< 箴言 知恵の泉 4 >

1 子供らよ、父の教を聞き、悟りを得るために耳を傾けよ。
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 わたしは、良い教訓を、あなたがたにさずける。わたしの教を捨ててはならない。
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 わたしもわが父には子であり、わが母の目には、ひとりのいとし子であった。
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 父はわたしを教えて言った、「わたしの言葉を、心に留め、わたしの戒めを守って、命を得よ。
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 それを忘れることなく、またわが口の言葉にそむいてはならない、知恵を得よ、悟りを得よ。
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 知恵を捨てるな、それはあなたを守る。それを愛せよ、それはあなたを保つ。
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 知恵の初めはこれである、知恵を得よ、あなたが何を得るにしても、悟りを得よ。
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 それを尊べ、そうすれば、それはあなたを高くあげる、もしそれをいだくならば、それはあなたを尊くする。
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 それはあなたの頭に麗しい飾りを置き、栄えの冠をあなたに与える」。
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 わが子よ、聞け、わたしの言葉をうけいれよ、そうすれば、あなたの命の年は多くなる。
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 わたしは知恵の道をあなたに教え、正しい道筋にあなたを導いた。
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 あなたが歩くとき、その歩みは妨げられず、走る時にも、つまずくことはない。
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 教訓をかたくとらえて、離してはならない、それを守れ、それはあなたの命である。
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 よこしまな者の道に、はいってはならない、悪しき者の道を歩んではならない。
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 それを避けよ、通ってはならない、それを離れて進め。
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 彼らは悪を行わなければ眠ることができず、人をつまずかせなければ、寝ることができず、
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 不正のパンを食らい、暴虐の酒を飲むからである。
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 正しい者の道は、夜明けの光のようだ、いよいよ輝きを増して真昼となる。
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 悪しき人の道は暗やみのようだ、彼らは何につまずくかを知らない。
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 わが子よ、わたしの言葉に心をとめ、わたしの語ることに耳を傾けよ。
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 それを、あなたの目から離さず、あなたの心のうちに守れ。
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 それは、これを得る者の命であり、またその全身を健やかにするからである。
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 油断することなく、あなたの心を守れ、命の泉は、これから流れ出るからである。
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 曲った言葉をあなたから捨てさり、よこしまな談話をあなたから遠ざけよ。
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 あなたの目は、まっすぐに正面を見、あなたのまぶたはあなたの前を、まっすぐに見よ。
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 あなたの足の道に気をつけよ、そうすれば、あなたのすべての道は安全である。
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 右にも左にも迷い出てはならない、あなたの足を悪から離れさせよ。
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.

< 箴言 知恵の泉 4 >