< Luo Tokosra 12 >

1 In yac akitkosr ke pacl Jehu el tokosra lun acn Israel, Joash el tokosra lun Judah, ac el leum in Jerusalem ke yac angngaul. Nina kial pa Zibiah, sie mutan ke siti Beersheba.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri cha Yehu, Yowasi anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka makumi anayi. Amayi ake anali Zibiya wa ku Beeriseba.
2 In moul lal nufon el oru ma LEUM GOD El insewowo kac mweyen mwet tol Jehoiada el lotel.
Yowasi anachita zolungama pamaso pa Yehova masiku onse amene wansembe Yehoyada ankamulangiza.
3 Tusruktu tiana kunausyukla nien alu lun mwet pegan, ac mwet uh srakna orek kisa ac akosak mwe keng we.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo opembedzerako mafanowo.
4 Joash el pangoneni mwet tol ac sap elos in liyaung na mani ma orekeni ke pacl in kisa ke Tempul, kewana mani ma pakpuki nu ke kisa, ac mani ma mwet uh sang ke insewowo.
Yowasi anati kwa ansembe, “Tolerani ndalama zonse zimene zimaperekedwa monga chopereka chopatulika ku Nyumba ya Yehova, ndalama zonse zamsonkho wa munthu aliyense, ndalama zomwe munthu amapereka akalonjeza ndiponso ndalama zimene munthu amapereka mwaufulu ku Nyumba ya Yehova.
5 Ma kunen kais sie mwet tol in liyaung mani ma orekeni sin mwet el karingin. Mani inge ma ac orekmakinyuk nu ke akwoyeyen acn musalla ke Tempul, ke pacl eneneyuk uh.
Wansembe aliyense alandire ndalamazo kuchokera kwa abwenzi ake, ndipo zigwiritsidwe ntchito yokonzera chilichonse chimene chipezeke kuti ndi chowonongeka mʼnyumbayo.”
6 Tusruktu ke yac aklongoul tolu ke pacl in leum lal Joash, mwet tol ah soenna orala kutu orekma in akwoyela acn musalla ke Tempul.
Koma pofika chaka cha 23 cha ufumu wa Yowasi, ansembewo anali asanakonze nyumbayo.
7 Ouinge Joash el pangnol Jehoiada ac mwet tol sayal ac siyuk selos, “Efu ku kowos tiana akwoye acn musalla ke Tempul uh? Ingela, kowos fah tia sifil liyaung mani kowos orani uh. Use in sang akwoyela Tempul.”
Choncho Mfumu Yowasi inayitanitsa wansembe Yehoyada ndi ansembe ena ndipo inafunsa kuti, “Chifukwa chiyani simukukonza malo owonongeka a mʼnyumbayi? Musasungenso ndalama zina zochokera kwa abwenzi anu, koma muzipereke kuti akonzere nyumbayi.”
8 Mwet tol elos insese in tia sifil sruok mani uh, ac elos insese pac tuh elos ac tia mukuikui ke akwoye Tempul uh.
Ansembe anavomera kuti salandiranso ndalama kuchokera kwa anthu ndipo kuti sindiwo amene ati akonzenso nyumbayo.
9 Na Jehoiada el eis box se ac orala pat se ke kafa ah, ac likiya pe loang se ma oan ke layen layot ke mwet uh ac utyak nu in Tempul uh. Mwet tol su orekma ke mutunoa uh ac sang mani nukewa ma orekeni sin mwet alu uh nu in box se inge.
Koma wansembe Yehoyada anatenga bokosi ndipo anabowola chivundikiro chake. Anayika bokosilo pambali pa guwa lansembe, kudzanja lamanja la aliyense amene akulowa mʼNyumba ya Yehovayo. Ansembe amene ankalondera pa khomopo ankaponya mʼbokosi ndalama zonse zimene ankabwera nazo ku nyumba ya Yehova.
10 Pacl nukewa ma ac yohk mani orekeni nu in box sac, na mwet sim lun tokosra ac mwet Tol Fulat ac tuku ac munanla silver uh in kofelik, ac pauniya.
Nthawi zonse akaona kuti mʼbokosimo muli ndalama zambiri, mlembi wa mfumu ndi mkulu wa ansembe ankabwera ndipo ankawerenga ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku Nyumba ya Yehova ndi kuziyika mʼmatumba.
