< Psalmorum 104 >

1 Ipsi David. Benedic anima mea Domino: Domine Deus meus magnificatus es vehementer. Confessionem, et decorem induisti:
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga. Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri; mwavala ulemerero ndi ufumu.
2 amictus lumine sicut vestimento: Extendens cælum sicut pellem:
Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala; watambasula miyamba ngati tenti
3 qui tegis aquis superiora eius. Qui ponis nubem ascensum tuum: qui ambulas super pennas ventorum.
ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake. Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake, ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.
4 Qui facis angelos tuos, spiritus: et ministros tuos ignem urentem.
Amapanga mphepo kukhala amithenga ake, malawi amoto kukhala atumiki ake.
5 Qui fundasti terram super stabilitatem suam: non inclinabitur in sæculum sæculi.
Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake; silingasunthike.
6 Abyssus, sicut vestimentum, amictus eius: super montes stabunt aquæ.
Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala; madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.
7 Ab increpatione tua fugient: a voce tonitrui tui formidabunt.
Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa, pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;
8 Ascendunt montes: et descendunt campi in locum, quem fundasti eis.
Inu munamiza mapiri, iwo anatsikira ku zigwa kumalo kumene munawakonzera.
9 Terminum posuisti, quem non transgredientur: neque convertentur operire terram.
Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa, iwo sadzamizanso dziko lapansi.
10 Qui emittis fontes in convallibus: inter medium montium pertransibunt aquæ.
Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa; madziwo amayenda pakati pa mapiri.
11 Potabunt omnes bestiæ agri: expectabunt onagri in siti sua.
Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo; abulu akuthengo amapha ludzu lawo.
12 Super ea volucres cæli habitabunt: de medio petrarum dabunt voces.
Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi; zimayimba pakati pa thambo.
13 Rigans montes de superioribus suis: de fructu operum tuorum satiabitur terra:
Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba; dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.
14 Producens fœnum iumentis, et herbam servituti hominum: Ut educas panem de terra:
Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye, ndi zomera, kuti munthu azilima kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:
15 et vinum lætificet cor hominis: Ut exhilaret faciem in oleo: et panis cor hominis confirmet.
vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu, mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala, ndi buledi amene amapereka mphamvu.
16 Saturabuntur ligna campi, et cedri Libani, quas plantavit:
Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino, mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.
17 illic passeres nidificabunt. Herodii domus dux est eorum:
Mbalame zimamanga zisa zawo; kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.
18 montes excelsi cervis: petra refugium herinaciis.
Mapiri ataliatali ndi a mbalale; mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.
19 Fecit lunam in tempora: sol cognovit occasum suum.
Mwezi umasiyanitsa nyengo ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.
20 Posuisti tenebras, et facta est nox: in ipsa pertransibunt omnes bestiæ silvæ.
Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku, ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.
21 Catuli leonum rugientes, ut rapiant, et quærant a Deo escam sibi.
Mikango imabangula kufuna nyama, ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.
22 Ortus est sol, et congregati sunt: et in cubilibus suis collocabuntur.
Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala; imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.
23 Exibit homo ad opus suum: et ad operationem suam usque ad vesperum.
Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake, kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.
24 Quam magnificata sunt opera tua Domine! omnia in sapientia fecisti: impleta est terra possessione tua.
Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova! Munazipanga zonse mwanzeru, dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.
25 Hoc mare magnum, et spatiosum manibus: illic reptilia, quorum non est numerus. Animalia pusilla cum magnis:
Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala, yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka, zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.
26 illic naves pertransibunt. Draco iste, quem formasti ad illudendum ei:
Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku, ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.
27 omnia a te expectant ut des illis escam in tempore.
Zonsezi zimayangʼana kwa Inu kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.
28 Dante te illis, colligent: aperiente te manum tuam, omnia implebuntur bonitate.
Mukazipatsa, zimachisonkhanitsa pamodzi; mukatsekula dzanja lanu, izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.
29 Avertente autem te faciem, turbabuntur: auferes spiritum eorum, et deficient, et in pulverem suum revertentur.
Mukabisa nkhope yanu, izo zimachita mantha aakulu; mukachotsa mpweya wawo, zimafa ndi kubwerera ku fumbi.
30 Emittes Spiritum tuum, et creabuntur: et renovabis faciem terræ.
Mukatumiza mzimu wanu, izo zimalengedwa ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.
31 Sit gloria Domini in sæculum: lætabitur Dominus in operibus suis:
Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya; Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;
32 Qui respicit terram, et facit eam tremere: qui tangit montes, et fumigant.
Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera, amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.
33 Cantabo Domino in vita mea: psallam Deo meo quamdiu sum.
Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse; ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.
34 Iucundum sit ei eloquium meum: ego vero delectabor in Domino.
Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye, pamene ndikusangalala mwa Yehova.
35 Deficiant peccatores a terra, et iniqui ita ut non sint: benedic anima mea Domino.
Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi ndipo anthu oyipa asapezekenso. Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga. Tamandani Yehova.

< Psalmorum 104 >