< Ījaba 7 >

1 Vai cilvēkam nav karš virs zemes, un vai viņa dienas nav kā algādža dienas?
“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi? Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?
2 Tā kā kalps ilgojās pēc ēnas un kā algādzis gaida uz savu algu,
Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo, kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,
3 Tāpat man nākuši daudz bēdīgi mēneši, un grūtas naktis man ir piešķirtas.
choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe, ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.
4 Kad apguļos, tad es saku: kad atkal celšos? un vakars vilcinājās, un es apnīkstu mētāties gultā līdz gaismai.
Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’ Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.
5 Mana miesa ir apsegta ar tārpiem un vātīm, mana āda sadzīst un čūlo atkal.
Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera, khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.
6 Manas dienas ir ātrākas nekā vēvera (audēja) spole un beidzās bez nekādas cerības.
“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu, ndipo amatha wopanda chiyembekezo.
7 Piemini, ka mana dzīvība ir vējš un mana acs labuma vairs neredzēs.
Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya; sindidzaonanso masiku achisangalalo.
8 Acs, kas nu mani redz, manis vairs neredzēs. Tavas acis uz mani skatās, un es vairs neesmu.
Amene akundiona tsopano akundiona; mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.
9 Mākonis iznīkst un aiziet, - tāpat kas kapā nogrimst, nenāks atkal augšām. (Sheol h7585)
Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka, momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera. (Sheol h7585)
10 Viņš neatgriezīsies atkal savā namā, un viņa vieta viņu vairs nepazīs.
Iye sadzabweranso ku nyumba kwake ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.
11 Tā tad es savu muti neturēšu, es runāšu savās sirds bēdās, es žēlošos savā sirdsrūgtumā.
“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete; ndidzayankhula mopsinjika mtima, ndidzadandaula mowawidwa mtima.
12 Vai tad es esmu kā jūra, vai kā liela jūras zivs, ka tu ap mani noliec vakti?
Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja kuti inu mundiyikire alonda?
13 Kad es saku: mana gulta man iepriecinās, manas cisas atvieglinās manas vaimanas,
Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,
14 Tad Tu mani izbiedē ar sapņiem, un caur parādīšanām Tu mani iztrūcini,
ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,
15 Tā ka mana dvēsele vēlās būt nožņaugta, labāki mirt nekā tā izģinst.
kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa, kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.
16 Es esmu apnicis, man netīk mūžam dzīvot; atstājies jel no manis, jo manas dienas ir kā nekas.
Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse. Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.
17 Kas ir cilvēks, ka Tu viņu tik augsti turi un ka Tu viņu lieci vērā,
“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere, kuti muzisamala zochita zake,
18 Un viņu piemeklē ik rītu, viņu pārbaudi ik acumirkli,
kuti muzimusanthula mmawa uliwonse ndi kumamuyesa nthawi yonse?
19 Ka Tu nemaz no manis neatstājies un mani nepameti, ne siekalas ierīt?
Kodi simudzaleka kumandizonda kuti ndipezeko mpata wopumula?
20 Ja esmu grēkojis, ko es Tev darīšu, Tu cilvēku sargs? Kāpēc Tu mani esi licis Sev par mērķi, ka es sev pašam palicis par nastu?
Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu, Inu wopenyetsetsa anthu? Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu? Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?
21 Un kāpēc Tu manus pārkāpumus nepiedod un neatņem manu noziegumu? Jo nu es apgulšos pīšļos, un kad Tu mani meklēsi, tad manis vairs nebūs.
Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga ndi kundichotsera machimo anga? Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda; mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

< Ījaba 7 >