< Giobbe 13 >

1 Ecco, tutto questo ha visto il mio occhio, l'ha udito il mio orecchio e l'ha compreso.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 Quel che sapete voi, lo so anch'io; non sono da meno di voi.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 Ma io all'Onnipotente vorrei parlare, a Dio vorrei fare rimostranze.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 Voi siete raffazzonatori di menzogne, siete tutti medici da nulla.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Magari taceste del tutto! sarebbe per voi un atto di sapienza!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Ascoltate dunque la mia riprensione e alla difesa delle mie labbra fate attenzione.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Volete forse in difesa di Dio dire il falso e in suo favore parlare con inganno?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Vorreste trattarlo con parzialità e farvi difensori di Dio?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Sarebbe bene per voi se egli vi scrutasse? Come s'inganna un uomo, credete di ingannarlo?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 Severamente vi redarguirà, se in segreto gli siete parziali.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Forse la sua maestà non vi incute spavento e il terrore di lui non vi assale?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Sentenze di cenere sono i vostri moniti, difese di argilla le vostre difese.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Tacete, state lontani da me: parlerò io, mi capiti quel che capiti.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Voglio afferrare la mia carne con i denti e mettere sulle mie mani la mia vita.
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Mi uccida pure, non me ne dolgo; voglio solo difendere davanti a lui la mia condotta!
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 Questo mi sarà pegno di vittoria, perché un empio non si presenterebbe davanti a lui.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Ascoltate bene le mie parole e il mio esposto sia nei vostri orecchi.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Ecco, tutto ho preparato per il giudizio, son convinto che sarò dichiarato innocente.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Chi vuol muover causa contro di me? Perché allora tacerò, pronto a morire.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 Solo, assicurami due cose e allora non mi sottrarrò alla tua presenza;
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 allontana da me la tua mano e il tuo terrore più non mi spaventi;
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 poi interrogami pure e io risponderò oppure parlerò io e tu mi risponderai.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Quante sono le mie colpe e i miei peccati? Fammi conoscere il mio misfatto e il mio peccato.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Perché mi nascondi la tua faccia e mi consideri come un nemico?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Vuoi spaventare una foglia dispersa dal vento e dar la caccia a una paglia secca?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 Poiché scrivi contro di me sentenze amare e mi rinfacci i miei errori giovanili;
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 tu metti i miei piedi in ceppi, spii tutti i miei passi e ti segni le orme dei miei piedi.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 Intanto io mi disfò come legno tarlato o come un vestito corroso da tignola.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Giobbe 13 >