< Neemia 7 >

1 Or quando le mura furon riedificate ed io ebbi messo a posto le porte, e i portinai, i cantori e i Leviti furono stabiliti nei loro uffici,
Khoma linamangidwa ndipo zitseko zinayikidwa. Pambuyo pake alonda a Nyumba ya Mulungu, oyimba nyimbo ndiponso Alevi anasankhidwa.
2 io detti il comando di Gerusalemme ad Hanani, mio fratello, e ad Hanania governatore del castello, perch’era un uomo fedele e timorato di Dio più di tanti altri.
Kenaka ine ndinasankha mʼbale wanga Hanani pamodzi ndi Hananiya woyangʼanira nsanja yankhondo kukhala olamulira Yerusalemu chifukwa iyeyu anali munthu odalirika ndi woopa Mulungu kuposa anthu ena.
3 E dissi loro: “Le porte di Gerusalemme non s’aprano finché il sole scotti; e mentre le guardie saranno ancora al loro posto, si chiudano e si sbarrino le porte; e si stabiliscano per far la guardia, gli abitanti di Gerusalemme, ciascuno al suo turno e ciascuno davanti alla propria casa”.
Ine ndinawawuza kuti, “Musalole kuti zipata za Yerusalemu zitsekulidwe mpaka dzuwa litatentha, ndipo alonda asanaweruke aonetsetse kuti atseka zitseko ndi kuzipiringidza. Musankhe alonda pakati pa anthu okhala mu Yerusalemu, ena akhale pa malo pawo ndi ena akhale moyangʼanana ndi nyumba zawo.”
4 Or la città era spaziosa e grande; ma dentro v’era poca gente, e non vi s’eran fabbricate case.
Tsono mzinda wa Yerusalemu unali wotambasuka ndiponso waukulu koma munali anthu ochepa ndipo nyumba zinali zisanamangidwe.
5 E il mio Dio mi mise in cuore di radunare i notabili, i magistrati e il popolo, per farne il censimento. E trovai il registro genealogico di quelli ch’eran tornati dall’esilio la prima volta, e vi trovai scritto quanto segue:
Ndipo Mulungu wanga anayika mu mtima mwanga maganizo oti ndisonkhanitse anthu olemekezeka, akuluakulu ndi anthu onse kuti alembetse mayina mwa mabanja awo. Ndinapeza buku limene munalembedwa mayina a mabanja a iwo amene anayamba kubwera kuchokera ku ukapolo. Izi ndi zimene ndinazipeza zitalembedwa mʼmenemo:
6 Questi son quei della provincia che tornarono dalla cattività; quelli che Nebucadnetsar, re di Babilonia, avea menati in cattività, e che tornarono a Gerusalemme e in Giuda, ciascuno nella sua città.
Awa ndi anthu a mʼchigawo cha Yuda amene anabwerera kuchokera ku ukapolo amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawatenga ukapolo. Iwo anabwerera ku Yerusalemu ndi ku Yuda, aliyense ku mzinda wa makolo ake.
7 Essi tornarono con Zorobabele, Jeshua, Nehemia, Azaria, Raamia, Nahamani, Mardocheo, Bilshan, Mispereth, Bigvai, Nehum e Baana. Censimento degli uomini del popolo d’Israele:
Anabwera pamodzi ndi atsogoleri awa: Zerubabeli, Yesuwa, Nehemiya, Azariya, Raamiya, Nahamani, Mordekai, Bilisani, Misipereti, Bigivai, Nehumu ndi Baana. Tsono chiwerengero cha anthu a ku Israeli chinali chotere:
