< Yeremia 49 >

1 Inilah yang dikatakan TUHAN mengenai Amon, "Mengapa tanah suku Gad direbut dan didiami orang-orang yang menyembah Dewa Milkom? Apakah sudah tak ada lagi orang Israel yang dapat membela daerah itu?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 Tapi akan tiba saatnya Aku membuat penduduk Raba, ibukota negeri Amon itu, mendengar pekik-pekik pertempuran. Kota itu akan menjadi reruntuhan dan desa-desa di sekitarnya terbakar habis. Lalu Israel akan mengambil kembali tanahnya dari orang-orang yang dahulu merebutnya.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 Hai orang Hesybon, menangislah sebab kota Ai sudah hancur! Hai wanita-wanita kota Raba, merataplah! Pakailah kain karung tanda sedih. Berlarilah ke sana ke mari penuh kebingungan. Milkom dewamu akan diangkut ke pembuangan bersama imam-imam dan para pejabat pemerintahnya!
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Hai kamu yang tak setia! Mengapa kamu membanggakan lembah-lembahmu yang subur? Apa sebab kamu mengandalkan kekayaanmu? Bagaimana mungkin kamu dapat berkata bahwa tak seorang pun berani menyerangmu?
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Kamu akan ditimpa kekejaman yang Kudatangkan dari segala pihak. Kamu akan lari, masing-masing berusaha menyelamatkan dirinya sendiri, dan tak ada yang mengumpulkan kamu lagi.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 Tapi di kemudian hari, keadaan bangsa Amon akan Kupulihkan. Aku, TUHAN, telah berbicara."
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Inilah yang dikatakan TUHAN Yang Mahakuasa mengenai Edom, "Apakah orang Edom tidak dapat berpikir secara bijaksana? Apakah para penasihatnya tidak memberi nasihat lagi kepada mereka? Sudah lenyapkah kebijaksanaan mereka!
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Hai penduduk Dedan, baliklah dan larilah! Pergilah bersembunyi. Aku akan menghancurkan keturunan Esau, karena sudah waktunya Aku menghukum mereka.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Kalau orang memetik buah anggur, selalu ada yang disisakannya, dan kalau pencuri datang pada malam hari, ia hanya mengambil apa yang diingininya.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Tetapi, Aku menyapu bersih milik keturunan Esau dan membuka rahasia tempat persembunyian mereka; mereka tak dapat menyembunyikan diri lagi. Orang Edom bersama saudara-saudara dan tetangga-tetangga mereka, semuanya sudah dibinasakan, tak seorang pun yang luput.
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Hai Edom! Tinggalkanlah anak-anak yatimmu kepada-Ku, Aku akan memelihara mereka. Biarlah para jandamu menaruh kepercayaannya kepada-Ku.
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Orang yang tidak patut dihukum pun, terkena hukuman juga, masakan kamu tidak? Pasti kamu harus dihukum!
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Aku bersumpah demi nama-Ku sendiri bahwa kota Bozra akan menjadi tempat yang mengerikan yang ditinggalkan orang. Orang akan menertawakannya dan memakai namanya sebagai kutukan. Semua desa di sekitarnya akan menjadi reruntuhan untuk selama-lamanya. Aku, TUHAN, telah berbicara."
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 Aku, Yeremia, berkata, "Hai Edom, aku telah menerima suatu berita dari TUHAN. Ia telah mengirim utusan kepada bangsa-bangsa untuk menyuruh mereka mengumpulkan tentara dan bersiap-siap untuk menyerang engkau.
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 TUHAN akan membuat engkau menjadi lemah dan dihina orang.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Engkau tertipu oleh keangkuhanmu. Tak ada yang takut kepadamu seperti sangkamu. Engkau tinggal di celah-celah batu, jauh di puncak gunung. Tapi, meskipun kaubuat rumahmu di tempat yang tinggi sekali, setinggi tempat sarang burung rajawali, TUHAN akan menurunkan engkau dari situ. Tuhanlah yang mengatakan semuanya itu."
