< Bhakolosai 1 >

1 Paulo, Intumwa ya Yesu Kristo mu kwenda kwa Nyamuanga, na Timotheo owasu,
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
2 ku bhekilisha na bhasu abheikanyibhwa mu Kristo bhanu bhali Kolosai. Echigongo chibhe kwemwe, no mulembe okusoka ku Nyamuanga Lata weswe.
Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
3 Echisosha isime ku Nyamuanga, Lata wa Latabhugenyi weswe Yesu Kristo, na echibhasabhila kwiya kafu.
Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
4 Chonguywe elikilisha lyemwe mu Yesu Kristo no kwenda kunu mulinakwo ku bhaliya bhona bhanu bhauywe ingulu ya Nyamuanga.
Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
5 Muli no kwenda kunu kulwo kwiikanya kwe chimali kunu mwabhikiywe Mulwile ingulu yemwe. Mwonguywe ingulu yo kwiikanya okwo okwe chimali guchali mu musango gwo kumasha, omusango gwo bhwana,
Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
6 gunu gwijile kwemwe. Omusango gwo bhwana gunu gwibhuye litwasho na kuswila Chalo chona. One eikola kutya mwiimwe okusokelela ku lusiku lunu mwonguywe no kwiingila okulubhana ne chigongo cha Nyamuanga mu kumasha.
umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
7 Gunu nigwo omusango gwo bhwana gunu mweigiye okusoka ku Epafra, omwendwa weswe omukosi wejasu, unu ali mukosi mwiikanyibhwa wa Kristo kulweswe.
Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
8 Epafra agukolele gumenyekane kweswe okwenda kwemwe mu Mwoyo.
Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
9 Kunsonga yo kwenda kunu, okusokelela ku lusiku lunu chonguywe kutya, chichali kusinga kubhasabhila. Echibhalikisho ati mwijusibhwe obhwenge bhwo kwenda kwaye mu bhwengeso bhwona no bhumenyi bhwe chinyamwoyo.
Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
10 Echisabhwa ati mulibhatile mu bhwiikanyibhwa obhwa Latabhugenyi mu ngendo ejo jikondelesishe. Echisabhwa ati omwibhula litwasho mu bhuli chikolwa che kisi na ati omukula mu bhumenyi bhwa Nyamuanga.
Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
11 Echisabhwa ati mutule okutendwa amanaga mu bhuli bhutulo okulubhana na managa ya likusho lyaye mu kwigumilisha na mu kwikomesha Leona.
Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
12 Echisabhwa ati, mu kukondelwa, omusosha isime ku Lata, unu abhakola emwe mutule okubha ebhala mu kulya omwandu gwa bhekilisha mu bhwelu.
ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
13 Achikisishe okusoka mu bhuteile bhwe chisute no kuchifululila mu bhukama bhwo Mwana waye omwendwa.
Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
14 Mu Mwana waye chili no kwelesha, unu ali musasisi we bhibhibhi.
Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
15 Omwana ni chijejekanyo cha Nyamuanga unu atakubhonekana. Ni wo bhubhele mu bhumogi bhwona.
Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
16 Kulwo kubha ku mwene ebhinu bhyona bhyayangilwe, bhilya bhinu bhili mu lwile na bhinu bhilimo mu chalo, bhinu ebhibhonekana na bhinu bhitakubhonekana. Bhikabha ni bhya chikama amwi bhya bhutulo amwi bhya bhutungi amwi ebhya managa, ebhinu bhyona bhiyangilwe no mwene na ingulu yaye.
Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
17 omwene niwe atangatiye ebhinu bhyona, na mu mwene bhinu bhyona bhigwatene amwi.
Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
18 No mwene niwe mutwe gwo mubhili niyo ikanisa, mwenene niwe obhwambilo no mwibhulwa wo bhubhele okusoka mu bhafuye, kwibhyo, ana omwanya gwo kwamba agati ye bhinu bhyona.
Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
19 Kulwo kubha Nyamuanga akondeleywe ati okukumila kwaye nukwikala mu mwene,
Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
20 no kugwatanya ebhinu bhyona kwaye ku mwene mu njila yo mwana waye. Nyamuanga akolele omulembe okulabha mu nsagama yo musalabha gwaye. Nyamuanga agwatanyisishe ebhinu bhyona mu mwenene, alabha ni bhinu bhya mu chalo amwi bhinu bhya Mulwile.
Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
21 Emwe one, mu mwanya gumwi kwaliga muli bhagenyi ku Nyamuanga na mwaliga muli bhasoko bhaye mu bhwenge na mu bhikolwa bhibhibhi.
Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
22 Mbe nawe woli abhagwatanyishe emwe kwo mubhili gwaye okulabha ku lufu. Akolele kutya koleleki abhalete emwe abhwelu, bhanu mutane-solo nolwo kakojole kona imbele yaye,
Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
23 mbe mukagendelela mu likilisha, lwa kutyo mwalumatanyibhwe ni mukomela, nolwo obhutasosibhwao no kusilwa kula mu kusoka mu liikanya lyo bhubhasi elyo musango gwo bhwana gunu mwonguywe. Gunu nigwo omusango gwo bhwana gunu gwalasibhwe ku bhuli munu unu ayangilwe emwalo yo lwile. Gunu nigwo omusango gwo bhwana gunu kugwo anye, Paulo, mwabhee mukosi.
ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
24 Woli enikondelelwa jinyako Jani kulwa ingulu yemwe. Nanye enikumisha mu mubhili gwani chinu chinkeyeye kulwa jinyako ja Kristo kulwa ingulu yo mubhili gwaye, gunu guli Kanisa.
Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
25 Anye nili mukosi wa likanisa linu, kisi-kisi no bhukosi bhunu nayanilwe okusoka ku Nyamuanga kulwa ingulu yemwe, okwijusha omusango gwa Nyamuanga.
Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
26 Chinu nicho echimali cha imbisike inu yaliga iselekelwe mu miyaka myafu na ku maimbo gona. Mbe nawe woli yasuluywe ku bhona bhanu abhekilisha mu mwene. (aiōn g165)
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
27 Ni ku bhaliya bhanu Nyamuanga aga endele okusulula kutyo bhuli obhunibhi bhwa likusho elya imbisike ye chimali inu agati ya Maanga. Ni ati Kristo abhalimo emwe, obhubhasi bhwa likusho linu elija.
Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
28 Unu niwe echimulasha. Nichibhekengya bhuli munu, no kumwiigisha bhuli munu kwo bhwengeso bhwona, koleleki ati chimulete bhuli munu akumiye mu Kristo.
Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
29 Ingulu ya ganu, anye enikomesha no kwilwanilila okulubhana na managa gaye ganu agakola emilimu munda yani mu bhutulo.
Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

< Bhakolosai 1 >