8 Figliuoli di Parosh, duemila centosettantadue.
Zidzukulu za Parosi 2,172
9 Figliuoli di Scefatia, trecentosettantadue.
Zidzukulu za Sefatiya 372
10 Figliuoli di Ara, seicento cinquantadue.
Zidzukulu za Ara 652
11 Figliuoli di Pahath-Moab, dei figliuoli di Jeshua e di Joab, duemila ottocentodiciotto.
Zidzukulu za Pahati-Mowabu (kudzera mu mʼbado wa Yesuwa ndi Yowabu) 2,818
12 Figliuoli di Elam, mille duecentocinquanta quattro.
Zidzukulu za Elamu 1,254
13 Figliuoli di Zattu, ottocentoquaranta cinque.
Zidzukulu za Zatu 845
14 Figliuoli di Zaccai, settecentosessanta.
Zidzukulu za Zakai 760
15 Figliuoli di Binnui, seicento quarantotto.
Zidzukulu za Binuyi 648
16 Figliuoli di Bebai, seicento ventotto.
Zidzukulu za Bebai 628
17 Figliuoli di Azgad, duemila trecento ventidue.
Zidzukulu za Azigadi 2,322
18 Figliuoli di Adonikam, seicento sessantasette.
Zidzukulu za Adonikamu 667
19 Figliuoli di Bigvai, duemila sessantasette.
Zidzukulu za Abigivai 2,067
20 Figliuoli di Adin, seicento cinquantacinque.
Zidzukulu za Adini 655
21 Figliuoli di Ater, della famiglia d’Ezechia, novantotto.
Zidzukulu za Ateri (kudzera mwa Hezekiya) 98
22 Figliuoli di Hashum, trecentoventotto.
Zidzukulu za Hasumu 328
23 Figliuoli di Bezai, trecento ventiquattro.
Zidzukulu za Bezayi 324
24 Figliuoli di Harif, centododici.
Zidzukulu za Harifu 112
25 Figliuoli di Gabaon, novantacinque.
Zidzukulu za Gibiyoni 95.
26 Uomini di Bethlehem e di Netofa, centottantotto.
Anthu a ku Betelehemu ndi Netofa 188
27 Uomini di Anathoth, centoventotto.
Anthu a ku Anatoti 128
28 Uomini di Beth-Azmaveth, quarantadue.
Anthu a ku Beti-Azimaveti 42
29 Uomini di Kiriath-Jearim, di Kefira e di Beeroth, settecentoquarantatre.
Anthu a ku Kiriati Yeyarimu Kefira ndi Beeroti 743
30 Uomini di Rama e di Gheba, seicentoventuno.
Anthu a ku Rama ndi Geba 621
31 Uomini di Micmas, centoventidue.
Anthu a ku Mikimasi 122
32 Uomini di Bethel e d’Ai, centoventitre.
Anthu a ku Beteli ndi Ai 123
33 Uomini d’un altro Nebo, cinquantadue.
Anthu a ku Nebo winayo 52
34 Figliuoli d’un altro Elam, mille duecentocinquanta quattro.
Ana a Elamu wina 1,254
35 Figliuoli di Harim, trecentoventi.
Zidzukulu za Harimu 320
36 Figliuoli di Gerico, trecento quarantacinque.
Zidzukulu za Yeriko 345
37 Figliuoli di Lod, di Hadid e d’Ono, settecentoventuno.
Zidzukulu za Lodi, Hadidi ndi Ono 721
38 Figliuoli di Senaa, tremila novecentotrenta.
Zidzukulu za Senaya 3,930.
39 Sacerdoti: figliuoli di Jedaia, della casa di Jeshua, novecento sessantatre.
Ansembe anali awa: A banja la Yedaya (ndiye kuti zidzukulu za Yesuwa) 973
40 Figliuoli di Immer, mille cinquantadue.
Zidzukulu za Imeri 1,052
41 Figliuoli di Pashur, mille duecento quarantasette.
Zidzukulu za Pasi-Huri 1,247
42 Figliuoli di Harim, mille diciassette.
Zidzukulu za Harimu 1,017.
43 Leviti: figliuoli di Jeshua e di Kadmiel, de’ figliuoli di Hodeva, settantaquattro.
Alevi anali awa: A banja la Yesuwa ndi Kadimieli, ndiye kuti zidzukulu za Hodaviya 74.
