< Giobbe 8 >

1 E BILDAD Suhita rispose, e disse:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Infino a quando proferirai tali ragionamenti, E [saranno] le parole della tua bocca [come] un vento impetuoso?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Iddio pervertirebbe egli il giudicio? L'Onnipotente pervertirebbe egli la giustizia?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Se i tuoi figliuoli hanno peccato contro a lui, Egli altresì li ha dati in mano del lor misfatto.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 [Ma] quant'è a te, se tu ricerchi Iddio, E chiedi grazia all'Onnipotente;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Se tu [sei] puro e diritto, Certamente egli si risveglierà di presente in favor tuo, E farà prosperare il tuo giusto abitacolo.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 E la tua condizione di prima sarà stata piccola, E l'ultima diventerà grandissima.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Perciocchè domanda pur le età primiere, E disponti ad informarti da' padri loro;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Imperocchè, quant'è a noi, [siamo sol da] ieri in qua, E non abbiamo intendimento; Perchè i nostri giorni [son] come un'ombra sopra la terra;
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Non insegnerannoti essi, [e non] parlerannoti, E non trarranno essi fuori ragionamenti dal cuor loro?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Il giunco sorgerà egli senza pantano? L'erba de' prati crescerà ella senz'acqua?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 E pure, mentre [è] ancor verde, e non [è] ancora segata, Si secca avanti ogni [altra] erba.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Tali [son] le vie di tutti quelli che dimenticano Iddio, E [così] perirà la speranza dell'ipocrita;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 La cui speranza sarà troncata, E la cui confidanza [sarà] una casa di ragnolo.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Egli si appoggerà in su la casa sua, ma quella non istarà ferma; Egli si atterrà ad essa, ma ella non istarà in piè.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 [Egli] è verdeggiante al sole, E i suoi rami si spandono fuori in sul giardino, nel quale è piantato;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Le sue radici s'intralciano presso alla fonte, Egli mira la casa di pietra.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Ma, se alcuno lo manderà in ruina, [divellendolo dal luogo suo], [Questo] lo rinnegherà dicendo: Io non ti vidi [giammai].
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ecco, tale [è] l'allegrezza della sua via, E dalla polvere ne germoglieranno altri.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Ecco, Iddio non disdegna l'[uomo] intiero; Ma altresì non presta la mano a' maligni.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Ancora empierà egli la tua bocca di riso, E le tue labbra di giubilo.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Quelli che ti odiano saranno vestiti di vergogna; Ma il tabernacolo degli empi non sarà [più].
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Giobbe 8 >