< Mazmur 7 >

1 Ratapan Daud, yang dinyanyikan bagi TUHAN karena Kus, orang Benyamin itu. Ya TUHAN Allahku, aku berlindung pada-Mu; selamatkanlah dan lepaskanlah aku dari semua orang yang mengejar aku.
Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini. Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu; pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,
2 Jangan biarkan mereka seperti singa menerkam dan menyeret aku dan tak ada pertolongan bagiku.
mwina angandikadzule ngati mkango, ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.
3 Ya TUHAN Allahku, sekiranya aku berlaku curang, berbuat jahat terhadap kawan, atau merugikan lawan tanpa alasan, sekiranya aku berbuat demikian,
Inu Yehova Mulungu wanga, ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,
4
ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere, kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,
5 biarlah aku dikejar dan ditangkap musuh, lalu dibunuh dan ditinggalkan di tanah.
pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira, lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi ndipo mundigoneke pa fumbi. (Sela)
6 Bangkitlah dalam kemarahan-Mu, ya TUHAN, lawanlah amukan musuh-musuhku. Bangkitlah untuk menolong aku, sebab Engkau menuntut keadilan.
Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu; nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga. Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.
7 Himpunlah bangsa-bangsa di sekeliling-Mu, dan berkuasalah atas mereka dari takhta-Mu di surga.
Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani. Alamulireni muli kumwambako;
8 Engkau menghakimi umat manusia; berilah aku keadilan, ya TUHAN, sebab aku tidak bersalah.
Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo. Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa, monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.
9 Hentikanlah kejahatan orang durhaka dan teguhkanlah hati orang baik, sebab Engkau Allah yang adil, yang menyelami hati dan pikiran manusia.
Inu Mulungu wolungama, amene mumasanthula maganizo ndi mitima, thetsani chiwawa cha anthu oyipa ndipo wolungama akhale motetezedwa.
10 Pelindungku ialah Allah yang menyelamatkan orang yang tulus hati.
Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba, amene amapulumutsa olungama mtima.
11 Allah adalah hakim yang adil, yang setiap saat menghukum orang jahat.
Mulungu amaweruza molungama, Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.
12 Kalau kelakuan mereka tidak berubah, Ia siap dengan senjata yang mematikan. Ia mengasah pedangnya dan merentangkan busurnya, lalu membidikkan panah-panah-Nya yang berapi.
Ngati munthu satembenuka, Mulungu adzanola lupanga lake, Iye adzawerama ndi kukoka uta.
Mulungu wakonza zida zake zoopsa; Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.
14 Lihatlah, orang jahat merencanakan kejahatan; ia membuat rencana jahat dan melakukan penipuan.
Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse. Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.
15 Ia menggali lubang untuk orang lain, tetapi ia sendiri jatuh ke dalamnya.
Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.
16 Jadi ia dihukum oleh kejahatannya sendiri, dan disiksa oleh kekerasannya sendiri.
Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini; chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.
17 Aku bersyukur kepada TUHAN sebab Ia adil, kunyanyikan pujian bagi TUHAN, Yang Mahatinggi.
Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake; ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

< Mazmur 7 >