< Psalmorum 66 >

1 in finem canticum psalmi resurrectionis iubilate Deo omnis terra
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
2 psalmum dicite nomini eius date gloriam laudi eius
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
3 dicite Deo quam terribilia sunt opera tua Domine in multitudine virtutis tuae mentientur tibi inimici tui
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
4 omnis terra adorent te et psallant tibi psalmum dicant nomini tuo diapsalma
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
5 venite et videte opera Dei terribilis in consiliis super filios hominum
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
6 qui convertit mare in aridam in flumine pertransibunt pede ibi laetabimur in ipso
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
7 qui dominatur in virtute sua in aeternum oculi eius super gentes respiciunt qui exasperant non exaltentur in semet ipsis diapsalma
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
8 benedicite gentes Deum nostrum et auditam facite vocem laudis eius
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
9 qui posuit animam meam ad vitam et non dedit in commotionem pedes meos
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
10 quoniam probasti nos Deus igne nos examinasti sicut examinatur argentum
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
11 induxisti nos in laqueum posuisti tribulationes in dorso nostro
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
12 inposuisti homines super capita nostra transivimus per ignem et aquam et eduxisti nos in refrigerium
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
13 introibo in domum tuam in holocaustis reddam tibi vota mea
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
14 quae distinxerunt labia mea et locutum est os meum in tribulatione mea
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
15 holocausta medullata offeram tibi cum incensu arietum offeram tibi boves cum hircis diapsalma
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
16 venite audite et narrabo omnes qui timetis Deum quanta fecit animae meae
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
17 ad ipsum ore meo clamavi et exaltavi sub lingua mea
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
18 iniquitatem si aspexi in corde meo non exaudiat Dominus
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
19 propterea exaudivit Deus adtendit voci deprecationis meae
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
20 benedictus Deus qui non amovit orationem meam et misericordiam suam a me
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< Psalmorum 66 >