< Proverbiorum 26 >

1 quomodo nix aestate et pluvia in messe sic indecens est stulto gloria
Ngati chisanu choti mbee nthawi yachilimwe kapena mvula nthawi yokolola, ndi momwe zilili ndi ulemu wowulandira chitsiru.
2 sicut avis ad alia transvolans et passer quolibet vadens sic maledictum frustra prolatum in quempiam superveniet
Ngati timba wokhalira kuwuluka kapena namzeze wokhalira kuzungulirazungulira, ndi mmenenso limachitira temberero lopanda chifukwa, silichitika.
3 flagellum equo et camus asino et virga dorso inprudentium
Mkwapulo ndi wokwapulira kavalo, chitsulo ndi cha mʼkamwa mwa bulu, choncho ndodo ndi yoyenera ku msana wa chitsiru.
4 ne respondeas stulto iuxta stultitiam suam ne efficiaris ei similis
Usayankhe chitsiru monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti ungadzakhale ngati chitsirucho.
5 responde stulto iuxta stultitiam suam ne sibi sapiens esse videatur
Koma nthawi zina umuyankhe monga mwa uchitsiru wake, kuopa kuti angamadziyese yekha wanzeru.
6 claudus pedibus et iniquitatem bibens qui mittit verba per nuntium stultum
Kutuma chitsiru kuti akapereke uthenga kuli ngati kudzidula mapazi ndipo kumakuyitanira mavuto.
7 quomodo pulchras frustra habet claudus tibias sic indecens est in ore stultorum parabola
Monga miyendo ya munthu wolumala imene ilibe mphamvu ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
8 sicut qui mittit lapidem in acervum Mercurii ita qui tribuit insipienti honorem
Kupereka ulemu kwa chitsiru zili ngati kukulunga mwala mʼlegeni.
9 quomodo si spina nascatur in manu temulenti sic parabola in ore stultorum
Monga umachitira mtengo waminga wobaya mʼdzanja la chidakwa ndi mmene ulili mwambi mʼkamwa mwa chitsiru.
10 iudicium determinat causas et qui inponit stulto silentium iras mitigat
Munthu amene amalemba ntchito chitsiru chongoyendayenda, ali ngati woponya mivi amene angolasa anthu chilaselase.
11 sicut canis qui revertitur ad vomitum suum sic inprudens qui iterat stultitiam suam
Chitsiru chimene chimabwerezabwereza uchitsiru wake chili ngati galu amene amabwerera ku masanzi ake.
12 vidisti hominem sapientem sibi videri magis illo spem habebit stultus
Munthu wa uchitsiru aliko bwino popeza pali chiyembekezo kuposana ndi munthu amene amadziyesa yekha kuti ndi wanzeru.
13 dicit piger leaena in via leo in itineribus
Munthu waulesi amati, “Mu msewu muli mkango, mkango woopsa ukuyendayenda mʼmisewu!”
14 sicut ostium vertitur in cardine suo ita piger in lectulo suo
Monga chitseko chimapita uku ndi uku pa zolumikizira zake, momwemonso munthu waulesi amangotembenukatembenuka pa bedi lake.
15 abscondit piger manus sub ascellas suas et laborat si ad os suum eas converterit
Munthu waulesi akapisa dzanja lake mu mʼbale; zimamutopetsa kuti alifikitse pakamwa pake.
16 sapientior sibi piger videtur septem viris loquentibus sententias
Munthu waulesi amadziyesa yekha wanzeru kuposa anthu asanu ndi awiri amene amayankha mochenjera.
17 sicut qui adprehendit auribus canem sic qui transit et inpatiens commiscetur rixae alterius
Munthu wongolowera mikangano imene si yake ali ngati munthu wogwira makutu a galu wongodziyendera.
18 sicut noxius est qui mittit lanceas et sagittas et mortem
Monga munthu wamisala amene akuponya sakali zamoto kapena mivi yoopsa,
19 sic vir qui fraudulenter nocet amico suo et cum fuerit deprehensus dicit ludens feci
ndi momwe alili munthu wonamiza mnzake, amene amati, “Ndimangoseka chabe!”
20 cum defecerint ligna extinguetur ignis et susurrone subtracto iurgia conquiescunt
Pakasowa nkhuni, moto umazima; chomwechonso pakasowa anthu amiseche mkangano umatha.
21 sicut carbones ad prunam et ligna ad ignem sic homo iracundus suscitat rixas
Monga alili makala pa moto wonyeka kapena mmene zimachitira nkhuni pa moto, ndi mmene alili munthu wolongolola poyambitsa mikangano.
22 verba susurronis quasi simplicia et ipsa perveniunt ad intima ventris
Mawu a munthu wamiseche ali ngati chakudya chokoma; chimene chimatsikira mʼmimba mwa munthu.
23 quomodo si argento sordido ornare velis vas fictile sic labia tumentia cum pessimo corde sociata
Monga mmene chiziro chimakutira chiwiya chadothi ndi mmene mawu oshashalika amabisira mtima woyipa.
24 labiis suis intellegitur inimicus cum in corde tractaverit dolos
Munthu wachidani amayankhula zabwino pamene mu mtima mwake muli chinyengo.
25 quando submiserit vocem suam ne credideris ei quoniam septem nequitiae sunt in corde illius
Ngakhale wotereyu mawu ake ali okoma, koma usamukhulupirire, pakuti mu mtima mwake mwadzaza zonyansa.
26 qui operit odium fraudulenter revelabitur malitia eius in concilio
Ngakhale amabisa chidani mochenjera, koma kuyipa kwakeko kudzaonekera poyera pa gulu la anthu.
27 qui fodit foveam incidet in eam et qui volvit lapidem revertetur ad eum
Ngati munthu akumba dzenje, adzagweramo yekha; ngati munthu agubuduza mwala, udzamupsinja iye mwini.
28 lingua fallax non amat veritatem et os lubricum operatur ruinas
Munthu wonama amadana ndi amene anawapweteka, ndipo pakamwa poshashalika pamabweretsa chiwonongeko.

< Proverbiorum 26 >