< Psalmorum 6 >

1 In finem in carminibus, Psalmus David, pro octava. Domine, ne in furore tuo arguas me, neque in ira tua corripias me,
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
2 Miserere mei Domine quoniam infirmus sum: sana me Domine quoniam conturbata sunt ossa mea.
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
3 Et anima mea turbata est valde: sed tu Domine usquequo?
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
4 Convertere Domine, et eripe animam meam: salvum me fac propter misericordiam tuam,
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
5 Quoniam non est in morte qui memor sit tui: in inferno autem quis confitebitur tibi? (Sheol h7585)
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
6 Laboravi in gemitu meo, lavabo per singulas noctes lectum meum: lacrymis meis stratum meum rigabo.
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
7 Turbatus est a furore oculus meus: inveteravi inter omnes inimicos meos.
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
8 Discedite a me omnes qui operamini iniquitatem: quoniam exaudivit Dominus vocem fletus mei.
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
9 Exaudivit Dominus deprecationem meam, Dominus orationem meam suscepit.
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
10 Erubescant, et conturbentur vehementer omnes inimici mei: convertantur et erubescant valde velociter.
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< Psalmorum 6 >