< Pāvila 1. Vēstule Timotejam 3 >

1 Tas ir patiesīgs vārds: ja kas iekāro bīskapa amatu, tas iekāro teicamu darbu.
Mawu woona ndi awa: Ngati munthu akufunitsitsa atakhala woyangʼanira, ndiye kuti akufuna ntchito yabwino.
2 Tad nu bīskapam pienākas būt nenoziedzīgam, vienas sievas vīram, sātīgam, prātīgam, godīgam, kas labprāt dod mājas vietu, un kas māk mācīt;
Tsono woyangʼanira ayenera kukhala munthu wopanda chotsutsika nacho, mwamuna wa mkazi mmodzi yekha, woganiza bwino, wodziretsa, waulemu, wosamala bwino alendo, wodziwa kuphunzitsa.
3 Kas nav dzērājs, ne rējējs, nedz negodīgas peļņas dzinējs, bet lēnīgs, ne strīdīgs, ne naudas kārīgs;
Asakhale chidakwa, asakhale wandewu, koma wofatsa, asakhale wokonda mikangano, kapena wokonda ndalama.
4 Kas savu namu labi valda, kam bērni, kas paklausa ar visu godu;
Akhale wodziwa kusamala bwino banja lake ndi kulera ana ake bwino, kuti akhale omvera ndi aulemu weniweni.
5 (Bet ja kas savu paša namu nezin valdīt, kā tas gādās par Dieva draudzēm?)
(Ngati munthu sadziwa kusamala banja lake lomwe, angathe bwanji kusamala mpingo wa Mulungu?)
6 Ne tāds, kas kristīgu ticību tikko uzņēmis, lai neuzpūšas un neiekrīt zaimotāja tiesā.
Asakhale wongotembenuka mtima kumene kuopa kuti angadzitukumule napezeka pa chilango monga Satana.
7 Bet viņam vajag arī labas liecības no tiem, kas ārā, ka neiekrīt nievāšanā un zaimotāja valgos.
Ayeneranso kukhala munthu wambiri yabwino ndi akunja, kuti anthu asamutonze nagwa mu msampha wa Satana.
8 Tāpat arī draudzes kopējiem būs būt godīgiem, kam nav divējādas mēles, ne vīna plītniekiem, nedz negodīgas peļņas dzinējiem,
Momwemonso atumiki, akhale anthu oyenera ulemu, woona mtima, osakhala okonda zoledzeretsa, osakonda kupeza zinthu mwachinyengo.
9 Kas ticības noslēpumu tur iekš šķīstas zināmas sirds.
Ayenera kugwiritsa mozama choonadi cha chikhulupiriro ndi kukhala ndi chikumbumtima chabwino.
10 Un šiem arīdzan būs papriekš tapt pārbaudītiem, pēc lai tie kalpo, ja tie ir bezvainīgi.
Ayambe ayesedwa kaye, ndipo ngati palibe kanthu kowatsutsa, aloleni akhale atumiki.
11 Tāpat arī sievām būs būt godīgām, ne mēlnesēm, bet sātīgām, uzticīgām visās lietās.
Momwemonso, akazi akhale olemekezeka, osasinjirira koma oganiza bwino ndi odalirika pa chilichonse.
12 Draudzes kopējiem būs būt vienas sievas vīriem, kas savus bērnus un savu namu labi valda.
Mtumiki akhale wokhulupirika kwa mkazi wake ndipo ayenera kukhala wosamalira bwino ana ake ndi onse a pa khomo pake.
13 Jo kas labi kalpojuši, tie pelnās labu pakāpi un daudz drošības iekš ticības, kas ir iekš Kristus Jēzus.
Iwo amene atumikira bwino amakhala ndi mbiri yabwino ndipo amakhala chitsimikizo chachikulu cha chikhulupiriro chawo mwa Khristu Yesu.
14 To es tev rakstu, cerēdams it drīz nākt pie tevis;
Ngakhale ndili ndi chiyembekezo choti ndifika komweko posachedwapa, ndikukulemberani malangizo awa.
15 Bet ja es aizkavētos, lai tu zini, kā pienākas turēties Dieva namā, kas ir tā dzīvā Dieva draudze, tās patiesības pīlārs un pamats.
Ine zina zikandichedwetsa kubwera, mudziwe za mmene anthu ayenera kukhalira mʼNyumba ya Mulungu, imene ndi mpingo wa Mulungu wamoyo, mzati ndi maziko achoonadi.
16 Un teicami liels ir tas dievbijāšanas noslēpums: Dievs ir parādīts miesā, taisnots garā, skatīts no eņģeļiem, sludināts tautām, ticēts pasaulē, uzņemts godībā.
Mosakayikira, chinsinsi cha chikhulupiriro chathu chachikulu: Khristu anaonekera ali ndi thupi la munthu, Mzimu anamuchitira umboni, angelo anamuona, analalikidwa pakati pa mitundu yonse, dziko lapansi linamukhulupirira, anatengedwa kupita kumwamba mwa ulemerero.

< Pāvila 1. Vēstule Timotejam 3 >