< Ufunuo 3 >

1 Khusuhwa uvamupelela unghwa mu salidi simba: 'Amemenyu ngha ula uvei ibateilile imepo lekhela khumo incha Nguluve ni nondwe lekhela khumo.” Neikhi manyile khila eikhyuvombile. Avanu vikhukhunghinia ukhuta uleimwumivu humbe u-fwile.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Sarde kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene amasunga mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu ndi nyenyezi zisanu ndi ziwiri. Iye akuti: Ndimadziwa ntchito zako; umadziwika kuti ndiwe wamoyo koma ndiwe wakufa.
2 Sisimukha uvei miho vweidulusye panghala anghasinghiile, pu leino nghaleipipi ukhufwa, pakhuva saneinchiwene imbombo nchakho ukhuta nchinonghelanile pamiho ngha Nguluve.
Dzuka! Limbitsa zimene zatsalira zomwe zatsala pangʼono kufa, pakuti ndaona kuti ntchito zako nʼzosakwanira pamaso pa Mulungu.
3 Pu leino kumbuheincha nchila unchvwa upile nukhupuleikha. Unchikonge. Mukhupela uvuvivi, puleino ungave savusisimukha nukhuva miho pu une nikhiwincha ndu munu undyasi, pu sukhalumanye akhavalelo ukhuyakhiva nikhwincha pa lyulve.
Choncho, kumbukira zimene unalandira ndi kumva; uzisunge ndipo ulape. Koma ngati sudzuka, ndidzabwera ngati mbala ndipo sudzadziwa nthawi imene ndidzabwere kwanu.
4 Pu leino khulei matavwa madebe ngha vanu ava mu Salidi vavo savalaminche eimyenda nghyovo vuvinghendangha paninie nune vuvafwalile eimyenda eimivalafu swe, pakhuva vanonghile.
Komabe uli ndi anthu angapo mu Sarde amene sanadetse zovala zawo. Amenewa adzayenda ndi Ine atavala zoyera popeza ndi oyenera kutero.
5 Ula uvei iva nduti punikhei kungangha eilitavwa lya mwene pavulongolo pa Daada vango, na pavasuhwa.
Amene adzapambane adzavala zoyera ngati ena aja. Sindidzafafaniza dzina lake mʼbuku lamoyo, koma ndidzamuchitira umboni pamaso pa Atate anga ndi angelo ake.
6 Uvei angave alei ni mbulukhutu apuleikhanghe eilimenyu eilei, eiyu u mepo ikhungheivula eimipelela.”
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”
7 Khusuhwa uvamupelela unghwa mu Filidefia simba: Amamenyu ngha ula ungholofu nuvwayeilweli, uvei alei neikhedeinduleilo khya Davitei, pu usikhuli u yunge uva khudeindula. Lola pupaleindyango udeindule neikhupile pu asikhuli unyakhudeinda.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Filadefiya kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa amene ndi woyera ndi woonadi, amene ali ndi kiyi ya Davide. Iye akatsekula palibe amene angatseke; ndipo akatseka palibe amene angatsekule.
8 Neilumanyile ulei nangho amakha madebe, pu eilimenyu lyango uleiveikhile munumbula yakho.
Iye akuti, ‘Ine ndimadziwa ntchito zako. Taona, ndakutsekulira pa khomo ndipo palibe wina amene angatseke. Ndikudziwa kuti uli ndi mphamvu zochepa komabe wasunga mawu anga ndipo sunandikane.
9 Lola! Punikhukhupa avange avandu lundamano lwa setano, vala aviita avene va Yuta humbe sava Yuta, pu vikhuvasyova avanu, lola vuyanikhuvumeileincha ukhuta vinchanghe pakhusona pamalunde nghakho. Puyavikhulumanya ukhuta niakhunghanile.
Amene ndi mpingo wa Satana, amene amadzitcha kuti ndi Ayuda pamene sali choncho, koma ndi onama, ndidzawabweretsa kwa inu ndi kuwagwetsa pansi pa mapazi anu kuti adzazindikire kuti ndimakukondani.
10 Ulwakhuva ulibiite eilimenyu lyango, nuvukifu pakhwiyumeileincha mulimenyu. Pu na yune nikhukhu lolelangha nukhukhyuvateila pa seikhei unghwa khungheliwa
Popeza mwasunga mawu anga woti mupirire ndipo mwawugwira mtima, Inenso ndidzakupulumutsani nthawi ya mayesero imene idzabwera pa dziko lonse lapansi kuyesa onse okhala pa dziko lapansi.
11 pakhuva nghukhwincha pakheilunga khyoni, khukhuva nghela vala vooni vavo valei mukheilunga.
Ine ndikubwera msanga. Gwiritsitsa chimene uli nacho kuti wina angakulande chipewa chako chaufumu.
