< U-Esta 5 >

1 Ngelanga lesithathu u-Esta wagqoka izembatho zakhe zobukhosi wema enkundleni engaphakathi kwesigodlo phambi kwendlu yenkosi. Inkosi yayihlezi esihlalweni sayo sobukhosi endlini yayo, ikhangele emnyango.
Tsiku lachitatu Estere anavala zovala zake zaufumu ndipo anayima mʼbwalo la mʼkati la nyumba yaufumu choyangʼana ku chipinda chachikulu cha mfumu. Mfumu inakhala pa mpando waufumu mʼchipinda chachikulu moyangʼana ku chipata cholowera mʼnyumba yaufumu.
2 Yathi ibona iNdlovukazi u-Esta imi enkundleni, yathokoza ngaye, yasiselula intonga yayo yegolide eyayisesandleni sayo, yamkhomba ngayo. U-Esta wasesondela wathinta isihloko sentonga.
Mfumu itaona Estere atayima mʼbwalomo inakondwera naye ndipo anamuloza ndi ndodo yagolide imene inali mʼdzanja lake. Choncho Estere anayandikira ndi kukhudza msonga ya ndodoyo.
3 Inkosi yasibuza yathi, “Kutheni Ndlovukazi Esta? Siyini isicelo sakho na? Uzanikwa loba yini, okungafika kungxenye yombuso.”
Kenaka mfumu inati kwa iye, “Kodi mukufuna chiyani, inu mfumukazi Estere? Nanga pempho lanu ndi chiyani? Ngakhale mutapempha theka la ufumu, ndidzakupatsani.”
4 U-Esta wathi, “Nxa inkosi ithokoza ngalokhu, bengicela ukuthi inkosi kanye loHamani beze lamhla edilini engililungisele yona.”
Ndipo Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni, mfumu, mubwere lero pamodzi ndi Hamani kuphwando limene ndakonzera inu mfumu.”
5 Inkosi yathi, “UHamani keze khathesi, ukuze kwenziwe okucelwa ngu-Esta.” Inkosi loHamani baya edilini elalilungiswe ngu-Esta.
Mfumu inati, “Muwuzeni abwere Hamani msanga, kotero kuti tichite monga Estere wapempha.” Choncho mfumu ndi Hamani anafika kuphwando limene Estere anakonza.
6 Kwathi besanatha iwayini, inkosi yambuza njalo u-Esta yathi, “Siyini isicelo sakho? Uzakukwamukeliswa. Kuyini okucelayo na? Uzanikwa loba yini okungafika kungxenye yombuso.”
Akumwa vinyo, mfumu inamufunsano Estere kuti, “Kodi ukupempha chiyani tsopano? Chimene uti upemphe ndikupatsa. Chopempha chako ndi chiti? Ngakhale utafuna mpaka theka la ufumu, ndidzakupatsa.”
7 U-Esta waphendula wathi, “Isikhalazo sami lesicelo sami yilokhu:
Estere anayankha kuti, “Pempho langa ndi chofuna changa ndi ichi:
8 Nxa inkosi ingamukela ngomusa njalo nxa inkosi ithokoza ngokwamukela isikhalazo sami njalo igcwalise isicelo sami, bengicela ukuthi inkosi kanye loHamani kusasa beze edilini engizabalungisela lona. Kulapho engizaphendula okubuzwe yinkosi.”
Ngati mwandikomera mtima mfumu ndiponso ngati chingakukondweretseni mfumu kundipatsa chimene ndapempha ndi kuchita zimene ndifuna, mubwere mawa inu mfumu ndi Hamani ku phwando limene ndidzakukonzerani. Ndipo ndidzakuyankhani mfumu funso lanu.”
9 UHamani wasuka lapho mhlalokho ethabe kakhulukazi. Kodwa uthe ebona uModekhayi esesangweni lenkosi wananzelela ukuthi kamsukumeli loba ukutshengisa ukwesaba phambi kwakhe, wagcwalelana ngokumthukuthelela uModekhayi.
Tsiku limenelo Hamani anatuluka wokondwa ndi wosangalala kwambiri. Koma ataona Mordekai pa chipata cha mfumu ndi kuti sanayimirire kapena kumupatsa ulemu pamene iye amadutsa, Hamani anamukwiyira kwambiri,
10 Kodwa wazibamba waya emzini wakhe, wabiza abangane bakhe ndawonye kanye loZereshi umkakhe,
komabe Hamani anadziletsa ndipo anapita ku nyumba kwake. Anayitana abwenzi ake pamodzi ndi mkazi wake Zeresi.
11 uHamani wasezincoma kubo ngenotho yakhe enengi, langamadodana akhe amanengi, kanye lazozonke izindlela inkosi eyayimhlonipha ngazo lokuthi imphakamise yambeka phezu kwezinye izikhulu leziphathamandla.
Hamani anawawuza za kuchuluka kwa chuma chake ndi kuti anali ndi ana aamuna ambiri. Anawawuzanso za mmene mfumu inamukwezera ndi kumuyika kukhala woposa nduna ndi olemekezeka onse.
12 UHamani wengeza wathi, “Njalo akusikho kodwa lokhu. Yimi ngedwa zwi umuntu omenywe yiNdlovukazi u-Esta ukuba ngiphelekezele inkosi edilini elenzileyo. Njalo usenginxusile kanye lenkosi kusasa.
Hamani anawonjeza kuti, “Ndipotu si zokhazi. Ndine ndekha amene ndayitanidwa pamodzi ndi mfumu kuphwando limene mfumukazi Estere anatikonzera. Ndipo mawa wandiyitananso pamodzi ndi mfumu.
13 Kodwa konke lokhu akungisuthisi ikakhulu nxa ngilokhu ngibona umJuda loya onguModekhayi ehlezi esangweni lenkosi.”
Koma zonsezi sindikhutira nazo ndikamaona nthawi zonse Myuda uja Mordekai atakhala pa chipata cha mfumu.”
14 Umkakhe uZereshi kanye labangane bakhe bonke bathi kuye, “Yenza indawo yokulengisa abantu, ibe zingalo ezingamatshumi ayisikhombisa lanhlanu ubude, ubusucela inkosi ekuseni ukuba ilengise uModekhayi lapho. Ube usuziyela edilini uchelesile.” Umcabango lo wamthokozisa kakhulu uHamani, yasisakhiwa indawo yokulengisa.
Mkazi wake Zeresi ndi abwenzi ake onse aja anamuwuza kuti, “Anthu apange mtanda wotalika mamita 23 ndipo mmawa upemphe mfumu kuti anthu akhomerepo Mordekai. Kenaka upite ndi mfumu kuphwando mokondwa.” Hamani anakondwera ndi uphungu umenewu ndipo mtanda unapangidwa.

< U-Esta 5 >