< Salmi 60 >

1 Mictam di Davide, da insegnare; [dato] al Capo de' Musici, sopra Susan-edut; intorno a ciò ch'egli diede il guasto alla Siria di Mesopotamia, ed alla Siria di Soba; e che Ioab, ritornando, sconfisse gl'Idumei nella valle del Sale, [in numero di] dodici mila O DIO, tu ci hai scacciati, tu ci hai dissipati, Tu ti sei adirato; [e poi], tu ti sei rivolto a noi.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Tu hai scrollata la terra, e l'hai schiantata; Ristora le sue rotture; perciocchè è smossa.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Tu hai fatte sentire al tuo popolo cose dure; Tu ci hai dato a bere del vino di stordimento.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 [Ma ora], tu hai dato a quelli che ti temono una bandiera, Per alzarla, per amor della [tua] verità. (Sela)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Acciocchè la tua diletta gente sia liberata, Salva[mi col]la tua destra, e rispondimi.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Iddio ha parlato per la sua santità: Io trionferò, Io spartirò Sichem, e misurerò la valle di Succot.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Mio [è] Galaad, e mio [è] Manasse, Ed Efraim [è] la forza del mio capo; Giuda [è] il mio legislatore;
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab [è] la caldaia del mio lavatoio; Io getterò le mie scarpe sopra Edom; O Palestina, fammi delle acclamazioni.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Chi mi condurrà nella città della fortezza? Chi mi menerà fino in Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Non [sarai desso] tu, o Dio, [che] ci avevi scacciati? E non uscivi [più] fuori, o Dio, co' nostri eserciti?
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Dacci aiuto, [per uscir] di distretta; Perciocchè il soccorso degli uomini [è] vanità.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 In Dio noi faremo prodezze; Ed egli calpesterà i nostri nemici.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Salmi 60 >