< Mazmur 2 >

1 Mengapa bangsa-bangsa membuat huru-hara dan suku-suku bangsa merencanakan yang sia-sia?
Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu? Akonzekeranji zopanda pake anthu?
2 Raja-raja dunia bangkit serentak dan para penguasa bermufakat melawan TUHAN dan raja pilihan-Nya.
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.
3 Penguasa-penguasa itu berkata, "Mari kita patahkan kekuasaan mereka dan merebut kemerdekaan kita!"
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo ndipo titaye zingwe zawo.”
4 Dari takhta-Nya di surga TUHAN tertawa dan mencemoohkan rencana mereka.
Wokhala mmwamba akuseka; Ambuye akuwanyoza iwowo.
5 Lalu mereka dibentak-Nya dengan marah, dan dikejutkan dengan murka-Nya.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
6 Kata-Nya, "Di Sion bukit-Ku yang suci telah Kulantik raja pilihan-Ku."
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.”
7 Kata raja, "Aku mau memaklumkan apa yang telah ditetapkan TUHAN. Kata-Nya kepadaku, 'Engkau putra-Ku, hari ini Aku menjadi Bapamu.
Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula: Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga; lero Ine ndakhala Atate ako.
8 Mintalah, maka semua bangsa Kuberikan kepadamu, dan seluruh bumi Kujadikan milikmu.
Tandipempha, ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako; malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
9 Mereka akan kaupatahkan dengan tongkat besi dan kaupecahkan seperti periuk tanah.'"
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo; udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”
10 Jadi perhatikanlah, hai raja-raja, camkanlah, hai penguasa-penguasa dunia!
Kotero, inu mafumu, chenjerani; chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Berbaktilah kepada TUHAN dengan takwa,
Tumikirani Yehova mwa mantha ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 sujudlah di hadapan-Nya dengan gemetar, jangan sampai TUHAN menjadi marah dan kamu dibinasakan seketika, sebab kemarahan-Nya menyala dengan tiba-tiba. Berbahagialah orang yang berlindung pada TUHAN!
Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye; kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu, pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa. Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.

< Mazmur 2 >