< 詩篇 92 >

1 安息日の歌、さんび いと高き者よ、主に感謝し、み名をほめたたえるのは、よいことです。
Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata. Nʼkwabwino kutamanda Yehova ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,
2 あしたに、あなたのいつくしみをあらわし、夜な夜な、あなたのまことをあらわすために、
Kulengeza chikondi chanu mmawa, ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,
3 十弦の楽器と立琴を用い、琴のたえなる調べを用いるのは、よいことです。
kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi ndi mayimbidwe abwino a zeze.
4 主よ、あなたはみわざをもってわたしを楽しませられました。わたしはあなたのみ手のわざを喜び歌います。
Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova; Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.
5 主よ、あなたのみわざはいかに大いなることでしょう。あなたのもろもろの思いは、いとも深く、
Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova, maganizo anu ndi ozamadi!
6 鈍い者は知ることができず、愚かな者はこれを悟ることができません。
Munthu wopanda nzeru sadziwa, zitsiru sizizindikira,
7 たとい、悪しき者は草のようにもえいで、不義を行う者はことごとく栄えても、彼らはとこしえに滅びに定められているのです。
kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula, adzawonongedwa kwamuyaya.
8 しかし、主よ、あなたはとこしえに高き所にいらせられます。
Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.
9 主よ、あなたの敵、あなたの敵は滅び、不義を行う者はことごとく散らされるでしょう。
Zoonadi adani anu Yehova, zoonadi adani anu adzawonongeka; onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.
10 しかし、あなたはわたしの角を野牛の角のように高くあげ、新しい油をわたしに注がれました。
Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati; mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.
11 わたしの目はわが敵の没落を見、わたしの耳はわたしを攻める悪者どもの破滅を聞きました。
Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane, makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.
12 正しい者はなつめやしの木のように栄え、レバノンの香柏のように育ちます。
Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa, adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
13 彼らは主の家に植えられ、われらの神の大庭に栄えます。
odzalidwa mʼnyumba ya Yehova, adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.
14 彼らは年老いてなお実を結び、いつも生気に満ち、青々として、
Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo, adzakhala anthete ndi obiriwira,
15 主の正しいことを示すでしょう。主はわが岩です。主には少しの不義もありません。
kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama; Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

< 詩篇 92 >