44 Cantori: figliuoli di Asaf, cento quarantotto.
Anthu oyimba: Zidzukulu za Asafu 148.
45 Portinai: figliuoli di Shallum, figliuoli di Ater, figliuoli di Talmon, figliuoli di Akkub, figliuoli di Hatita, figliuoli di Shobai, centotrentotto.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Salumu, Ateri, Talimoni, Hatita ndi Sobai 138.
46 Nethinei: figliuoli di Tsiha, figliuoli di Hasufa, figliuoli di Tabbaoth,
Anthu ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Zidzukulu za Ziha, zidzukulu za Hasufa, zidzukulu za Tabaoti,
47 figliuoli di Keros, figliuoli di Sia, figliuoli di Padon,
Zidzukulu Kerosi, zidzukulu za Siya, zidzukulu za Padoni
48 figliuoli di Lebana, figliuoli di Hagaba, figliuoli di Salmai,
Zidzukulu za Lebana za Hagaba, ndi za Salimayi,
49 figliuoli di Hanan, figliuoli di Ghiddel, figliuoli di Gahar,
Zidzukulu za Hanani, zidzukulu za Gideli, zidzukulu za Gahari,
50 figliuoli di Reaia, figliuoli di Retsin, figliuoli di Nekoda,
Zidzukulu za Reyaya, zidzukulu za Rezini, zidzukulu za Nehoda,
51 figliuoli di Gazzam, figliuoli di Uzza, figliuoli di Paseah,
Zidzukulu za Gazamu, zidzukulu za Uza, zidzukulu za Paseya,
52 figliuoli di Besai, figliuoli di Meunim, figliuoli di Nefiscesim,
Zidzukulu za Besai, zidzukulu za Meunimu, zidzukulu za Nefusimu,
53 figliuoli di Bakbuk, figliuoli di Hakufa, figliuoli di Harhur,
Zidzukulu za Bakibuku, zidzukulu za Hakufa, zidzukulu za Harihuri,
54 figliuoli di Bazlith, figliuoli di Mehida, figliuoli di Harsha,
Zidzukulu za Baziliti, zidzukulu za Mehida, zidzukulu za Harisa,
55 figliuoli di Barkos, figliuoli di Sisera, figliuoli di Temah,
Zidzukulu za Barikosi, zidzukulu za Sisera, zidzukulu za Tema
56 figliuoli di Netsiah, figliuoli di Hatifa.
Zidzukulu za Neziya, ndi zidzukulu za Hatifa.
57 Figliuoli dei servi di Salomone: figliuoli di Sotai, figliuoli di Sofereth, figliuoli di Perida,
Zidzukulu za antchito a Solomoni: Zidzukulu za Sotai, zidzukulu za Sofereti, zidzukulu za Perida
58 figliuoli di Jala, figliuoli di Darkon, figliuoli di Ghiddel,
zidzukulu za Yaala, zidzukulu za Darikoni, zidzukulu za Gideli,
59 figliuoli di Scefatia, figliuoli di Hattil, figliuoli di Pokereth-Hatsebaim, figliuoli di Amon.
zidzukulu za Sefatiya, zidzukulu za Hatilu zidzukulu za Pokereti-Hazebaimu ndi zidzukulu Amoni.
60 Totale dei Nethinei e de’ figliuoli de’ servi di Salomone, trecentonovantadue.
Anthu onse ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi zidzukulu za antchito a Solomoni analipo 392.
61 Ed ecco quelli che tornarono da Tel-Melah, da Tel-Harsha, da Kerub-Addon e da Immer, e che non avean potuto stabilire la loro genealogia patriarcale per dimostrare ch’erano Israeliti:
Ali munsiwa anachokera ku Teli-Mela, Teri-Harisa, Kerubi, Adoni, ndi Imeri, koma sanathe kunena mwa tchutchutchu kuti makolo awo kapena mafuko awo analidi Aisraeli kapena ayi.
