< Nehemiah 5 >

1 In kutu pacl tok pus na sin mwet uh, mukul ac mutan, mutawauk in torkaskas lain mwet Jew wialos.
Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo.
2 Kutu selos fahk mu, “Arulana yohk sou lasr uh. Kut enenu wheat kut in mongo kac tuh kut in moul.”
Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”
3 Kutu pac selos fahk mu, “Kut kitala ima lasr, nien grape lasr, ac lohm sesr in eis wheat fal nu sesr tuh kut in tia misa ke masrinsral.”
Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”
4 Oasr pac kutu selos fahk, “Kut enenu in ngusr mani in akfalye tax lasr nu sin tokosra ke ima lasr ac nien grape lasr.
Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu.
5 Kut oana mwet Jew wiasr, srah sefanna. Tulik natusr uh oapana tulik natulos. A inge, kut oru tuh tulik natusr uh in mwet kohs. Kutu sin acn natusr uh kukakinyukla tari nu ke mwet kohs. A wangin ma kut ku in oru mweyen ima lasr ac nien grape lasr itukla liki kut.”
Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”
6 Ke nga lohng torkaskas lalos, nga kasrkusrak,
Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri.
7 ac nunkauk ma nga in oru kac. Na nga sang kas in kai nu sin mwet kol ac mwet pwapa lun mwet uh ac fahk, “Kowos akkeokye mwet wiowos sifacna ke kowos eis ma laesla yohk liki ma fal.” Nga pangon sie tukeni lulap nu sin mwet uh, in pwapa ke elya se inge.
Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu
8 Na nga fahk, “Ke kuiyasr nufon kut tuh molela mwet Jew wiasr su tuh sifacna kukakunulosla nu sin mwetsac. A inge kowos oru tuh mwet na wiowos in kukakunulosla sifacna nu suwos, mwet Jew.” Ouinge wanginna ma mwet kol elos ku in fahk, na elos tia kas.
ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.
9 Na nga fahk, “Ma kowos oru an tia wo! Kowos enenu in akos God ac oru ma suwohs. Fin ouinge, kowos fah tia oru kutena sripa tuh mwet lokoalok lasr, mwet pegan, in ku in akkolukye kut.
Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi?
10 Nga lela nu sin mwet uh elos in ngusr mani ac mwe mongo sik, na mwet wiyu ac mwet orekma luk elos oru oana nga oru. Inge lela kut nukewa in sisla eisyen ma laesla selos.
Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja!
11 Sisla soemoul nukewa lalos nu suwos: finne mani, ku wheat, ku wain, ku oil in olive. Mesinge kowos in folokonang nu selos ima lalos, nien grape lalos, insak olive, ac lohm selos!”
Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”
12 Mwet kol elos topuk, “Kut ac oru oana ma kom fahk. Kut ac folokonang ma lalos, ac kut ac tia eis soemoul lalos.” Nga pangoneni mwet tol, ac sap tuh mwet kol in oru fulahk lalos ye mutalos tuh elos fah oru oana ma elos wulela kac inge.
Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.” Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo.
13 Na nga sarukla mwe lohl liki infulwuk, ac osrokla ac fahk, “God El fah osrokla kutena suwos su ac tia karingin wulela la, oana ma kowos liye nga oru inge. God El fah eisla lohm suwos ac ma lowos nukewa, ac tia filiya kutena ma nu suwos.” Mwet nukewa su wi tukeni sac fahk, “Amen!” ac kaksakin LEUM GOD. Ac mwet kol elos karinganangna wuleang lalos.
Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!” Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.
14 In yac singoul luo ke nga governor lun acn Judah, mutawauk ke yac aklongoul nwe ke yac se aktolngoul luo ma Artaxerxes el tokosra fulat, nga ac sou luk tiana eis kitakat ke mwe mongo su fal nu sin sie governor in eis.
Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa.
15 Governor nukewa meet likiyu, elos sang sap toasr nu sin mwet uh tuh elos in akfalye ipin silver angngaul ke len se, nu ke mwe mongo ac wain. Finne mwet kulansap lun governor, elos oayapa oru upa nu sin mwet uh. Tusruktu nga oru siena, mweyen nga akfulatye God.
Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu.
16 Nga sang kuiyuk nufon in sifil musai pot uh, ac tia suk in eis kutena acn nu sik sifacna. Mwet kulansap luk nukewa elos wi pac orekma ke musa uh.
Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.
17 Len nukewa mwet Jew siofok lumngaul wi mwet kol lalos elos mongo ke tepu luk, sayen pacna mwet su tuku liki mutunfacl ma apinkutla.
Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150.
18 Kais sie len nga srukak cow soko, sheep na wowo onkosr, ac won na pus, ac len singoul nukewa nga srukak pac wain sasu nimen mwet uh. Tuh ke sripen nga etu lah toasr ma mwet uh enenu in akfalye, oru nga tiana suk ke ma fal nga in eis ke wal lun governor.
Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.
19 Nga siyuk sum, O God, tuh kom in esamyu ac akinsewowoyeyu ke ma nukewa ma nga oru nu sin mwet inge.
Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.

< Nehemiah 5 >