12 Ula uvei iva induti punikhupe langha ukhuta avenchanghe mbanda va nyumba imbalanche eiya Nguluve, pusalahuma khunji lusikhu. Punikhu leisimba eilitavwa lya Nguluve vango, eilitavwa lya vunvhenge vwa Nguluve vango, “Uvunchenge uvwa (Yerusalemu umpya, uvunchenge uvukhwikha pasi ukhuhuma khulyanya kihwa Nguluve vango), neilitavwa lyango eilipya.
Iye amene adzapambane ndidzamusandutsa mzati wa mʼNyumba ya Mulungu wanga. Sadzatulukamonso. Pa iye ndidzalemba dzina la Mulungu wanga ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, Yerusalemu watsopano, umene ukubwera pansi kuchokera kumwamba kwa Mulungu wanga; ndipo pa iye ndidzalembanso dzina langa latsopano.
13 Ula uvei alei nimbulukhutu aleipuleikhe eilimenyu eilei eilyu u mepo ukhungheivula eimipelela.'
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.’”
14 “Khu suhwa uva mupelela unghulei khu Leokadia simba: 'Amamenyu ngha mwene nghango Amina, vuvule uvei vakhuhuveilivwa hange intangeili ungholofu, umbaha nuvulongonchi vwa fyoni ifipeliwe nu Nguluve.
“Lembera mngelo wampingo wa ku Laodikaya kuti: Awa ndi mawu ochokera kwa Ameni, mboni yokhulupirika ndi yoona, gwero la zolengedwa zonse za Mulungu.
15 Neinchimanyile imbombo nchakho ukhuta uve saleinchinchimu hange suleipyufu, pu yale yiva huba uve nchinchimu avyo uve pyufu!
Ine ndimadziwa ntchito zako, kuti sindiwe wozizira kapena wotentha. Ndikanakonda ukanakhala wozizira kapena wotentha!
16 Leino ulwakhuva uve uvufukhefu uleifukhefu na vuvunchinchimu uleinchinchimu pusunonghile palyune leino punikhukhubeha mundomo nghwango unghu.
Tsono popeza ndiwe wofunda chabe, sindiwe wotentha kapena wozizira, ndatsala pangʼono kuti ndikulavule mʼkamwa mwanga.
17 Ulwakhuva vwiita, “Une neileikavi, neileineikhyuma khyukhingi pasanileinuvufumbwe vwa khunonghwa kheininie.” Pu leino sulumanyile ukhuta uve ulei nghanchu fincho yuve vusanghania, nulei nghanchu sawilola ubofwile amiho uleivubwinda.
Iwe umati: ‘Ndine wolemera, ndine wachuma ndipo sindisowa kanthu.’ Koma sudziwa kuti ndiwe wovutika, womvetsa chisoni, waumphawi, wosaona ndi wamaliseche.
18 Punikhukhutanga amasangho unghule khulyune ulutalama ulunonchivwe nu mwoto ukhuta puve ikavi, unya myenda eimivalafu einghing'alang'adeikha ukhuta pufwale yuve, pu lekhe ukhuvonia isoni incha vubwinda vwakho, ni mono incha khubakhala mu miho nghakho pu lolanghe.
Ndikukulangiza kuti ugule kwa Ine golide woyengedwa ndi moto kuti ukhale wolemera. Ugule zovala zoyera kuti uvale ndi kuphimba umaliseche wako wochititsa manyaziwo. Ndiponso ugule kwa Ine mankhwala a mʼmaso kuti uwone.
19 Voni uvunivanghanile une nikhuvataneila nukhuvamanyisya, nukhuvavunga. Puleino unghimbange nukhupela inongwa.
Amene ndimawakonda ndimawadzudzula ndi kuwalanga. Choncho chita changu ndipo lapa.
20 Lola niemile pandyango ni hodencha. Ula uvei ipuleikha eilimenyu lyango vunihodeincha puangave ideindula undyango. Punikhwingeila khumwene nu khulya pninie numwene, navope paninie nune.
Taonani ndayima pa khomo ndikugogoda. Ngati wina amva mawu anga natsekula chitseko, Ine ndidzalowamo ndi kudya naye, Ine ndi iyeyo.
21 Ula uvei iva ndutu paligoha vei ula nikhupinchangha uvutama uvwa khutama paninie nune pakheinyalwangula, nduvu une neikhava nduti puneitamile paninie nu Daada vango pa kheinyalwanghula khya mwene.
Amene adzapambana, ndidzamupatsa ufulu wokhala nane pamodzi pa mpando wanga waufumu monga mmene Ine ndinapambana ndi kukhala pansi ndi Atate anga pa mpando wawo waufumu.
22 Ula uvei alei nimbulukhutu apuleikhanghe khila eikhyu u mepo ikhungheivula eimipalela.”
Amene ali ndi makutu, amve zimene Mzimu akuwuza mipingo.”

< Ufunuo 3 >