< Salmi 73 >

1 Salmo di Asaf CERTAMENTE Iddio [è] buono ad Israele, A [quelli che son] puri di cuore.
Salimo la Asafu. Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli, kwa iwo amene ndi oyera mtima.
2 Ora, quant'è a me, quasi che incapparono i miei piedi; Come nulla [mancò] che i miei passi non isdrucciolassero.
Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka; ndinatsala pangʼono kugwa.
3 Perciocchè io portava invidia agl'insensati, Veggendo la prosperità degli empi.
Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira, pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.
4 Perciocchè non [vi sono] alcuni legami alla lor morte; E la lor forza [è] prosperosa.
Iwo alibe zosautsa; matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.
5 [Quando] gli [altri] uomini [sono] in travagli, essi non [vi son] punto; E non ricevono battiture col rimanente degli uomini.
Saona mavuto monga anthu ena; sazunzika ngati anthu ena onse.
6 Perciò, la superbia li cinge a giusa di collana; La violenza li involge [come] un vestimento.
Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo; amadziveka chiwawa.
7 Gli occhi escono loro fuori per lo grasso; Avanzano le immaginazioni del cuor [loro].
Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa; zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.
8 Son dissoluti, e per malizia ragionano di oppressare; Parlano da alto.
Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa; mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”
9 Mettono la lor bocca dentro al cielo, E la lor lingua passeggia per la terra.
Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.
10 Perciò, il popolo di Dio riviene a questo, [Veggendo che] l'acqua gli è spremuta a bere a pien [calice],
Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo ndi kumwa madzi mochuluka.
11 E dice: Come [può essere che] Iddio sappia [ogni cosa], E che vi sia conoscimento nell'Altissimo?
Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji? Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”
12 Ecco, costoro [son] empi, e pur godono pace e tranquillità in perpetuo; Ed accrescono le [lor] facoltà.
Umu ndi mmene oyipa alili; nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.
13 Indarno [adunque] in vero ho nettato il mio cuore, Ed ho lavate le mie mani nell'innocenza.
Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera; pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.
14 Poichè son battuto tuttodì, Ed ogni mattina il mio gastigamento [si rinnuova].
Tsiku lonse ndapeza mavuto; ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.
15 Se io dico: Io ragionerò così; Ecco, io son disleale inverso la generazione de' tuoi figliuoli.
Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,” ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.
16 Io ho adunque pensato di [volere] intender questo; Ma [la cosa] mi è parsa molto molesta.
Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi, zinandisautsa kwambiri
17 Infino a tanto che sono entrato ne' santuari di Dio; [Ed] ho considerato il fine di coloro.
kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu; pamenepo ndinamvetsa mathero awo.
18 Certo, tu li metti in isdruccioli; Tu li trabocchi in ruine.
Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera; Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.
19 Come sono eglino stati distrutti in un momento! [Come] son venuti meno, e sono stati consumati per casi spaventevoli!
Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa, amasesedwa kwathunthu ndi mantha!
20 [Son] come un sogno, dopo che [l'uomo] si è destato; O Signore, quando tu [ti] risveglierai, tu sprezzerai la lor vana apparenza.
Monga loto pamene wina adzuka, kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye, mudzawanyoza ngati maloto chabe.
21 Quando il mio cuore era inacerbito, Ed io era punto nelle reni;
Pamene mtima wanga unasautsidwa ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,
22 Io [era] insensato, e non aveva conoscimento; Io era inverso te [simile] alle bestie.
ndinali wopusa ndi wosadziwa; ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.
23 Ma pure io sono stato del continuo teco; Tu mi hai preso per la man destra.
Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse; mumandigwira dzanja langa lamanja.
24 Tu mi condurrai per lo tuo consiglio, E poi mi riceverai [in] gloria;
Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.
25 Chi [è] per me in cielo, [fuor che te?] Io non voglio [altri] che te in terra.
Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu? Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.
26 La mia carne ed il mio cuore erano venuti meno: [Ma] Iddio [è] la rocca del mio cuore, e la mia parte in eterno.
Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka, koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga ndi cholandira changa kwamuyaya.
27 Perciocchè, ecco, quelli che si allontanano da te periranno; Tu distruggerai ogni uomo che fornica[ndo si svia] da te.
Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka; Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.
28 Ma quant'è a me, egli mi [è] buono di accostarmi a Dio; Io ho posta nel Signore Iddio la mia confidanza, Per raccontar tutte le opere sue.
Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu. Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

< Salmi 73 >