< Numeri 34 >

1 IL Signore parlò ancora a Mosè, dicendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Comanda a' figliuoli d'Israele, e di' loro: Conciossiachè voi siate [ora] per entrar nel paese di Canaan, quest'[è] il paese che vi scaderà per eredità, [cioè] il paese di Canaan, secondo i suoi confini.
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 E siavi il lato meridionale dal deserto di Sin alle frontiere di Edom; e l'estremità del mar salato sia il vostro confine dal mezzodi verso oriente.
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 E giri questo confine dal mezzodì verso la salita di Acrabbim, e passi a Sin, e arrivino le sue estremità a Cades-barnea, dal mezzodì; e proceda in Hasa-raddar, e passi in Asmon;
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 poi volti questo confine da Asmon verso il Torrente di Egitto, e arrivino le sue estremità al mare.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 E per confine occidentale siavi il mar grande, e i confini. Questo siavi il confine occidentale.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 E questo siavi il confine settentrionale: Dal mar grande segnatevi il monte di Hor;
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 dal monte di Hor, segnatevi per confine là dove si entra in Hamat; e arrivino le estremità di questo confine a Sedad;
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 e proceda fino a Zifron, e arrivino le sue estremità in Hasar-enan. Questo sia il vostro confine settentrionale.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 Poi segnatevi, per confine orientale, da Hasar-enan a Sefam.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 E scenda questo confine da Sefam in Ribla, dirincontro alla Fonte; poi scenda, e tocchi il lato del mare di Chinneret, verso oriente.
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 Poi scenda al Giordano, e arrivino le sue estremità al mar salato. Questo sia il vostro paese, [limitato] per li suoi confini d'ogn'intorno.
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 E Mosè comandò, e disse a' figliuoli di Israele: Quest'[è] il paese, del quale voi partirete la possessione a sorte; il quale il Signore ha comandato che si dia a nove tribù e mezza;
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 conciossiachè la tribù de' Rubeniti, secondo le lor nazioni paterne, e la tribù de' Gaditi, secondo le lor nazioni paterne, e la metà della tribù di Manasse, abbiano ricevuta la loro eredità.
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 Queste due tribù e mezza hanno ricevuta la loro eredità di qua dal Giordano di Gerico, verso oriente.
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 Il Signore parlò ancora a Mosè, dicendo:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Questi [sono] i nomi degli uomini che vi partiranno l'eredità del paese: Eleazaro Sacerdote, e Giosuè, figliuolo di Nun.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Prendete ancora di ciascuna tribù uno de' Capi, per far la partizione del paese.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 E questi [sono] i nomi degli uomini: Della tribù di Giuda, Caleb, figliuolo di Gefunne;
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 Della tribù de' figliuoli di Simeone, Samuele, figliuolo di Ammihud;
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 Della tribù di Beniamino, Elidad, figliuolo di Chislon;
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 Della tribù de' figliuoli di Dan, il Capo, Bucchi, figliuolo di Iogli;
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 De' figliuoli di Giuseppe, della tribù de' figliuoli di Manasse, il Capo, Hanniel, figliuolo di Efod;
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 E della tribù de' figliuoli di Efraim, il Capo, Chemuel, figliuolo di Siftan;
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 E della tribù de' figliuoli di Zabulon, il Capo, Elisafan, figliuolo di Parnac;
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 E della tribù de' figliuoli d'Issacar, il Capo, Patiel, figliuolo di Azan;
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 E della tribù de' figliuoli di Aser, il Capo, Ahihud, figliuolo di Selomi;
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 E della tribù de' figliuoli di Neftali, il Capo, Pedahel, figliuolo di Ammihud.
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 Questi [son] quelli, a' quali il Signore comandò di far la partizone dell'eredità a' figliuoli d'Israele, nel paese di Canaan.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

< Numeri 34 >