< Proverbi 5 >

1 Figliuol mio, attendi alla mia sapienza, Inchina il tuo orecchio al mio intendimento;
Mwana wanga, mvetsera bwino za nzeru zimene ndikukuwuzazi, tchera khutu ku mawu odziwitsa bwino zinthu ndikukupatsa,
2 Acciocchè tu osservi gli avvedimenti, E che le tue labbra conservino la scienza.
kuti uthe kuchita zinthu mochenjera ndi mwanzeru ndiponso kuti utetezedwe ku mayankhulidwe a mkazi wachilendo.
3 Perciocchè le labbra della [donna] straniera stillano favi di miele. E il suo palato [è] più dolce che olio;
Pakuti mkazi wachigololo ali ndi mawu okoma ngati uchi. Zoyankhula zake ndi zosalala ngati mafuta,
4 Ma il fine di essa [è] amaro come assenzio, Acuto come una spada a due tagli.
koma kotsirizira kwake ngowawa ngati ndulu; ngakuthwa ngati lupanga lakuthwa konsekonse.
5 I suoi piedi scendono alla morte; I suoi passi fanno capo all'inferno. (Sheol h7585)
Mapazi ake amatsikira ku imfa; akamayenda ndiye kuti akupita ku manda. (Sheol h7585)
6 I suoi sentieri sono vaganti, senza che essa sappia ove va, Perchè non considera attentamente la via della vita.
Iye saganizirapo za njira ya moyo; njira zake ndi zokhotakhota koma iye sadziwa izi.
7 Ora dunque, figliuoli, ascoltatemi, E non vi dipartite da' detti della mia bocca.
Tsopano ana inu, mundimvere; musawasiye mawu anga.
8 Allontana la tua via da essa, E non accostarti all'uscio della sua casa;
Uziyenda kutali ndi mkazi wotereyo, usayandikire khomo la nyumba yake,
9 Che talora tu non dia il tuo onore agli stranieri, E gli anni tuoi al crudele;
kuopa kuti ungadzalanditse ulemerero wako kwa anthu ena; ndi zaka zako kwa anthu ankhanza,
10 Che talora i forestieri non si sazino delle tue facoltà; E che le tue fatiche [non vadano] nella casa dello strano;
kapenanso alendo angadyerere chuma chako ndi phindu la ntchito yako kulemeretsa anthu ena.
11 [E che tu non] gema alla fine, Quando la tua carne ed il tuo corpo saranno consumati;
Potsiriza pa moyo wako udzabuwula, thupi lako lonse litatheratu.
12 E non dica: Come ebbi io in odio l'ammaestramento? E come rigettò il mio cuore la correzione?
Ndipo udzati, “Mayo ine, ndinkadana ndi kusunga mwambo! Mtima wanga unkanyoza chidzudzulo!
13 E [come] non ascoltai la voce di quelli che mi ammaestravano, E non inchinai il mio orecchio a quelli che m'insegnavano?
Sindinamvere aphunzitsi anga kapena alangizi anga.
14 Quasi che sono stato in ogni male, In mezzo della raunanza e della congregazione.
Ine ndatsala pangʼono kuti ndiwonongeke pakati pa msonkhano wonse.”
15 Bevi delle acque della tua cisterna, E de' ruscelli di mezzo della tua fonte.
Imwa madzi a mʼchitsime chakochako, madzi abwino ochokera mʼchitsime chako.
16 Spandansi le tue fonti fuori, Ed i ruscelli delle [tue] acque per le piazze.
Kodi akasupe ako azingosefukira mʼmisewu? Kodi mitsinje yako izingoyendayenda mʼzipata za mzinda?
17 Sieno [quelle acque] a te solo, E a niuno strano teco.
Mitsinjeyo ikhale ya iwe wekha, osati uyigawireko alendo.
18 Sia la tua fonte benedetta; E rallegrati della moglie della tua giovanezza.
Yehova adalitse kasupe wako, ndipo usangalale ndi mkazi wa unyamata wako.
19 [Siati ella] una cerva amorosa, ed una cavriuola graziosa; Inebbrinti le sue mammelle in ogni tempo; Sii del continuo invaghito del suo amore.
Iye uja ali ngati mbalale yayikazi yokongola ndiponso ngati gwape wa maonekedwe abwino. Ukhutitsidwe ndi mawere ake nthawi zonse, ndipo utengeke ndi chikondi chake nthawi zonse.
20 E perchè, figliuol mio, t'invaghiresti della straniera, Ed abbracceresti il seno della forestiera?
Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukukopeka ndi mkazi wachigololo? Bwanji ukukumbatira mkazi wachilendo?
21 Conciossiachè le vie dell'uomo [sieno] davanti agli occhi del Signore, E ch'egli consideri tutti i suoi sentieri.
Pakuti mayendedwe onse a munthu Yehova amawaona, ndipo Iye amapenyetsetsa njira zake zonse.
22 Le iniquità dell'empio lo prenderanno, Ed egli sarà ritenuto con le funi del suo peccato.
Ntchito zoyipa za munthu woyipa zimamukola yekha; zingwe za tchimo lake zimamumanga yekha.
23 Egli morrà per mancamento di correzione; E andrà errando per la molta sua pazzia.
Iye adzafa chifukwa chosowa mwambo, adzasocheretsedwa chifukwa cha uchitsiru wake waukulu.

< Proverbi 5 >