< Salmi 52 >

1 Maschil di Davide, [dato] al Capo de' Musici; intorno a ciò che Doeg Idumeo era venuto a rapportare a Saulle che Davide era entrato in casa di Ahimelec O POSSENTE [uomo], perchè ti glorii del male? La benignità del Signore [dura] sempre.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, ndakatulo ya Davide; pamene Doegi Mwedomu anapita kwa Sauli ndi kunena kuti “Davide wapita ku nyumba ya Ahimeleki.” Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira ndi zoyipa, iwe munthu wamphamvu? Nʼchifukwa chiyani ukudzitamandira tsiku lonse, iwe munthu wochititsa manyazi pamaso pa Mulungu?
2 La tua lingua divisa malizie; [Ella è] come un rasoio affilato, [o tu], operatore d'inganni.
Tsiku lonse umakhalira kuganizira za kuwononga ena; lilime lako lili ngati lumo lakuthwa, ntchito yako nʼkunyenga.
3 Tu hai amato il male più che il bene; La menzogna più che il parlare dirittamente.
Iwe umakonda choyipa mʼmalo mwa kuyankhula choonadi. Umakonda kunama kupambana kuyankhula zoona. (Sela)
4 Tu hai amate tutte le parole di ruina, O lingua frodolente.
Umakonda mawu onse opweteka, iwe lilime lachinyengo!
5 Iddio altresì ti distruggerà in eterno; Egli ti atterrerà, e ti divellerà dal [tuo] tabernacolo, E ti diradicherà dalla terra de' viventi. (Sela)
Zoonadi Mulungu adzakutsitsa kupita ku chiwonongeko chamuyaya: iye adzakukwatula ndi kukuchotsa mʼtenti yako; iye adzakuzula kuchoka mʼdziko la amoyo.
6 E i giusti lo vedranno, e temeranno; E si rideranno di lui, [dicendo: ]
Olungama adzaona zimenezi ndi kuchita mantha; adzamuseka nʼkumanena kuti,
7 Ecco l'uomo [che] non aveva posto Iddio [per] sua fortezza; Anzi si confidava nella grandezza delle sue ricchezze, E si fortificava nella sua malizia.
“Pano tsopano pali munthu amene sanayese Mulungu linga lake, koma anakhulupirira chuma chake chambiri nalimbika kuchita zoyipa!”
8 Ma io [sarò] come un ulivo verdeggiante nella Casa di Dio; Io mi confido nella benignità di Dio in sempiterno.
Koma ine ndili ngati mtengo wa olivi wobiriwira bwino mʼnyumba ya Mulungu; ndimadalira chikondi chosatha cha Mulungu kwa nthawi za nthawi.
9 [O Signore], io ti celebrerò in eterno; perciocchè tu avrai operato; E spererò nel tuo Nome, perciocchè [è] buono, [Ed è] presente a' tuoi santi.
Ine ndidzakutamandani kwamuyaya chifukwa cha zimene mwachita; chifukwa cha zimene mwachita; mʼdzina lanu ndidzayembekezera pakuti dzina lanulo ndi labwino. Ndidzakutamandani pamaso pa oyera mtima anu.

< Salmi 52 >