< Psalmorum 94 >

1 psalmus David quarta sabbati Deus ultionum Dominus Deus ultionum libere egit
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 exaltare qui iudicas terram redde retributionem superbis
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 usquequo peccatores Domine usquequo peccatores gloriabuntur
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 effabuntur et loquentur iniquitatem loquentur omnes qui operantur iniustitiam
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 populum tuum Domine humiliaverunt et hereditatem tuam vexaverunt
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 viduam et advenam interfecerunt et pupillos occiderunt
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 et dixerunt non videbit Dominus nec intelleget Deus Iacob
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 intellegite qui insipientes estis in populo et stulti aliquando sapite
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 qui plantavit aurem non audiet aut qui finxit oculum non considerat
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 qui corripit gentes non arguet qui docet hominem scientiam
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Dominus scit cogitationes hominum quoniam vanae sunt
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 beatus homo quem tu erudieris Domine et de lege tua docueris eum
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 ut mitiges ei a diebus malis donec fodiatur peccatori fovea
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 quia non repellet Dominus plebem suam et hereditatem suam non derelinquet
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 quoadusque iustitia convertatur in iudicium et qui iuxta illam omnes qui recto sunt corde diapsalma
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 quis consurget mihi adversus malignantes aut quis stabit mecum adversus operantes iniquitatem
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 nisi quia Dominus adiuvit me paulo minus habitavit in inferno anima mea (questioned)
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 si dicebam motus est pes meus misericordia tua Domine adiuvabat me
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 secundum multitudinem dolorum meorum in corde meo consolationes tuae laetificaverunt animam meam
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 numquid aderit tibi sedis iniquitatis qui fingis dolorem in praecepto
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 captabunt in animam iusti et sanguinem innocentem condemnabunt
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 et factus est Dominus mihi in refugium et Deus meus in adiutorem spei meae
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 et reddet illis iniquitatem ipsorum et in malitia eorum disperdet eos disperdet illos Dominus Deus noster
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Psalmorum 94 >