< Proverbiorum 21 >

1 sicut divisiones aquarum ita cor regis in manu Domini quocumque voluerit inclinabit illud
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 omnis via viri recta sibi videtur adpendit autem corda Dominus
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 facere misericordiam et iudicium magis placent Domino quam victimae
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 exaltatio oculorum et dilatatio cordis lucerna impiorum peccatum
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 cogitationes robusti semper in abundantia omnis autem piger semper in egestate
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 qui congregat thesauros lingua mendacii vanus est et inpingetur ad laqueos mortis
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 rapinae impiorum detrahent eos quia noluerunt facere iudicium
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 perversa via viri aliena est qui autem mundus est rectum opus eius
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 melius est sedere in angulo domatis quam cum muliere litigiosa et in domo communi
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 anima impii desiderat malum non miserebitur proximo suo
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 multato pestilente sapientior erit parvulus et si sectetur sapientem sumet scientiam
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 excogitat iustus de domo impii ut detrahat impios in malum
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 qui obturat aurem suam ad clamorem pauperis et ipse clamabit et non exaudietur
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 munus absconditum extinguet iras et donum in sinu indignationem maximam
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 gaudium iusto est facere iudicium et pavor operantibus iniquitatem
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 vir qui erraverit a via doctrinae in coetu gigantum commorabitur
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 qui diligit epulas in egestate erit qui amat vinum et pinguia non ditabitur
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 pro iusto datur impius et pro rectis iniquus
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 melius est habitare in terra deserta quam cum muliere rixosa et iracunda
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 thesaurus desiderabilis et oleum in habitaculo iusti et inprudens homo dissipabit illud
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 qui sequitur iustitiam et misericordiam inveniet vitam et iustitiam et gloriam
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 civitatem fortium ascendit sapiens et destruxit robur fiduciae eius
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 qui custodit os suum et linguam suam custodit ab angustiis animam suam
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 superbus et arrogans vocatur indoctus qui in ira operatur superbiam
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 desideria occidunt pigrum noluerunt enim quicquam manus eius operari
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 tota die concupiscit et desiderat qui autem iustus est tribuet et non cessabit
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 hostiae impiorum abominabiles quia offeruntur ex scelere
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 testis mendax peribit vir oboediens loquitur victoriam
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 vir impius procaciter obfirmat vultum suum qui autem rectus est corrigit viam suam
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 non est sapientia non est prudentia non est consilium contra Dominum
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 equus paratur ad diem belli Dominus autem salutem tribuet
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Proverbiorum 21 >