11 Tukun elos simusla lupan mani silver inge, na ac itukyang nu sin mwet ma kol orekma ke Tempul an, ac ma inge ac sang moli kamtu, mwet musa,
Ankati akadziwa kuti ndalamazo zilipo zingati, ankazipereka kwa anthu amene ankayangʼanira ntchito yokonza nyumbayo. Ndalamazo ankalipira anthu amene ankagwira ntchito yokonza Nyumba ya Yehova, amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba,
12 mwet akmusra, mwet tufahl eot, ac molela sak ac eot ma orekmakinyuk, ac in moli ma nukewa ma eneneyuk saya.
amisiri a miyala ndiponso anthu ophwanya miyala. Iwo ankagula matabwa ndi miyala yosema yokonzera Nyumba ya Yehova ndipo ankalipira zinthu zonse zofunika pokonzanso nyumbayo.
13 Tusruktu mani inge tia orekmakinyuk in sang moli mwet orek cup silver, pol, mwe ukuk, ku kufwa in akwoye lam, ku kutena kain ma orek ke silver ku gold.
Koma ndalama zomwe anthu ankabwera nazo ku nyumbayo sanagulire siliva wopangira mabeseni, zozimitsira nyale, mbale zowazira magazi, malipenga kapena ziwiya zina zilizonse zagolide kapena zasiliva za ku Nyumba ya Yehova.
14 Orekmakinyukla nufon in moli mwet orekma, ac in moli kufwa nu ke akwoye lohm.
Ndalamazi anazipereka kwa anthu antchito amene anazigwiritsa ntchito yokonzera nyumbayo.
15 Mwet karingin orekma uh elos arulana suwohs ke orekma lalos, pwanang tia eneneyuk elos in akpwayei ouiyen orekma lalos ke mani.
Koma sanawafunse kuti afotokoze kagwiritsidwe ntchito ka ndalama zolipira amene ankagwira ntchito, chifukwa anthuwo ankagwira ntchitoyo mokhulupirika kwambiri.
16 Mani ma orekeni ke mwe kisa in akfalye ma koluk lukma, ku mwe kisa ke ma koluk, tia wi itukyang nu in box sac, mweyen ma inge ma lun mwet tol.
Ndalama zomwe zinkaperekedwa pa nsembe yopepesera machimo ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo sanabwere nazo ku Nyumba ya Yehova pakuti zinali za ansembe.
17 In pacl sac, Tokosra Hazael lun Syria el mweuni siti Gath ac eisla acn we, na el wotela mu el ac mweuni pac acn Jerusalem.
Pa nthawi imeneyo, Hazaeli, mfumu ya Aramu anapita kukathira nkhondo mzinda wa Gati nawulanda. Kenaka Hazaeli anatembenuka kupita kukathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu.
18 Tokosra Joash lun Judah el orani mani in kisa nukewa ma tuh orekeni ac kisaiyukla nu sin LEUM GOD sel Jehoshaphat, Jehoram, ac Ahaziah, su tokosra meet lukel, ac sang ma inge weang mwe sang lal sifacna wi gold nukewa ma oan in nien fwil mwe kasrup in Tempul ac in lohm sin tokosra, ac supwala nufon ma inge in mwe lung nu sel Tokosra Hazael. Na Hazael el us mwet mweun lal ac som liki acn Jerusalem.
Koma Yowasi mfumu ya Yuda anatenga zinthu zonse zopatulika zomwe anazipatula Yehosafati, Yehoramu, ndi Ahaziya abambo ake, mafumu a Yuda ndi mphatso zonse zomwe iye mwini anazipereka: golide yense amene anapezeka mʼnyumba yosungiramo chuma cha mʼnyumba ya Yehova ndi zomwe zinali mʼnyumba ya mfumu, nazipereka kwa Hazaeli mfumu ya Aramu. Pamenepo iye anachoka ku Yerusalemuko.
19 Ma nukewa saya ma Tokosra Joash el orala simla oasr in [Sramsram Matu Ke Tokosra Lun Judah].
Ndipo ntchito zina za Yowasi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
20 Mwet pwapa lal Joash elos orala pwapa lukma lalos ac unilya ke lohm se ke acn koaneyukla kutulap in Jerusalem ke inkanek soko ma oatula nu Silla.
Akuluakulu ake anamuchitira chiwembu ndi kumupha ku Beti Milo, pa njira yotsikira ku Silo.
21 Jozacar wen natul Shimeath, ac Jehozabad wen natul Shomer, pa sringlilya el misa. Joash el pukpuki inkulyuk lun tokosra in Siti sel David, ac Amaziah wen natul, el aolul in tokosra.
Yozakara mwana wa Simeati ndi Yehozabadi mwana wa Someri atumiki ake anamukantha nafa. Ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Amaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Luo Tokosra 12 >