62 figliuoli di Delaia, figliuoli di Tobia, figliuoli di Nekoda, seicento quarantadue.
Zidzukulu za Delaya, zidzukulu za Tobiya ndi zidzukulu za Nekoda 642.
63 Di tra i sacerdoti: figliuoli di Habaia, figliuoli di Hakkots, figliuoli di Barzillai, il quale avea sposato una delle figliuole di Barzillai, il Galaadita, e fu chiamato col nome loro.
Ndiponso ena pakati pa ansembe anali awa: zidzukulu za Hobiya, zidzukulu za Hakozi ndi zidzukulu za Barizilai (munthu amene anakwatira mwana wamkazi wa Barizilai wa ku Giliyadi ndipo amatchedwa dzina limenelo).
64 Questi cercarono i loro titoli genealogici, ma non li trovarono, e furon quindi esclusi, come impuri, dal sacerdozio;
Iwowa anafufuzafufuza mayina awo mʼbuku la mibado ya mabanja awo ndipo sanapeze mayina awo kotero anachotsedwa pa unsembe nawerengedwa ngati odetsedwa pa chipembedzo.
65 e il governatore disse loro di non mangiare cose santissime finché non si presentasse un sacerdote per consultar Dio con l’Urim e il Thummim.
Choncho bwanamkubwa anawawuza anthuwo kuti asamadye nawo chakudya china chilichonse choperekedwa kwa Mulungu mpaka patapezeka wansembe wodziwa kugwiritsa bwino ntchito ya Urimu ndi Tumimu.
66 La raunanza, tutt’assieme, noverava quarantaduemila trecentosessanta persone,
Chiwerengero chonse cha anthuwa chinali 42,360.
67 senza contare i loro servi e le loro serve, che ammontavano a settemila trecento trentasette. Avevan pure duecento quarantacinque cantori e cantatrici.
Kuwonjezera pamenepa panali antchito awo aamuna ndi aakazi 7,337 ndiponso anthu aamuna ndi aakazi oyimba nyimbo okwanira 245.
68 Avevano settecento trentasei cavalli, duecento quarantacinque muli,
Panali akavalo 736, abulu angʼonoangʼono 245.
69 quattrocento trentacinque cammelli, seimila settecentoventi asini.
Ngamira zawo zinalipo 435 ndipo abulu analipo 6,720.
70 Alcuni dei capi famiglia offriron dei doni per l’opera. Il governatore diede al tesoro mille dariche d’oro, cinquanta coppe, cinquecentotrenta vesti sacerdotali.
Atsogoleri ena a mabanja anapereka mphatso zothandizira ntchito. Bwanamkubwa anapereka ku thumba losungira chuma, ndalama zagolide za makilogalamu asanu ndi atatu, mabeseni makumi asanu ndi zovala za ansembe 530.
71 E tra i capi famiglia ve ne furono che dettero al tesoro dell’opera ventimila dariche d’oro e duemila duecento mine d’argento.
Atsogoleri ena amabanja anapereka ku thumba losungira chuma ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndiponso ndalama za siliva zokwana makilogalamu 1,250.
72 Il resto del popolo dette ventimila dariche d’oro, duemila mine d’argento e sessantasette vesti sacerdotali.
Anthu ena onse otsala anapereka ndalama zagolide zokwana makilogalamu 168, ndalama za siliva zokwana makilogalamu 140, ndiponso zovala za ansembe 67.
73 I sacerdoti, i Leviti i portinai, i cantori, la gente del popolo, i Nethinei e tutti gl’Israeliti si stabilirono nelle loro città.
Choncho ansembe, Alevi, alonda a Nyumba ya Mulungu, anthu oyimba nyimbo, ena mwa anthu wamba, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu pamodzi ndi Aisraeli ena onse ankakhala mʼmizinda yawo. Pofika mwezi wachisanu ndi chiwiri Aisraeli onse anali atakhazikika mʼmizinda yawo.

< Neemia 7 >