< 詩篇 25 >

1 ああヱホバよ わがたましひは汝をあふぎ望む
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 わが神よわれなんぢに依賴めり ねがはくはわれに愧をおはしめたまふなかれ わが仇のわれに勝誇ることなからしめたまへ
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 實になんぢを俟望むものははぢしめられず 故なくして信をうしなふものは愧をうけん
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 ヱホバよなんぢの大路をわれにしめし なんぢの徑をわれにをしへたまへ
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 我をなんぢの眞理にみちびき我ををしへたまへ 汝はわがすくひの神なり われ終日なんぢを俟望む
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 なんぢのあはれみと仁慈とはいにしへより絶ずあり ヱホバよこれを思ひいだしたまへ
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 わがわかきときの罪とわが愆とはおもひいでたまふなかれ ヱホバよ汝のめぐみの故になんぢの仁慈にしたがひて我をおもひいでたまへ
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 ヱホバはめぐみ深くして直くましませり 斯るがゆゑに道をつみびとにをしへ
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 謙だるものを正義にみちびきたまはん その道をへりくだる者にしめしたまはん
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 ヱホバのもろもろの道はそのけいやくと證詞とをまもるものには仁慈なり眞理なり
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 わが不義はおほいなり ヱホバよ名のために之をゆるしたまへ
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 ヱホバをおそるる者はたれなるか 之にそのえらぶべき道をしめしたまはん
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 かかる人のたましひは平安にすまひ その裔はくにをつぐべし
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 ヱホバの親愛はヱホバをおそるる者とともにあり ヱホバはその契約をかれらに示したまはん
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 わが目はつねにヱホバにむかふ ヱホバわがあしを網よりとりいだしたまふ可ればなり
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 ねがはくは歸りきたりて我をあはれみたまへ われ獨わびしくまた苦しみをるなり
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 願くはわが心のうれへをゆるめ我をわざはひより脱かれしめたまへ
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 わが患難わが辛苦をかへりみ わがすべての罪をゆるしたまへ
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 わが仇をみたまへ かれらの數はおほし情なき憾をもてわれをにくめり
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 わがたましひをまもり我をたすけたまへ われに愧をおはしめたまふなかれ 我なんぢに依賴めばなり
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 われなんぢを挨望むねがはくは完全と正直とわれをまもれかし
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 神よすべての憂よりイスラエルを贖ひいだしたまへ
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< 詩篇 25 >