< Psalmi 120 >

1 Svētku dziesma. Es piesaucu To Kungu savās bēdās, un Viņš mani paklausa.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga, ndipo Iye amandiyankha.
2 Kungs, izglāb manu dvēseli no melkuļu lūpām un viltnieku mēlēm.
Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza, ndi kwa anthu achinyengo.
3 Ko viltīgā mēle Tev dos, jeb ko viņa Tev pieliks?
Kodi adzakuchitani chiyani, ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?
4 Tā ir kā varoņa asas bultas, kā degošas paegļu ogles.
Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo, ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.
5 Ak vai, man, ka esmu svešinieks iekš Mešeha, un ka man jādzīvo Kedara dzīvokļos.
Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki, kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!
6 Par ilgu manai dvēselei dzīvot pie tiem, kas mieru ienīst.
Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati pa iwo amene amadana ndi mtendere.
7 Es turu mieru, bet tikko es runāju, tad tie ceļ ķildu.
Ine ndine munthu wamtendere; koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

< Psalmi 120 >