< Job 8 >

1 Respondens autem Baldad Suhites, dixit:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Usquequo loqueris talia, et spiritus multiplex sermones oris tui?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Numquid Deus supplantat judicium? aut Omnipotens subvertit quod justum est?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Etiam si filii tui peccaverunt ei, et dimisit eos in manu iniquitatis suæ:
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 tu tamen si diluculo consurrexeris ad Deum, et Omnipotentem fueris deprecatus;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 si mundus et rectus incesseris: statim evigilabit ad te, et pacatum reddet habitaculum justitiæ tuæ,
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 in tantum ut si priora tua fuerint parva, et novissima tua multiplicentur nimis.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Interroga enim generationem pristinam, et diligenter investiga patrum memoriam
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (hesterni quippe sumus, et ignoramus, quoniam sicut umbra dies nostri sunt super terram),
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 et ipsi docebunt te, loquentur tibi, et de corde suo proferent eloquia.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Numquid vivere potest scirpus absque humore? aut crescere carectum sine aqua?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Cum adhuc sit in flore, nec carpatur manu, ante omnes herbas arescit.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Sic viæ omnium qui obliviscuntur Deum, et spes hypocritæ peribit.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Non ei placebit vecordia sua, et sicut tela aranearum fiducia ejus.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Innitetur super domum suam, et non stabit; fulciet eam, et non consurget.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Humectus videtur antequam veniat sol, et in ortu suo germen ejus egredietur.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Super acervum petrarum radices ejus densabuntur, et inter lapides commorabitur.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Si absorbuerit eum de loco suo, negabit eum, et dicet: Non novi te.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Hæc est enim lætitia viæ ejus, ut rursum de terra alii germinentur.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Deus non projiciet simplicem, nec porriget manum malignis,
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 donec impleatur risu os tuum, et labia tua jubilo.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Qui oderunt te induentur confusione, et tabernaculum impiorum non subsistet.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Job 8 >