< Proverbi 3 >

1 Figliuol mio, non dimenticare il mio insegnamento; E il cuor tuo guardi i miei comandamenti;
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 Perchè ti aggiungeranno lunghezza di giorni, Ed anni di vita, e prosperità.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Benignità e verità non ti abbandoneranno; Legateli in su la gola, scrivili in su la tavola del tuo cuore;
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 E tu troverai grazia e buon senno Appo Iddio, ed appo gli uomini.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Confidati nel Signore con tutto il tuo cuore; E non appoggiarti in su la tua prudenza.
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 Riconoscilo in tutte le tue vie, Ed egli addirizzerà i tuoi sentieri.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Non reputarti savio appo te stesso; Temi il Signore, e ritratti dal male.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 [Ciò] sarà una medicina al tuo bellico, Ed un inaffiamento alle tue ossa.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Onora il Signore con le tue facoltà, E con le primizie d'ogni tua rendita;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 Ed i tuoi granai saran ripieni di beni in ogni abbondanza, E le tue tina traboccheranno di mosto.
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Figliuol mio, non disdegnar la correzione del Signore; E non ti rincresca il suo gastigamento;
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Perciocchè il Signore gastiga chi egli ama; Anzi come un padre il figliuolo [ch]'egli gradisce.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Beato l'uomo che ha trovata sapienza, E l'uomo che ha ottenuto intendimento.
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 Perciocchè il traffico di essa [è] migliore che il traffico dell'argento, E la sua rendita [è migliore] che l'oro.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Ella [è] più preziosa che le perle; E tutto ciò che tu hai di più caro non la pareggia.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Lunghezza di giorni è alla sua destra; Ricchezza e gloria alla sua sinistra.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Le sue vie [son] vie dilettevoli, E tutti i suoi sentieri [sono] pace.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Ella [è] un albero di vita a quelli che si appigliano ad essa; E beati coloro che la ritengono.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Il Signore ha fondata la terra con sapienza; Egli ha stabiliti i cieli con intendimento.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Per lo suo conoscimento gli abissi furono fessi, E l'aria stilla la rugiada.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Figliuol mio, non dipartansi giammai [queste cose] dagli occhi tuoi; Guarda la ragione e l'avvedimento;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 E quelle saranno vita all'anima tua, E grazia alla tua gola.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Allora camminerai sicuramente per la tua via, Ed il tuo piè non incapperà.
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 Quando tu giacerai, non avrai spavento; E [quando] tu ti riposerai, il tuo sonno sarà dolce.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Tu non temerai di subito spavento, Nè della ruina degli empi, quando ella avverrà.
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Perciocchè il Signore sarà al tuo fianco, E guarderà il tuo piè, che non sia preso.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Non negare il bene a quelli a cui è dovuto, Quando è in tuo potere di far[lo].
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Non dire al tuo prossimo: Va', e torna, E domani te [lo] darò, se tu [l]'hai appo te.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Non macchinare alcun male contro al tuo prossimo Che abita in sicurtà teco.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Non litigar con alcuno senza cagione, S'egli non ti ha fatto alcun torto.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Non portare invidia all'uomo violento, E non eleggere alcuna delle sue vie.
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 Perciocchè l'[uomo] perverso [è] cosa abbominevole al Signore; Ma [egli comunica] il suo consiglio con gli [uomini] diritti.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 La maledizione del Signore [è] nella casa dell'empio; Ma egli benedirà la stanza de' giusti.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Se egli schernisce gli schernitori, Dà altresì grazia agli umili.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 I savi possederanno la gloria; Ma gli stolti se ne portano ignominia.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Proverbi 3 >