< Salmi 135 >

1 Alleluia. Lodate il nome dell’Eterno. Lodatelo, o servi dell’Eterno,
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 che state nella casa dell’Eterno, nei cortili della casa del nostro Dio.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Lodate l’Eterno, perché l’Eterno è buono; salmeggiate al suo nome, perché è amabile.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Poiché l’Eterno ha scelto per sé Giacobbe, ha scelto Israele per suo speciale possesso.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Sì, io conosco che l’Eterno è grande, e che il nostro Signore è al disopra di tutti gli dèi.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 L’Eterno fa tutto ciò che gli piace, in cielo e in terra, nei mari e in tutti gli abissi.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Egli fa salire i vapori dalle estremità della terra, fa i lampi per la pioggia, fa uscire il vento dai suoi tesori.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Egli percosse i primogeniti d’Egitto, così degli uomini come degli animali.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Mandò segni e prodigi in mezzo a te, o Egitto, su Faraone e su tutti i suoi servitori.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Egli percosse grandi nazioni, e uccise re potenti:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon, re degli Amorei, e Og, re di Basan, e tutti i regni di Canaan.
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 E dette il loro paese in eredità, in eredità a Israele, suo popolo.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 O Eterno, il tuo nome dura in perpetuo; la memoria di te, o Eterno, dura per ogni età.
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Poiché l’Eterno farà giustizia al suo popolo, ed avrà compassione dei suoi servitori.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Gl’idoli delle nazioni sono argento e oro, opera di mano d’uomo.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Hanno bocca e non parlano; hanno occhi e non vedono;
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 hanno orecchi e non odono, e non hanno fiato alcuno nella loro bocca.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Simili ad essi siano quelli che li fanno, tutti quelli che in essi confidano.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Casa d’Israele, benedite l’Eterno! Casa d’Aaronne, benedite l’Eterno!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Casa di Levi, benedite l’Eterno! Voi che temete l’Eterno, benedite l’Eterno!
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Sia benedetto da Sion l’Eterno, che abita in Gerusalemme! Alleluia.
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Salmi 135 >