< Yeremia 1 >

1 Buku ini berisi kata-kata Yeremia anak Hilkia, salah seorang imam dari kota Anatot di wilayah Benyamin.
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 TUHAN berbicara kepada Yeremia pada tahun ketiga belas pemerintahan Yosia anak Amon raja Yehuda.
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 Sesudah itu TUHAN berbicara lagi kepadanya berkali-kali, mulai pada masa pemerintahan Yoyakim anak Yosia sampai pada tahun kesebelas pemerintahan Zedekia anak Yosia. Pada bulan kelima tahun itu juga penduduk Yerusalem diangkut ke pembuangan.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 TUHAN berkata kepadaku,
Yehova anayankhula nane kuti,
5 "Sebelum Aku membentuk engkau dalam rahim ibumu, dan sebelum engkau lahir, Aku sudah memilih dan mengangkat engkau untuk menjadi nabi bagi bangsa-bangsa."
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Aku menjawab, "Ya TUHAN Yang Mahatinggi, aku tidak pandai berbicara karena aku masih terlalu muda."
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Tetapi TUHAN menjawab, "Jangan katakan engkau masih terlalu muda. Kalau Aku mengutus engkau kepada siapa pun, kau harus pergi, dan semua yang Kusuruh kaukatakan, haruslah kausampaikan kepada mereka.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Jangan takut kepada mereka, sebab Aku akan menyertai engkau untuk melindungi engkau. Aku, TUHAN, telah berbicara!"
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Setelah itu TUHAN mengulurkan tangan-Nya, dan menjamah mulutku lalu berkata, "Dengarlah dan umumkanlah kata-kata yang Kuucapkan ini.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Hari ini Aku memberikan kepadamu kuasa atas bangsa-bangsa dan kerajaan-kerajaan--kuasa untuk menumbangkan dan meruntuhkan, untuk menggulingkan dan membinasakan, untuk membangun dan menanam."
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 TUHAN bertanya kepadaku, "Apa yang kaulihat, Yeremia?" Aku menjawab, "Dahan pohon badam, TUHAN."
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 "Benar," kata TUHAN, "Aku menjaga agar semua yang Kukatakan menjadi kenyataan."
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Lalu TUHAN bertanya lagi kepadaku, "Apa lagi yang kaulihat?" Aku menjawab, "Di sebelah utara kulihat periuk yang isinya sedang mendidih dan hampir terbalik ke arah sini."
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 TUHAN berkata, "Dari utara malapetaka akan meluap dan menimpa semua penduduk negeri ini.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Aku akan menyuruh semua bangsa di sebelah utara datang untuk menguasai Yerusalem. Tembok-tembok di sekeliling kota ini serta pintu-pintu gerbangnya dan semua kota di Yehuda akan mereka rebut.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Aku akan menghukum umat-Ku, karena mereka berdosa dan membelakangi Aku. Mereka telah mempersembahkan kurban kepada ilah-ilah lain, dan membuat patung-patung serta menyembahnya.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Bersiap-siaplah, Yeremia! Pergilah dan sampaikanlah kepada mereka, semua yang Kuperintahkan kepadamu. Jangan takut kepada mereka, supaya engkau jangan Kubuat lebih takut lagi kalau berhadapan dengan mereka.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Dengarkan! Engkau akan ditentang oleh penduduk negeri ini, yaitu raja-raja Yehuda, para pejabat pemerintah, para imam, dan rakyat. Tetapi hari ini Aku memberikan kepadamu kekuatan untuk melawan mereka. Engkau akan menjadi seperti kota berbenteng, seperti tiang besi dan tembok tembaga. Mereka tidak akan dapat mengalahkan engkau, sebab Aku akan menyertai dan melindungi engkau. Aku, TUHAN, telah berbicara."
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Yeremia 1 >