikhathi zonke emva kokusuka kwami libe lesikhumbuzo salezizinto.
Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
16 Ngoba sasingalandeli izinganekwane zobuqili, lapho silazisa amandla lokuza kweNkosi yethu uJesu Kristu, kodwa sasingabazibonelayo ubukhulu bayo.
Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
17 Ngoba wemukela udumo lobukhosi okuvela kuNkulunkulu uBaba, lapho ilizwi elinje lafikiswa kuye ngenkazimulo yobukhosi lisithi: Le yiNdodana yami ethandekayo mina engithokoza kuyo;
Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
18 lalelilizwi thina salizwa livela ezulwini, lapho sasilaye entabeni engcwele.
Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
19 Njalo silelizwi eliqinileyo kakhulu lesiprofetho, elenza kuhle ukuliqaphelisa njengesibane esikhanyayo endaweni emnyama, luze lukhanye usuku, lekhwezi liphumele enhliziyweni zenu;
Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
20 lisazi lokhu kuqala, ukuthi kasikho isiprofetho sombhalo esivela kungcazelo engeyakhe.
Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
21 Ngoba kakuzanga kulethwe isiprofetho ngentando yomuntu, kodwa abantu abangcwele bakaNkulunkulu bakhuluma beqhutshwa nguMoya oNgcwele.
Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.

< 2 UPhetro 1 >