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 TUHAN berkata, "Malapetaka yang menimpa Edom akan begitu hebat sehingga setiap orang yang lewat di situ akan terkejut dan takut.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Sebagaimana Sodom dan Gomora dimusnahkan bersama desa-desa di sekitarnya, begitu juga Edom. Tak seorang pun akan tinggal lagi di sana. Aku, TUHAN, telah berbicara.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 Seperti singa muncul dari hutan lebat dekat Sungai Yordan dan mendatangi padang tempat domba merumput, demikianlah Aku akan datang dan membuat orang Edom lari dari negeri mereka dengan tiba-tiba. Lalu Aku akan memilih seorang pemimpin untuk memerintah bangsa itu. Siapakah dapat disamakan dengan Aku? Siapakah berani membuat perkara dengan Aku? Apakah ada pemimpin yang dapat melawan Aku?
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Karena itu, dengarkanlah apa yang telah Kurencanakan terhadap orang Edom, dan apa yang hendak Kulakukan terhadap penduduk kota Teman. Anak-anak mereka pun akan diseret pergi, dan semua orang akan ketakutan.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Apabila Edom jatuh, akan terdengar keributan yang begitu hebat sehingga seluruh dunia goncang; teriakan-teriakan penduduknya akan terdengar sampai ke Laut Gelagah.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Seperti burung rajawali menyambar dengan sayap terkembang, begitulah musuh akan datang dan menyambar Bozra. Pada hari itu tentara Edom akan ketakutan seperti wanita yang mau melahirkan."
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Inilah yang dikatakan TUHAN tentang Damsyik. "Penduduk kota Hamat dan Arpad khawatir dan gelisah karena mendengar berita buruk. Hati mereka risau dan terombang-ambing seperti gelombang laut.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Penduduk Damsyik menjadi lemah, dan lari ketakutan. Mereka kesakitan dan menderita seperti wanita yang mau melahirkan.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Kota termasyhur dan riang gembira itu kini sepi tanpa penghuni.
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Pada hari itu pemuda-pemudanya akan tewas di jalan-jalan kotanya, dan seluruh tentaranya dihancurkan.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 Tembok-tembok Damsyik akan Kubakar, dan istana-istana Raja Benhadad Kuhanguskan. Aku, TUHAN Yang Mahakuasa, telah berbicara."
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Inilah yang dikatakan TUHAN tentang suku Kedar dan daerah-daerah kekuasaan Hazor, yang telah direbut Nebukadnezar raja Babel, "Hai Nebukadnezar, seranglah suku Kedar dan binasakanlah orang-orang di sebelah timur!
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Rampaslah ternak domba, unta, serta kemah-kemah mereka dengan segala isinya, dan berteriaklah kepada mereka, 'Teror meliputi kamu!'
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Hai kamu orang Hazor! Aku, TUHAN, berkata: Cepatlah pergi mengungsi, dan bersembunyi. Nebukadnezar raja Babel telah merencanakan untuk menyerang kamu. Ia berkata,
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 'Ayo maju! Mari kita menyerang orang-orang yang merasa aman dan tentram itu. Kota mereka tidak terlindung karena tak ada pintu gerbangnya dan tak ada palangnya.'"
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 TUHAN berkata lagi kepada Nebukadnezar, "Rampaslah unta-unta dan seluruh ternak mereka! Orang-orang yang rambutnya dipotong pendek itu akan Kuserakkan ke mana-mana. Aku akan mendatangkan malapetaka ke atas mereka dari segala pihak.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 Hazor akan terlantar untuk selama-lamanya dan menjadi tempat bersembunyi anjing hutan. Tak seorang pun akan tinggal di sana lagi. Aku, TUHAN, telah berbicara."
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 Tak lama setelah Zedekia menjadi raja Yehuda, TUHAN Yang Mahakuasa berbicara kepadaku tentang negeri Elam.
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 TUHAN berkata, "Aku akan membunuh semua ahli memanah yang membuat Elam sangat kuat.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Aku akan meniupkan angin ke Elam dari segala jurusan, dan menyerakkan penduduknya ke mana-mana sehingga tidak ada satu negeri pun yang tidak kedatangan pengungsi-pengungsi dari Elam itu.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 Aku akan membuat orang Elam takut kepada musuh yang mau membunuh mereka. Aku sangat marah kepada mereka dan akan menghancurkan mereka. Akan Kukirim tentara yang memerangi mereka sampai mereka habis sama sekali.
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Raja-raja dan pejabat-pejabat mereka akan Kuhancurkan, dan di negeri mereka akan Kudirikan takhta-Ku.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 Tapi di kemudian hari, keadaan Elam akan Kupulihkan. Aku, TUHAN, telah berbicara."
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Yeremia 49 >