< ULukha 21 >

1 UJesu wathi ekhangela wabona izinothi zifaka iminikelo yazo esitsheni somnikelo.
Yesu atayangʼana, anaona olemera akuyika mphatso zawo mu chosungira ndalama za mʼNyumba ya Mulungu.
2 Wabona njalo umfelokazi ongumyanga efaka okuzinhlamvana kwethusi okubili.
Iye anaonanso mkazi wamasiye wosauka akuyikamo timakopala tiwiri.
3 Wathi, “Ngilitshela iqiniso ngithi umfelokazi lo ongumyanga unikele okudlula bonke abanye.
Iye anati, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mkazi wamasiye wosaukayu wapereka zambiri kuposa ena onsewa.
4 Bonke lababantu banikele izipho zabo ngokwenotho yabo, kodwa yena ebuyangeni bakhe ufake konke abelakho.”
Anthu onsewa atapa mphatso zawo kuchokera pa zochuluka zimene ali nazo; koma uyu, mwa umphawi wake, wapereka zonse zimene ali nazo.”
5 Abanye abafundi bakhe babekhulukhuluma ngokubalazwa kwethempeli ngamatshe amahle langezipho ezazinikelwe kuNkulunkulu. Kodwa uJesu wathi,
Ena mwa ophunzira ake ankachita ndemanga za mmene Nyumba ya Mulungu anayikongoletsera ndi miyala yokongola ndiponso zinthu zina zomwe anthu anapereka kwa Mulungu. Koma Yesu anati,
6 “Mayelana lalokhu elikubona lapha, sizafika isikhathi lapho okungeyikutshiywa ilitshe phezu kwelinye; wonke azaphoselwa phansi.”
“Koma zimene mukuziona panozi, nthawi idzafika pamene ngakhale mwala umodzi omwe sudzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
7 Babuza bathi, “Mfundisi, izinto lezi zizakwenzakala nini? Njalo sizakuba yini isibonakaliso sokuthi sezizakwenzeka na?”
Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, kodi zonsezi zidzachitika liti? Ndipo tidzaonera chiyani kuti zili pafupi kuchitika?”
8 Waphendula wathi, “Qaphelani lingakhohliswa. Ngoba abanengi bazakuza ngebizo lami besithi, ‘Nginguye,’ njalo bathi, ‘Isikhathi sesisondele.’ Lingabalandeli.
Iye anayankha kuti, “Chenjerani kuti musanyengedwe. Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati ‘Ine ndine Iye’ ndi kuti ‘Nthawi yayandikira.’ Musadzawatsate iwo.
9 Nxa lisizwa ngezimpi lezikhukhulambuso, lingethuki. Lezizinto kuzamele zenzeke kuqala, kodwa isiphetho kasizukufika ngalesosikhathi.”
Mukadzamva zankhondo ndi zipolowe, musadzachite mantha. Zinthu izi ziyenera kuchitika poyamba, koma chimaliziro sichidzafika nthawi yomweyo.”
10 Wasesithi kubo: “Isizwe sizavukela isizwe, lombuso uvukele umbuso.
Kenaka anawawuza kuti, “Mtundu wa anthu udzawukirana ndi mtundu wina, ndi ufumu kuwukira ufumu wina.
11 Kuzakuba lokuzamazama komhlaba okukhulu, indlala lezifo ezindaweni ezinengi, izehlakalo ezesabekayo lezibonakaliso ezinengi zivela emkhathini.
Kudzakhala zivomerezi zazikulu, njala ndi miliri mʼmalo osiyanasiyana, ndi zinthu zoopsa ndi zizindikiro zamphamvu kuchokera kumwamba.
12 Kodwa kungakenzakali konke lokhu bazalibamba, balihlukuluze. Bazalinikela emasinagogweni baliphosele lasezintolongweni njalo lizamiswa phambi kwamakhosi lababusi ngenxa yebizo lami.
“Koma zonsezi zisanachitike, adzakugwirani ndi kukuzunzani. Adzakuperekani ku masunagoge ndi ku ndende, ndipo adzakutengerani pamaso pa mafumu ndi olamulira, ndipo zonsezi zidzachitika chifukwa cha dzina langa.
13 Lokhu kuzalenza libe ngofakazi kimi.
Umenewu udzakhala mwayi wanu ochitira umboni.
14 Kodwa bekani amaphaphu phansi, lingazihluphi ngokuthi lizazivikela lisithini.
Koma tsimikizani mtima kuti musadzade nkhawa za momwe mudzadzitchinjirizire.
15 Ngoba ngizalinika amazwi lokuhlakanipha ukuze angabikhona ezitheni zenu ozalehlula loba aliphikise.
Pakuti Ine ndidzakupatsani mawu ndi nzeru kotero kuti palibe mmodzi wa adani anu adzathe kuwakana kapena kuwatsutsa.
16 Lizanikelwa ngabazali, ngabafowenu layizihlobo labangane njalo abanye benu bazalibulala.
Inu mudzaperekedwa ndi makolo anu, abale, anansi ndi abwenzi anu ndipo ena mwa inu adzakuphani.
17 Bonke abantu bazalizonda ngenxa yami.
Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine.
18 Kodwa kakuyikubhubha lanwele olulodwa emakhanda enu.
Koma palibe tsitsi limodzi la mʼmutu mwanu lidzawonongeke.
19 Bekezelani, lizasindiswa.
Mukadzalimbikira ndiye mudzapeze moyo.
