< Psalmi 48 >

1 Koraha bērnu dziesma. Dziedātāju vadonim. Tas Kungs ir liels un ļoti teicams mūsu Dieva pilsētā Viņa svētā kalnā.
Nyimbo. Salimo la ana a Kora. Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.
2 Jauki paceļas Ciānas kalns, visas zemes prieks, ziemeļa pusē, tā lielā Ķēniņa pilsēta.
Lokongola mu utali mwake, chimwemwe cha dziko lonse lapansi. Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni, mzinda wa Mfumu yayikulu.
3 Dievs viņas pilīs ir atzīts par patvērumu.
Mulungu ali mu malinga ake; Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.
4 Jo redzi, ķēniņi sapulcējās un atnāca kopā;
Pamene mafumu anasonkhana pamodzi, pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,
5 Tie redzēja un brīnījās, tie iztrūcinājās un steidzās projām.
iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri; anathawa ndi mantha aakulu.
6 Drebēšana tos tur aizņēma, mokas tā kā sievu bērnu sāpēs.
Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera, ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.
7 Tu sadauzi lielos jūras kuģus caur austriņu.
Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.
8 Tā kā bijām dzirdējuši, tā to esam redzējuši Tā Kunga Cebaot pilsētā, mūsu Dieva pilsētā. Dievs to stiprinās mūžīgi. (Sela)
Monga momwe tinamvera, kotero ife tinaona mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse, mu mzinda wa Mulungu wathu. Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.
9 Ak Dievs, mēs pieminam Tavu žēlastību Tavā svētā namā.
Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu, ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.
10 Ak Dievs, tā kā Tavs vārds, tāpat ir Tava slava līdz pasaules galam, Tava labā roka ir taisnības pilna.
Monga dzina lanu, Inu Mulungu, matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.
11 Lai Ciānas kalns priecājās un Jūda meitas lai līksmojās Tavu tiesu labad.
Phiri la Ziyoni likukondwera, midzi ya Yuda ndi yosangalala chifukwa cha maweruzo anu.
12 Ejat ap Ciānu un apmetaties ap viņu, skaitiet viņas torņus.
Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo, werengani nsanja zake.
13 Liekat vērā viņas mūrus, apraugāt viņas augstos namus, ka pēcnākamiem radiem to varat izteikt.
Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake, penyetsetsani malinga ake, kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.
14 Jo šis Dievs ir mūsu Dievs mūžīgi mūžam. Viņš mūs vadīs līdz mūža galam.
Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha; Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

< Psalmi 48 >