< Salmi 146 >

1 ALLELUIA. Anima mia, loda il Signore.
Tamandani Yehova. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
2 Io loderò il Signore, mentre viverò; Io salmeggerò al mio Dio, mentre durerò.
Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.
3 Non vi confidate in principi, [Nè] in alcun figliuol d'uomo, che non ha modo di salvare.
Musamadalire mafumu, anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.
4 Il suo fiato uscirà, ed egli se ne ritornerà nella sua terra; In quel dì periranno i suoi disegni.
Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi; zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.
5 Beato colui che ha l'Iddio di Giacobbe in suo aiuto, La cui speranza [è] nel Signore Iddio suo
Wodala ndi amene thandizo lake ndi Mulungu wa Yakobo.
6 Il quale ha fatto il cielo e la terra, Il mare, e tutto ciò ch'[è] in essi; Che osserva la fede in eterno;
Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo; Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.
7 Il qual fa ragione agli oppressati; [E] dà del cibo agli affamati. Il Signore scioglie i prigioni.
Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala. Yehova amamasula amʼndende,
8 Il Signore apre [gli occhi] a' ciechi; Il Signore rileva quelli che son chinati; Il Signore ama i giusti.
Yehova amatsekula maso anthu osaona, Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi, Yehova amakonda anthu olungama.
9 Il Signore guarda i forestieri; Egli solleva l'orfano e la vedova; E sovverte la via degli empi.
Yehova amasamalira alendo ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye, koma amasokoneza njira za anthu oyipa.
10 Il Signore regna in eterno, E il tuo Dio, o Sion, per ogni età. Alleluia.
Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya, Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse. Tamandani Yehova.

< Salmi 146 >