20 Lingabona iJerusalema isihonqolozelwe yizimpi lizakwazi ukuthi incithakalo isisondele.
“Mukadzaona Yerusalemu atazingidwa ndi magulu ankhondo, inu mudzadziwe kuti kuwonongeka kwake kuli pafupi.
21 Lapho-ke akuthi labo abaseJudiya babalekele ezintabeni, abasedolobheni kabaphume, kuthi labo abasemaphandleni bangangeni edolobheni.
Pamenepo amene ali ku Yudeya adzathawire ku mapiri, amene ali mu mzinda adzatulukemo, ndi amene ali ku midzi asadzalowe mu mzinda.
22 Ngoba lesi yisikhathi sokujeziswa ukugcwalisa konke okwalotshwayo.
Pakuti iyi ndi nthawi yachilango pokwaniritsa zonse zimene zinalembedwa.
23 Yeka ubulukhuni obuzakuba khona ngalezonsuku kwabesifazane abakhulelweyo labangabadlezane! Kuzakuba khona ukuhlukuluzeka okukhulu elizweni lolaka phezu kwabantu.
Zidzakhala zoopsa nthawi imenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! Kudzakhala masautso aakulu mʼdziko ndipo anthu onse adzawakwiyira.
24 Bazakuwa ngenkemba babuthwe babe yizibotshwa zezizwe zonke. IJerusalema izagidagidwa ngabeZizwe kuze kugcwaliseke izikhathi zabeZizwe.
Iwo adzaphedwa ndi lupanga ndi kutengedwa ukapolo kupita ku mayiko wonse. Yerusalemu adzaponderezedwa ndi anthu a mitundu ina mpaka nthawi ya a mitundu ina itakwaniritsidwa.
25 Kuzabakhona izibonakaliso elangeni, enyangeni lasezinkanyezini. Emhlabeni izizwe zizakuba phakathi kosizi lokudideka ngenxa yokuhuba lokukhaphaza kolwandle.
“Padzakhala zizindikiro zodabwitsa pa dzuwa, mwezi ndi nyenyezi. Pa dziko lapansi, mitundu ya anthu idzakhala mʼmasautso ndipo idzathedwa nzeru pakumva mkokomo ndi mafunde a mʼnyanja.
26 Abantu bazaphela amandla ngokwesaba, behlutshwa yilokho okuzayo emhlabeni, ngoba izisekelo zasezulwini zizazanyazanyiswa.
Anthu adzakomoka chifukwa cha mantha, akadzamva za zimene zikubwera pa dziko lapansi, pakuti zinthu zamlengalenga zidzagwedezeka.
27 Ngalesosikhathi bazayibona iNdodana yoMuntu isiza ngeyezi ilamandla lenkazimulo enkulu.
Nthawi imeneyo adzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
28 Nxa lezizinto seziqala ukwenzakala manini liqine, liphakamise amakhanda enu, ngoba ukuhlengwa kwenu sekusondela.”
Zinthu izi zikadzayamba kuchitika, mudzayimirire ndi kutukula mitu yanu, chifukwa chipulumutso chanu chayandikira.”
29 Wabatshela umfanekiso lo wathi, “Khangelani esihlahleni somkhiwa kanye lezinye zonke izihlahla.
Iye anawawuza fanizo ili, “Taonani mtengo wamkuyu ndi mitengo ina yonse.
30 Nxa zihluma lizazibonela lani njalo lazi ukuthi ihlobo selisondele.
Ikamatulutsa masamba, mumakhoza kudzionera nokha ndi kudziwa kuti dzinja lili pafupi.
31 Kanjalo-ke, nxa lingabona lezizinto sezisenzakala, lazi ukuthi umbuso kaNkulunkulu ususondele.
Chimodzimodzinso, mukadzaona zinthu zonsezi, dziwani kuti ufumu wa Mulungu uli pafupi.
32 Ngilitshela iqiniso, lesisizukulwane kasiyikudlula zize zenzakale zonke lezizinto.
“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika.
33 Izulu lomhlaba kuzedlula, kodwa amazwi ami kawayikwedlula lanini.
Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
34 Nanzelelani funa inhliziyo zenu zithundubale ngokuzitika lokudakwa lokunqineka ngezinto zalimpilo, ngoba lolosuku luzalijuma njengomjibila.
“Samalani, kuti mitima yanu ingalemetsedwe ndi maphwando, kuledzera ndi kudera nkhawa za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingadzakupezeni modzidzimutsa ngati msampha.
35 Ngoba luzafikela bonke labo abahlala kuwo wonke umhlaba.
Pakuti lidzafika pa onse okhala pa dziko lonse lapansi.
36 Hlalani lilindile, likhulekele ukuthi liphephe kukho konke osekuzakwenzeka masinyane, lokuthi libe lamandla okuma phambi kweNdodana yoMuntu.”
Khalani tcheru nthawi zonse ndi kupemphera kuti inu mudzathe kuthawa zonse zimene zili pafupi kuchitika, ndi kuti mudzathe kuyima pamaso pa Mwana wa Munthu.”
37 Insuku zonke uJesu wayefundisa ethempelini kuthi kusihlwa aphume ayechitha ubusuku eqaqeni olwaluthiwa yiNtaba yama-Oliva,
Tsiku lililonse Yesu amaphunzitsa ku Nyumba ya Mulungu, ndi madzulo ali wonse Iye amachoka kukakhala pa phiri la Olivi usiku wonse.
38 njalo abantu bonke babesiza ekuseni kakhulu ukuzamuzwa ethempelini.
Ndipo anthu onse amabwera mmamawa kudzamumva Iye ku Nyumba ya Mulungu.

< ULukha 21 >