< Mazmur 111 >

1 Pujilah TUHAN! Dengan segenap hati aku bersyukur kepada TUHAN di tengah himpunan umat-Nya.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Sungguh ajaib perbuatan-perbuatan TUHAN, layak diselidiki oleh orang-orang yang menyukainya.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Pekerjaan TUHAN agung dan terpuji, keadilan-Nya kekal abadi.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 TUHAN itu pengasih dan penyayang, Ia melakukan perbuatan-perbuatan yang mengagumkan, supaya kita tetap mengingatnya.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Ia memberi rezeki kepada orang yang takwa, dan selalu ingat akan perjanjian-Nya.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 Ia telah menunjukkan kuasa-Nya kepada umat-Nya, dengan memberi mereka tanah pusaka bangsa-bangsa.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 TUHAN adil dan setia dalam segala tindakan-Nya, segala perintah-Nya dapat diandalkan.
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Hukum-Nya bertahan sepanjang masa, diberikan dalam kebenaran dan keadilan.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Ia membebaskan umat-Nya, dan mengadakan perjanjian kekal dengan mereka. Dialah TUHAN yang kudus dan perkasa!
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 Barangsiapa ingin menjadi bijaksana harus menghormati TUHAN, Ia memberi pengertian kepada semua orang yang taat. Terpujilah TUHAN sepanjang masa!
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Mazmur 111 >