< Salmi 102 >

1 Preghiera dell’afflitto quand’è abbattuto e spande il suo lamento dinanzi all’Eterno. Deh ascolta la mia preghiera, o Eterno, e venga fino a te il mio grido!
Pemphero la munthu wosautsidwa, pamene walefuka, nakhuthulira pamaso pa Yehova kulira kwakeko. Yehova imvani pemphero langa; kulira kwanga kopempha thandizo kufike kwa Inu.
2 Non mi nasconder la tua faccia nel dì della mia distretta; inclina a me il tuo orecchio; nel giorno che io grido, affrettati a rispondermi.
Musandibisire nkhope yanu pamene ndili pa msautso. Munditcherere khutu; pamene ndiyitana ndiyankheni msanga.
3 Poiché i miei giorni svaniscono come fumo, e le mie ossa si consumano come un tizzone.
Pakuti masiku anga akupita ngati utsi; mafupa anga akunyeka ngati nkhuni zoyaka.
4 Colpito è il mio cuore come l’erba, e si è seccato; perché ho dimenticato perfino di mangiare il mio pane.
Mtima wanga wakanthidwa ndipo ukufota ngati udzu; ndipo ndimayiwala kudya chakudya changa.
5 A cagion della voce dei miei gemiti, le mie ossa s’attaccano alla mia carne.
Chifukwa cha kubuwula kwanga kofuwula ndatsala chikopa ndi mafupa okhaokha.
6 Son simile al pellicano del deserto, son come il gufo de’ luoghi desolati.
Ndili ngati kadzidzi wa ku chipululu, monga kadzidzi pakati pa mabwinja.
7 Io veglio, e sono come il passero solitario sul tetto.
Ndimagona osapeza tulo; ndakhala ngati mbalame yokhala yokha pa denga.
8 I miei nemici m’oltraggiano ogni giorno; quelli che son furibondi contro di me si servon del mio nome per imprecare.
Tsiku lonse adani anga amandichita chipongwe; iwo amene amandinyoza, amagwiritsa ntchito dzina langa ngati temberero.
9 Poiché io mangio cenere come fosse pane, e mescolo con lagrime la mia bevanda,
Pakuti ndimadya phulusa ngati chakudya changa ndi kusakaniza chakumwa changa ndi misozi
10 a cagione della tua indignazione e del tuo cruccio; poiché m’hai levato in alto e gettato via.
chifukwa cha ukali wanu waukulu, popeza Inu mwandinyamula ndi kunditayira kumbali.
11 I miei giorni son come l’ombra che s’allunga, e io son disseccato come l’erba.
Masiku anga ali ngati mthunzi wa kumadzulo; Ine ndikufota ngati udzu.
12 Ma tu, o Eterno, dimori in perpetuo, e la tua memoria dura per ogni età.
Koma Inu Yehova, muli pa mpando wanu waufumu kwamuyaya; kudziwika kwanu ndi kokhazikika ku mibado yonse.
13 Tu ti leverai ed avrai compassione di Sion, poiché è tempo d’averne pietà; il tempo fissato è giunto.
Inu mudzadzuka ndi kuchitira chifundo Ziyoni pakuti ndi nthawi yoti muonetse kukoma mtima kwanu pa iyeyo; nthawi yoyikika yafika.
14 Perché i tuoi servitori hanno affezione alle sue pietre, ed hanno pietà della sua polvere.
Pakuti miyala yake ndi yokondedwa kwa atumiki anu; fumbi lake lokha limawachititsa kuti amve chisoni.
15 Allora le nazioni temeranno il nome dell’Eterno, e tutti i re della terra la tua gloria,
Mitundu ya anthu idzaopa dzina la Yehova, mafumu onse a dziko lapansi adzalemekeza ulemerero wanu.
16 quando l’Eterno avrà riedificata Sion, sarà apparso nella sua gloria,
Pakuti Yehova adzamanganso Ziyoni ndi kuonekera mu ulemerero wake.
17 avrà avuto riguardo alla preghiera dei desolati, e non avrà sprezzato la loro supplicazione.
Iye adzayankha pemphero la anthu otayika; sadzanyoza kupempha kwawo.
18 Questo sarà scritto per l’età a venire, e il popolo che sarà creato loderà l’Eterno,
Zimenezi zilembedwe chifukwa cha mibado ya mʼtsogolo, kuti anthu amene sanabadwe adzatamande Yehova:
19 perch’egli avrà guardato dall’alto del suo santuario; dal cielo l’Eterno avrà mirato la terra
“Yehova anayangʼana pansi kuchokera ku malo ake opatulika mmwamba, kuchokera kumwamba anayangʼana dziko lapansi,
20 per udire i gemiti de’ prigionieri, per liberare i condannati a morte,
kuti amve kubuwula kwa anthu a mʼndende, kuti apulumutse amene anayenera kuphedwa.”
21 affinché pubblichino il nome dell’Eterno in Sion e la sua lode in Gerusalemme,
Kotero dzina la Yehova lidzalengezedwa mu Ziyoni ndi matamando ake mu Yerusalemu,
22 quando i popoli e i regni si raduneranno insieme per servire l’Eterno.
pamene mitundu ya anthu ndi maufumu adzasonkhana kuti alambire Yehova.
23 Egli ha abbattuto le mie forze durante il mio cammino; ha accorciato i miei giorni.
Iye anathyola mphamvu zanga pa nthawi ya moyo wanga; Iyeyo anafupikitsa masiku anga.
24 Io ho detto: Dio mio, non mi portar via nel mezzo dei miei giorni; i tuoi anni durano per ogni età.
Choncho Ine ndinati: “Musandichotse, Inu Mulungu wanga, pakati pa masiku a moyo wanga; zaka zanu zimakhalabe pa mibado yonse.
25 Tu fondasti ab antico la terra, e i cieli son l’opera delle tue mani.
Pachiyambi Inu munakhazikitsa maziko a dziko lapansi ndipo mayiko akumwamba ndi ntchito ya manja anu.
26 Essi periranno, ma tu rimani; tutti quanti si logoreranno come un vestito; tu li muterai come una veste e saranno mutati.
Izi zidzatha, koma Inu mudzakhalapo; zidzatha ngati chovala. Mudzazisintha ngati chovala ndipo zidzatayidwa.
27 Ma tu sei sempre lo stesso, e gli anni tuoi non avranno mai fine.
Koma Inu simusintha, ndipo zaka zanu sizidzatha.
28 I figliuoli de’ tuoi servitori avranno una dimora, e la loro progenie sarà stabilita nel tuo cospetto.
Ana a atumiki anu adzakhala pamaso panu; zidzukulu zawo zidzakhazikika pamaso panu.”

< Salmi 102 >