< Leviticus 20 >

1 LEUM GOD El fahk nu sel Moses
Yehova anawuza Mose kuti,
2 elan fahkang nu sin mwet Israel, “Kutena suwos, ku kutena mwetsac su muta inmasrlowos, su asang tulik natu in kisakinyukla nu sin god Molech, ac fah tatngal el sin mwet in acn se inge nufon nwe ke el misa.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala.
3 Kutena mwet su sang sie sin tulik natul nu sel Molech ac oru tuh Lohm Nuknuk Mutal sik in fohkfokla ac aklusrongtenye Ine mutal luk, nga fah lainul, ac tia sifil oekul mu el sie sin mwet luk.
Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera.
4 Tusruktu mwet in acn sac fin pilesru ma mwet sac orala uh ac tia unilya,
Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha,
5 nga ac fah sifacna forang lainul, ac sou lal nufon, ac mwet nukewa ma welul in tia inse pwaye nu sik a elos alu nu sel Molech. Nga fah tia sifilpa oakalos mu elos mwet luk.
Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”
6 “Fin oasr kutena mwet ma forla ac suk kasru sin mwet su sramsram nu sin ngun fohkfok, nga fah forang lainul ac tia sifilpa oakal mu el sie sin mwet luk.
“‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.
7 Sifacna liyekowosyang tuh kowos in mutal, tuh nga pa LEUM GOD lowos.
“‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
8 Akos ma sap luk, mweyen nga LEUM GOD lowos, su akmutalyekowosla.”
Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.
9 LEUM GOD El sang pac oakwuk ten inge nu selos. Kutena mwet su selngawi papa tumal ku nina kial fah anwuki. El sifacna pa sang mwatan misa lal.
“‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.
10 Sie mwet fin orek kosro nu sin mutan kien sie pac mwet Israel, kewana mukul se ac mutan se ma orek kosro fah anwuki.
“‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.
11 Sie mukul su orek kosro nu sin sie sin mutan kien papa tumal, el akmwekinye papa tumal, ke ma inge mukul sac ac mutan sac kewa ac fah anwuki. Eltal na pa sifacna oru in anwuki eltal.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.
12 Mukul se fin kosro nu sin mutan kien sie sie wen natul, el ac mutan sac kewa fah anwuki. Eltal oru ouiya na koluk se, ac sifacna pwanang in anwuki eltal.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
13 Mukul se fin orek inkanek in kosro nu sin sie pac mukul, eltal orala sie ouiya ma arulana srungayuk. Ke ma inge, ac fah anwuki eltal. Eltal sifacna pwanang in anwuki eltal.
“‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
14 Sie mukul fin payukyak sin sie mutan ac oayapa nina kien mutan sac, eltal kewa fah isisyak in misa, ke sripen lumah na koluk se ma eltal orala uh. Kain ouiya se inge fah tia filfilla in orek inmasrlowos.
“‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.
15 Mukul se fin orek kosro nu sin soko ma orakrak, mukul sac ac ma orakrak soko an fah anwuki.
“‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.
16 Mutan se fin suk inkanek in orek kosro nu sin soko ma orakrak, mutan sac ac kosro soko ah kewa ac fah anwuki. Ma na eltal oru pa misa laltal.
“‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.
17 Mukul se fin payukyak sin tamtael se lal, ku nu sin acn se nutin papa tumal ku nina kial saya, na eltal fah akmwekinyeyuk ye mutun mwet uh, ac lillilla liki acn mwet uh muta we. El orek kosro nu sin ma loul, ouinge ac fah kaiyuk el oana ma fal in orek nu sel.
“‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.
18 Mukul se fin orek kosro nu sin sie mutan ke pacl mutan sac el mas mutan, eltal kewa fah lisyukla liki inmasrlon mwet uh, mweyen eltal kunausla oakwuk ke ma su tia nasnas.
“‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.
19 Mukul se fin orek kosro nu sin sie sin mutan wien papa tumal ku mutan wien nina kial, eltal na kewa fah eis kaiyuk ma fal in orek nu seltal ke sripen pukasr laltal uh.
“‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.
20 Mukul se fin orek kosro nu sin mutan kien tamulel lun papa tumal ku nina kial, el akmwekinye tamulel sac. Ke ma inge el ac mutan sac fah eis mwata kac; kewana seltal ac fah wangin tulik natu.
“‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.
21 Mukul se fin eisla mutan kien tamulel lal, eltal kewa ac fah wangin tulik natultal. El orala sie ma na tia nasnas, ac akmwekinyala tamulel lal.
“‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.
22 LEUM GOD El fahk, “Liyaung ma sap luk ac oakwuk luk nukewa, tuh acn Canaan su nga ac us kowos nu we fah tia siskowosla.
“‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni.
23 Nimet oru facsin lun mwet su muta we. Nga ac lusak mwet pegan liki acn we tuh kowos fah ku in utyak nu we. Nga arulana kwase ouiya koluk lalos.
Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo.
24 Tusruktu nga wuleot tari nu suwos ke facl se inge, sie acn mut ac kasrup fohk we, tuh in ma lowos, ac nga fah sot nu suwos. Nga LEUM GOD lowos, ac nga srikowosla tari liki inmasrlon mutunfacl nukewa saya.
Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.
25 Ke ma inge, kowos fah arulana oru in kalem inmasrlon kosro ac won ma nasnas ac ma su tia nasnas. Nimet kowos kang kosro ku won ma nga akkalemye tari mu tia nasnas. Kowos fin kang ma inge, na ac oru kowos tia nasnas.
“‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu.
26 Kowos fah mutal ac fah ma luk mukena, mweyen nga LEUM GOD, ac nga mutal. Nga srikowosla liki mutunfacl saya tuh kowos fah ma luk mukena.
Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.
27 “Kutena mukul ku mutan su sramsram nu sin ngunin mwet misa ac fah tatngal el nwe ke el misa; ac kutena mwet su oru ouinge uh, el sifacna oru elan misa.”
“‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’”

< Leviticus 20 >