< Ezekiel 30 >

1 LEUM GOD El sifil kaskas nu sik ac fahk,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Mwet sukawil moul la, palye ac fahkak kas su nga, LEUM GOD Fulatlana, fahk inge. Kom in wowoyak ac fahk kas inge: Sie len aksangeng summa!
“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena. “‘Ufuwule mawu awa akuti, ‘Kalanga, tsiku lafika!’
3 Len sac apkuranme, len se ma LEUM GOD El ac mukuila, Sie len lohsrlosr ke pukunyeng, ac len in lokoalok nu sin mutunfacl uh.
Pakuti tsiku layandikira, tsiku la Yehova lili pafupi, tsiku la mitambo yakuda, tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.
4 Ac fah oasr mweun in facl Egypt Ac ongoiya lulap in acn Ethiopia. Mwet puspis in acn Egypt ac fah anwuki. Facl sac ac fah kunausyukla Ac ma nukewa we fah musalla.
Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto ndipo mavuto adzafika pa Kusi. Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto, chuma chake chidzatengedwa ndipo maziko ake adzagumuka.
5 “Mwet mweun nukewa ma utuku liki acn Ethiopia, Libya, Lydia, Arabia, Kub, ac oayapa liki inmasrlon mwet luk sifacna, ac fah misa ke mweun sac.”
Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.
6 LEUM GOD El fahk, “Liki acn Migdol layen epang, nwe in acn Aswan layen eir, mwet nukewa ma loango acn Egypt ac fah anwuki ke mweun uh. Un mwet mweun watwen lun acn Egypt ac fah kunausyukla. Nga, LEUM GOD Fulatlana, pa fahk ma inge.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: “‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu. Adzaphedwa ndi lupanga kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’” ndikutero Ine Ambuye Yehova.
7 Facl sac ac fah arulana sikiyukla yohk liki acn nukewa faclu, ac siti we uh ac fah oan arulana musalsalu.
“‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja kupambana mabwinja ena onse opasuka, ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka kupambana mizinda ina yonse.
8 Ke nga ac esukak acn Egypt, ac mwet loango acn we nukewa misa uh, na elos ac fah etu lah nga pa LEUM GOD.
Nditatha kutentha Igupto ndi kupha onse omuthandiza, pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
9 “Ke len se ma kunanula acn Egypt, nga ac fah supwala mwet utuk kas in oayak som nu Ethiopia, in okasak mwet we su tiana etu ke ma sikyak inge, ac elos ac fah arulana tuninfongla. Len sacn akuranna tuku!”
“‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.
10 LEUM GOD Fulatlana El fahk, “Nga ac fah orekmakunul Tokosra Nebuchadnezzar lun acn Babylonia in tulokinya mwe kasrup lun Egypt.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.
11 El, ac mwet mweun sulallal lal, ac fah tuku ac sukela acn we. Elos ac fah mweuni acn Egypt ke cutlass, na facl sac ac fah sessesla ke monin mwet misa.
Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja adzabwera kudzawononga dzikolo. Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.
12 Nga ac fah oru Infacl Nile in paola, ac sang facl Egypt nu inpoun mwet koluk. Mwet in mutunfacl saya ac fah arulana kunausla acn we nufon. Nga, LEUM GOD, pa fahk ma inge.”
Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa. Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo. Ine Yehova ndayankhula.
13 Na LEUM GOD Fulatlana El fahk, “Nga ac fah kunausla ma sruloala ac god lusrongten nukewa in acn Memphis. Ac fah wangin mwet in leumi acn Egypt, ac nga fah oru tuh mwet nukewa in arulana sangeng.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Ndidzawononga mafano ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi. Simudzakhalanso mfumu mu Igupto, ndipo ndidzaopseza dziko lonse.
14 Nga ac oru tuh siti Pathros layen eir in Egypt in sikiyukla, ac esukak siti Zoan layen epang. Nga ac fah kalyei Thebes, capital lun acn we.
Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi, ndi kutentha mzinda wa Zowani. Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.
15 Nga ac fah oru tuh Pelusium, su potiyukyak arulana ku, in pula kasrkusrak luk. Nga fah kunausla un mwet mweun lun acn Thebes.
Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu, linga lolimba la Igupto, ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.
16 Nga fah esukak acn Egypt, ac siti Pelusium ac fah muta in keok lulap. Pot lun acn Thebes ac fah kunausyukla, ac siti uh ac fah sronoti.
Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto; Peluziumu adzazunzika ndi ululu. Malinga a Thebesi adzagumuka, ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.
17 Mukul fusr in siti Heliopolis ac Bubastis ac fah misa ke mweun, ac mwet saya ac fah sruoh ac muta in kapir.
Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti adzaphedwa ndi lupanga ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.
18 Lohsr lulap ac fah putati nu fin Tahpanhes ke nga ac kunausla ku lun acn Egypt ac aksafyela ku se ma elos konkin kac. Sie pukunyeng ac fah afinya facl Egypt, ac mwet in siti nukewa we ac fah sruoh ac muta in kapir.
Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima pamene ndidzathyola goli la Igupto; motero kunyada kwake kudzatha. Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda, ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.
19 Ke nga ac kalyei acn Egypt in lumah se inge, elos ac fah etu lah nga pa LEUM GOD.”
Kotero ndidzalanga dziko la Igupto, ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”
20 Ke len akitkosr in malem se meet ke yac aksingoul sie in sruoh lasr, LEUM GOD El kaskas nu sik ac fahk,
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
21 “Mwet sukawil, nga koteya poun tokosra lun Egypt. Wanginna mwet kapriya ku lohsak in mahla tuh elan ku in sifil sruok cutlass natul.
“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga.
22 Na pa inge ma nga, LEUM GOD Fulatlana, ac fahk uh: Nga lainul tokosra lun Egypt. Nga ac fah kotalik paol kewa — lacpo ma srakna wo, ac layen ma musalla tari — na cutlass natul ac fah putatla liki paol.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake.
23 Nga ac fah akfahsryelik mwet Egypt nu fin faclu nufon.
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri.
24 Na nga ac fah akkeye poun tokosra lun Babylonia, ac sang nu inpaol cutlass nutik uh. Tusruktu nga ac koteya poun tokosra lun Egypt, ac el ac fah sasao ac misa ye mutun mwet lokoalok lal.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo.
25 Aok, nga fah akmunasyal, ac akkeye tokosra lun Babylonia. Ke nga ac sang cutlass nutik uh nu sel ac el kolla nu facl Egypt, mwet nukewa ac fah etu lah nga pa LEUM GOD.
Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto.
26 Nga ac akfahsryelik mwet Egypt nu fin faclu nufon. Na elos ac fah etu lah nga pa LEUM GOD.”
Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiel 30 >