< ヨブ 記 8 >

1 時にシュヒ人ビルダデ答へて曰く
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 何時まで汝かかる事を言や 何時まで汝の口の言語を大風のごとくにするや
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 神あに審判を曲たまはんや 全能者あに公義を曲たまはんや
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 汝の子等かれに罪を獲たるにや之をその愆の手に付したまへり
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 汝もし神に求め 全能者に祈り
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 清くかつ正しうしてあらば必ず今汝を顧み汝の義き家を榮えしめたまはん
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 然らば汝の始は微小くあるとも汝の終は甚だ大ならん
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 請ふ汝過にし代の人に問へ 彼らの父祖の尋究めしところの事を學べ
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (我らは昨日より有しのみにて何をも知ず 我らが世にある日は影のごとし)
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 彼等なんぢを教へ汝を諭し 言をその心より出さざらんや
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 葦あに泥なくして長んや 萩あに水なくしてそだたんや
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 是はその青くして未だ刈ざる時にも他の一切の草よりは早く槁る
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 神を忘るる者の道は凡て是のごとく 悖る者の望は空しくなる
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 その恃む所は絶れ その倚ところは蜘蛛網のごとし
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 その家に倚かからんとすれば家立ず 之に堅くとりすがるも保たじ
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 彼日の前に青緑を呈はし その枝を園に蔓延らせ
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 その根を石堆に盤みて石の屋を眺むれども
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 若その處より取のぞかれなばその處これを認めずして我は汝を見たる事なしと言ん
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 視よその道の喜樂是のごとし 而してまた他の者地より生いでん
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 それ神は完全人を棄たまはず また惡き者の手を執りたまはず
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 遂に哂笑をもて汝の口に充し歡喜を汝の唇に置たまはん
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 汝を惡む者は羞恥を着せられ 惡き者の住所は無なるべし
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< ヨブ 記 8 >