< Proverbiorum 29 >

1 viro qui corripientem dura cervice contemnit repentinus superveniet interitus et eum sanitas non sequitur
Munthu amene amawumitsabe khosi lake atadzudzulidwa kwambiri, adzawonongeka mwadzidzidzi popanda chomuchiritsa.
2 in multiplicatione iustorum laetabitur vulgus cum impii sumpserint principatum gemet populus
Anthu olungama akamalamulira mʼdziko anthu amakondwa, koma ngati dziko lilamulidwa ndi anthu oyipa mtima anthu amadandaula.
3 vir qui amat sapientiam laetificat patrem suum qui autem nutrit scorta perdet substantiam
Munthu amene amakonda nzeru amasangalatsa abambo ake, koma woyenda ndi akazi achiwerewere amasakaza chuma chake.
4 rex iustus erigit terram vir avarus destruet eam
Mfumu imalimbitsa dziko poweruza mwachilungamo, koma mfumu imene imawumiriza anthu kuti ayipatse mphatso imawononga dziko.
5 homo qui blandis fictisque sermonibus loquitur amico suo rete expandit gressibus eius
Munthu woshashalika mnzake, akudziyalira ukonde mapazi ake.
6 peccantem virum iniquum involvet laqueus et iustus laudabit atque gaudebit
Munthu woyipa amakodwa ndi machimo ake, koma wochita chilungamo amayimba lokoma.
7 novit iustus causam pauperum impius ignorat scientiam
Munthu wolungama amasamalira anthu osauka, koma woyipa salabadira zimenezi.
8 homines pestilentes dissipant civitatem sapientes avertunt furorem
Anthu onyoza atha kuwutsa ziwawa mu mzinda, koma anthu anzeru amaletsa ukali.
9 vir sapiens si cum stulto contenderit sive irascatur sive rideat non inveniet requiem
Ngati munthu wanzeru atsutsana ndi chitsiru, chitsirucho chimachita phokoso ndi kumangoseka ndipo sipakhala mtendere.
10 viri sanguinum oderunt simplicem iusti quaerunt animam eius
Anthu okhetsa magazi amadana ndi munthu wangwiro koma anthu olungama amasamalira moyo wake.
11 totum spiritum suum profert stultus sapiens differt et reservat in posterum
Munthu wopusa amaonetsa mkwiyo wake, koma munthu wanzeru amadzigwira.
12 princeps qui libenter audit verba mendacii omnes ministros habebit impios
Ngati wolamulira amvera zabodza, akuluakulu ake onse adzakhala oyipa.
13 pauper et creditor obviam fuerunt sibi utriusque inluminator est Dominus
Munthu wosauka ndi munthu wopondereza anzake amafanana pa kuti: Yehova ndiye anawapatsa maso onsewa.
14 rex qui iudicat in veritate pauperes thronus eius in aeternum firmabitur
Ngati mfumu iweruza osauka moyenera, mpando wake waufumu udzakhazikika nthawi zonse.
15 virga atque correptio tribuet sapientiam puer autem qui dimittitur voluntati suae confundet matrem suam
Ndodo ndi chidzudzulo zimapatsa nzeru koma mwana womulekerera amachititsa amayi ake manyazi.
16 in multiplicatione impiorum multiplicabuntur scelera et iusti ruinas eorum videbunt
Oyipa akamalamulira zoyipa zimachuluka, koma anthu olungama adzaona kugwa kwa anthu oyipawo.
17 erudi filium tuum et refrigerabit te et dabit delicias animae tuae
Umulange mwana wako ndipo adzakupatsa mtendere ndi kusangalatsa mtima wako.
18 cum prophetia defecerit dissipabitur populus qui custodit legem beatus est
Ngati uthenga wochokera kwa Yehova supezeka anthu amangochita zofuna zawo; koma wodala ndi amene amasunga malamulo.
19 servus verbis non potest erudiri quia quod dicis intellegit et respondere contemnit
Munthu wantchito sangalangizidwe ndi mawu okha basi; ngakhale awamvetse mawuwo sadzatha kuchitapo kanthu.
20 vidisti hominem velocem ad loquendum stulti magis speranda est quam illius correptio
Ngakhale munthu wa uchitsiru nʼkuti ndiponi popeza chikhulupiriro chilipo kuposa munthu wodziyesa yekha kuti ndi wanzeru poyankhula.
21 qui delicate a pueritia nutrit servum suum postea illum sentiet contumacem
Ngati munthu asasatitsa wantchito wake kuyambira ali mwana, potsirizira adzapeza kuti wantchitoyo wasanduka mlowachuma wake.
22 vir iracundus provocat rixas et qui ad indignandum facilis est erit ad peccata proclivior
Munthu wamkwiyo amayambitsa mikangano, ndipo munthu waukali amachita zolakwa zambiri.
23 superbum sequitur humilitas et humilem spiritu suscipiet gloria
Kunyada kwa munthu kudzamutsitsa, koma munthu wodzichepetsa amalandira ulemu.
24 qui cum fure partitur odit animam suam adiurantem audit et non indicat
Woyenda ndi munthu wakuba ndi mdani wa moyo wake womwe; amalumbira koma osawulula kanthu.
25 qui timet hominem cito corruet qui sperat in Domino sublevabitur
Kuopa munthu kudzakhala ngati msampha, koma aliyense amene amadalira Yehova adzatetezedwa.
26 multi requirunt faciem principis et a Domino iudicium egreditur singulorum
Anthu ambiri amafunitsitsa kuti wolamulira awakomere mtima, koma munthu amaweruzidwa mwachilungamo ndi thandizo la Yehova basi.
27 abominantur iusti virum impium et abominantur impii eos qui in recta sunt via
Anthu olungama amanyansidwa ndi anthu achinyengo; koma anthu oyipa amanyansidwa ndi anthu a mtima wowongoka.

< Proverbiorum 29 >