< Proverbiorum 31 >

1 verba Lamuhel regis visio qua erudivit eum mater sua
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 quid dilecte mi quid dilecte uteri mei quid dilecte votorum meorum
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 ne dederis mulieribus substantiam tuam et vias tuas ad delendos reges
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 noli regibus o Lamuhel noli regibus dare vinum quia nullum secretum est ubi regnat ebrietas
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 ne forte bibat et obliviscatur iudiciorum et mutet causam filiorum pauperis
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 date siceram maerentibus et vinum his qui amaro sunt animo
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 bibant ut obliviscantur egestatis suae et doloris non recordentur amplius
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 aperi os tuum muto et causis omnium filiorum qui pertranseunt
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 aperi os tuum decerne quod iustum est et iudica inopem et pauperem
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 aleph mulierem fortem quis inveniet procul et de ultimis finibus pretium eius
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 beth confidit in ea cor viri sui et spoliis non indigebit
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 gimel reddet ei bonum et non malum omnibus diebus vitae suae
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 deleth quaesivit lanam et linum et operata est consilio manuum suarum
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 he facta est quasi navis institoris de longe portat panem suum
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 vav et de nocte surrexit deditque praedam domesticis suis et cibaria ancillis suis
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 zai consideravit agrum et emit eum de fructu manuum suarum plantavit vineam
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 heth accinxit fortitudine lumbos suos et roboravit brachium suum
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 teth gustavit quia bona est negotiatio eius non extinguetur in nocte lucerna illius
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 ioth manum suam misit ad fortia et digiti eius adprehenderunt fusum
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 caph manum suam aperuit inopi et palmas suas extendit ad pauperem
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 lameth non timebit domui suae a frigoribus nivis omnes enim domestici eius vestiti duplicibus
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 mem stragulam vestem fecit sibi byssus et purpura indumentum eius
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 nun nobilis in portis vir eius quando sederit cum senatoribus terrae
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 samech sindonem fecit et vendidit et cingulum tradidit Chananeo
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 ain fortitudo et decor indumentum eius et ridebit in die novissimo
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 phe os suum aperuit sapientiae et lex clementiae in lingua eius
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 sade considerat semitas domus suae et panem otiosa non comedet
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 coph surrexerunt filii eius et beatissimam praedicaverunt vir eius et laudavit eam
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 res multae filiae congregaverunt divitias tu supergressa es universas
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 sin fallax gratia et vana est pulchritudo mulier timens Dominum ipsa laudabitur
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 thau date ei de fructu manuum suarum et laudent eam in portis opera eius
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

< Proverbiorum 31 >