< Mazmur 145 >

1 Pujian dari Daud. Aku mau mengagungkan Engkau, ya Allahku dan Rajaku, dan memuji Engkau selama-lamanya.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Setiap hari aku mau bersyukur kepada-Mu, dan memuliakan Engkau selama-lamanya.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Sebab TUHAN agung dan sangat terpuji, kebesaran-Nya tidak terselami.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Turun-temurun orang akan memuji perbuatan-Mu dan mewartakan keperkasaan-Mu.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Mereka akan memberitakan keagungan dan kemuliaan-Mu, karya-Mu yang mengagumkan akan kurenungkan.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Mereka mewartakan perbuatan-perbuatan-Mu yang dahsyat, kebesaran-Mu akan kumaklumkan.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Orang akan menceritakan segala kebaikan-Mu dan menyanyi tentang keadilan-Mu.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 TUHAN itu pengasih dan penyayang, lambat marah dan selalu mengasihi.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Ia murah hati kepada setiap orang, dan mengasihani semua ciptaan-Nya.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Semua ciptaan-Mu akan memuji Engkau, ya TUHAN, seluruh umat-Mu akan bersyukur kepada-Mu.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Mereka akan mengagungkan kuasa-Mu sebagai Raja, dan menceritakan keperkasaan-Mu,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 supaya semua orang tahu perbuatan-Mu yang besar, serta kerajaan-Mu yang mulia dan semarak.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Pemerintahan-Mu tetap sepanjang masa, kekuasaan-Mu bertahan turun-temurun. TUHAN setia kepada semua janji-Nya, Ia penuh kasih dalam segala perbuatan-Nya.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 TUHAN menolong orang yang dalam kesusahan, Ia menegakkan orang yang tertunduk.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Semua makhluk hidup mengharapkan Engkau; Kauberi mereka makan pada waktunya.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Engkau memenuhi segala keperluan mereka, sehingga mereka tidak berkekurangan.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 TUHAN adil dalam segala tindakan-Nya dan penuh kasih dalam segala perbuatan-Nya.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Ia dekat pada orang yang berseru kepada-Nya, dan memohon kepada-Nya dengan tulus hati.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Ia menyenangkan hati orang-orang yang takwa; Ia mendengar seruan mereka dan menyelamatkan mereka.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Ia melindungi setiap orang yang mencintai Dia, tetapi orang jahat dibinasakan-Nya.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Aku mau memuji TUHAN selalu, semoga semua makhluk-Nya memuji nama TUHAN untuk selama-lamanya.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.

< Mazmur 145 >