< Sog̒u 1 >

1 Un notika pēc Jozuas nāves, ka Israēla bērni To Kungu vaicāja un sacīja: kas mums ies priekšā, karot pret Kanaāniešiem?
Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
2 Un Tas Kungs sacīja: Jūdam būs iet: redzi, Es to zemi esmu devis viņa rokā.
Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
3 Tad Jūda sacīja uz Sīmeanu, savu brāli: nāc man līdz uz manu daļu, un karosim pret Kanaāniešiem, tad es arīdzan tev iešu līdz uz tavu daļu. Un Sīmeans viņam gāja līdz.
Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
4 Un Jūda cēlās, un Tas Kungs nodeva viņu rokā Kanaāniešus un Fereziešus, un tas kāva Bezekā desmit tūkstoš vīrus.
Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
5 Un tie atrada Adoni-Bezeku Bezekā un karoja pret viņu un sakāva Kanaāniešus un Fereziešus.
Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
6 Un Adoni-Bezeks bēga, bet tie viņam dzinās pakaļ un to sagūstīja un nocirta īkšķus pie viņa rokām un kājām.
Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
7 Tad Adoni-Bezeks sacīja: septiņdesmit ķēniņi ar nocirstiem roku un kāju īkšķiem salasīja apakš mana galda druskas; kā es esmu darījis, tā man Dievs ir atmaksājis. Un tie to veda uz Jeruzālemi, un viņš tur nomira.
Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
8 Jo Jūda bērni bija karojuši pret Jeruzālemi un to uzņēmuši un ar zobena asmeni situši un to pilsētu iededzinājuši.
Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
9 Un pēc tam Jūda bērni nogāja karot pret tiem Kanaāniešiem, kas dzīvoja kalnos un pret dienas vidu un ielejā.
Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
10 Un Jūda cēlās pret tiem Kanaāniešiem, kas Hebronē dzīvoja, (bet Hebrones vārds bija senāk KiriatArba, ) un tie kāva Zezaju un Aķimanu un Talmaju.
Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
11 Un no turienes tie cēlās pret tiem, kas Debirā dzīvoja, bet Debiras vārds bija senāk KiriatZevere.
Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
12 Un Kālebs sacīja: kas KiriatZeveri kaus un viņu uzņems, tam es savu meitu Aksu došu par sievu.
Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
13 Tad to uzņēma Otniēls, Ķenasa, Kāleba jaunākā brāļa, dēls, un viņš tam Aksu, savu meitu, deva par sievu.
Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
14 Un notikās, kad viņa pie tā nāca, tad viņa to paskubināja, no viņas tēva tīrumu lūgt, un viņa nolēca no ēzeļa; tad Kālebs uz to sacīja: kas tev ir?
Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
15 Un tā uz viņu sacīja: dod man svētību, jo tu man esi devis diena vidus zemi, tad dod man arī ūdens avotus. Tad Kālebs viņai deva avotus augšā un avotus ielejā.
Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
16 Un tā Kenieša, Mozus tēvoča, bērni, gāja Jūda bērniem līdz no tās palmu pilsētas uz Jūda tuksnesi, kas no Arada uz dienas vidu, un nogāja un dzīvoja starp tiem ļaudīm.
Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
17 Un Jūda cēlās ar savu brāli Sīmeanu, un tie kāva tos Kanaāniešus, kas Cevatā dzīvoja, un tos izdeldēja; un nosauca tās pilsētas vārdu Horma.
Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
18 Un Jūda uzņēma arī Gacu ar viņas apgabalu, un Askalonu ar viņas apgabalu un Ekronu ar viņas apgabalu.
Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
19 Un Tas Kungs bija ar Jūdu, ka viņš tos kalnus ieņēma. Jo tos, kas ielejā dzīvoja, viņš nevarēja izdzīt, tāpēc ka tiem bija dzelzs rati.
Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
20 Un Kālebam tie deva Hebroni, kā Mozus bija runājis, un tas no turienes izdzina Enaka trīs dēlus.
Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
21 Bet Benjamina bērni neizdzina tos Jebusiešus, kas Jeruzālemē dzīvoja; un Jebusieši dzīvo Jeruzālemē ar Benjamina bērniem kopā līdz šai dienai.
Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
22 Un Jāzepa nams arī cēlās uz Bēteli, un Tas Kungs bija ar viņiem.
A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
23 Un Jāzepa nams lika Bēteli izlūkot, bet šīs pilsētas vārds senāk bija Lūza.
Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
24 Un tie izlūki redzēja vīru no pilsētas ārā nākam un sacīja uz viņu: rādi mums jel, kur pilsētā var iekļūt, tad mēs darīsim žēlastību pie tevis.
Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
25 Un kad viņš tiem rādīja, kur tie varēja iekļūt pilsētā, tad tie to pilsētu sita ar zobena asmeni, bet to vīru un visus viņa radus tie lika mierā.
Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
26 Tad tas vīrs nogāja uz Hetiešu zemi un uztaisīja pilsētu un nosauca viņas vārdu Lūza; tas ir viņas vārds līdz šai dienai.
Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
27 Un Manasus neizdzina tos, kas bija Betzeanā, un viņas ciemos, nedz Taēnakā un viņas ciemos, nedz Dorā un viņas ciemos, nedz Jebleamā un viņas ciemos, nedz Meģidū un viņas ciemos, un tie Kanaānieši iesāka palikt šai zemē.
Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
28 Bet kad Israēls palika stiprs, tad viņš Kanaāniešus piespieda pie klausības, bet izdzīt tos neizdzina.
Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
29 Efraīms arīdzan neizdzina tos Kanaāniešus, kas Gazerā dzīvoja, bet Kanaānieši dzīvoja starp viņiem Gazerā.
Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
30 Zebulons neizdzina Kitronas iedzīvotājus, nedz Naālalas iedzīvotājus, bet Kanaānieši dzīvoja starp viņiem un klausīja.
Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
31 Ašers neizdzina Akas iedzīvotājus, nedz tos iedzīvotājus, kas Sidonā. Aķelabā, Akzibā, Elbā, Afekā, Rekobā,
A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
32 Bet Ašerieši dzīvoja starp Kanaāniešiem, tās zemes iedzīvotājiem, jo viņi tos neizdzina.
Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
33 Naftalus neizdzina tos iedzīvotājus no BetŠemesas, nedz tos iedzīvotājus no ZetAnatas, bet dzīvoja starp Kanaāniešiem, tās zemes iedzīvotājiem, bet BetŠemesas un BetAnatas iedzīvotāji tiem palika par klausītājiem.
Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
34 Un Amorieši iedzina Dana bērnus kalnos, jo tie tiem neļāva nākt ielejā.
Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
35 Amorieši arī iesāka palikt Eres kalnos Ajalonā un Zaālbima, bet Jāzepa nama roka tos spieda, ka tie palika par klausītājiem.
Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
36 Un Amoriešu robeža bija no Akrabu kalniem un no Zelas uz augšu.
Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.

< Sog̒u 1 >