< Mazmur 135 >

1 Pujilah TUHAN! Pujilah nama TUHAN, hai kamu hamba-hamba-Nya
Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
2 yang berbakti di Rumah TUHAN di kediaman Allah kita.
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Pujilah TUHAN, sebab Ia baik, pujilah nama-Nya, sebab Ia murah hati.
Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
4 Ia memilih Yakub bagi diri-Nya, umat Israel dijadikan milik-Nya.
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
5 Sebab aku tahu TUHAN sungguh besar, Ia agung melebihi segala dewa.
Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
6 Ia melakukan apa yang dikehendaki-Nya, di langit dan di bumi, di laut dan di samudra yang dalam.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
7 Dari ujung bumi Ia mendatangkan awan, dibuat-Nya kilat untuk hujan. Lalu Ia memerintahkan angin supaya keluar dari tempat penyimpanan-Nya.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
8 Di Mesir Ia membunuh semua anak sulung dari manusia maupun binatang.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
9 Di sana dibuat-Nya banyak keajaiban dan tanda untuk menghukum raja dan semua pegawainya.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Ia membinasakan banyak bangsa, dan membunuh raja-raja perkasa:
Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihon raja Amori dan Og raja Basan, serta semua raja di Kanaan.
Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 Lalu negeri mereka diserahkan-Nya menjadi milik Israel, umat-Nya.
ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
13 Ya TUHAN, Engkau akan tetap diwartakan, dan nama-Mu diingat oleh semua keturunan,
Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 sebab Engkau memberi keadilan kepada umat-Mu, dan mengasihani hamba-hamba-Mu.
Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
15 Berhala mereka dari emas dan perak, buatan tangan manusia.
Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
16 Mereka mempunyai mulut, tetapi tak dapat berbicara, mempunyai mata, tetapi tak dapat melihat.
Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
17 Mereka mempunyai telinga, tetapi tak dapat mendengar, dari mulutnya tidak keluar napas.
makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Semoga begitulah nasib orang-orang yang membuatnya, dan yang percaya kepadanya.
Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
19 Pujilah TUHAN, hai umat Israel, pujilah Dia, hai imam-imam Allah!
Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Pujilah TUHAN, hai orang-orang Lewi, pujilah Dia, kamu semua yang takwa.
Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Pujilah TUHAN di Sion, di Yerusalem tempat kediaman-Nya. Pujilah TUHAN!
Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.

< Mazmur 135 >