< Psalmi 85 >

1 Koraha bērnu dziesma, dziedātāju vadonim. Tu, ak Kungs, Savai zemei lēnīgs bijis un Jēkaba cietumu novērsis,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Yehova munakomera mtima dziko lanu; munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.
2 Tu Savu ļaužu noziegumu esi piedevis, visus viņu grēkus apklājis; (Sela)
Munakhululukira mphulupulu za anthu anu ndi kuphimba machimo awo onse. (Sela)
3 Tu visu Savu dusmību atņēmis, no Savas karstās bardzības atstājies:
Munayika pambali ukali wanu wonse ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.
4 Atved mūs atpakaļ, ak Dievs, mūsu Pestītājs, un lai Tava dusmība pret mums mitās.
Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu, ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.
5 Vai tad Tu mūžīgi pret mums gribi dusmoties un Tavu bardzību turēt uz bērnu bērniem?
Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?
6 Vai tad Tu negribi mūs atkal atspirdzināt, ka Tavi ļaudis iekš Tevis var priecāties?
Kodi simudzatitsitsimutsanso, kuti anthu anu asangalale mwa Inu?
7 Parādi mums, Kungs, Tavu žēlastību un dod mums Tavu pestīšanu.
Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova, ndipo tipatseni chipulumutso chanu.
8 Es klausīšu, ko Tas Kungs, tas stiprais Dievs, runā, jo Viņš sola mieru Saviem ļaudīm un Saviem svētiem, lai tie negriežās uz ģeķību.
Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena; Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake, koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.
9 Tiešām, Viņa palīdzība ir tuvu klāt tiem, kas Viņu bīstas, ka mūsu zemē gods mājo,
Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye, kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.
10 Ka žēlastība un uzticība sastopas, ka taisnība un miers skūpstās,
Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi; chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.
11 Ka patiesība no zemes izaug un taisnība no debesīm skatās.
Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi, ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.
12 Un Tas Kungs dos labumu un mūsu zeme dos savus augļus.
Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino, ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.
13 Taisnība staigās Viņa priekšā un ņemsies Viņa pēdas par ceļu.
Wolungama amapita patsogolo pake ndi kukonza njira za mapazi ake.

< Psalmi 85 >